Deuteronomo 18 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 18:1-22

Zopereka za kwa Ansembe ndi Alevi

1Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo. 2Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.

3Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati. 4Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu, 5pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.

6Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse, 7kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova. 8Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.

Makhalidwe Oletsedwa

9Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo. 10Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti, 11wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo. 12Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi. 13Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

Aneneri

14Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero. 15Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo. 16Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”

17Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino. 18Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula. 19Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa. 20Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”

21Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?” 22Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.

New Serbian Translation

5. Мојсијева 18:1-22

Свештенство

1Свештеници – Левити, цело Левијево племе, неће имати дела ни наследства са Израиљем. Нека живе од паљених жртава које се приносе Господу, јер је то њихов део. 2Они, дакле, неће имати наследства међу својом браћом; Господ је њихово наследство, како им је и рекао.

3Ово је право по коме свештеници имају да примају од народа – од оних који приносе на жртву било вола или овцу: плећку, вилице и желудац. То треба дати свештенику. 4Даваћеш му и првину од жита, вина и уља, као и првину од вуне својих оваца, 5јер је Господ, Бог твој, од свих племена одабрао њега и његове синове да заувек стоје и служе у име Господње.

6Ако неки Левит који живи у једном од твојих градова, било где у Израиљу, из свег срца пожели да се пресели у место које одабере Господ, 7може да служи тамо у име Господа, Бога свога, као сва његова браћа Левити, који стоје тамо пред Господом. 8Нека прима исти део као и други, без обзира на продану очевину.

Упозорење против незнабожачких обичаја

9Кад дођеш у земљу коју ти даје Господ, Бог твој, немој да се учиш да чиниш гнусна дела тих народа. 10Нека се не нађе међу тобом неко ко би свога сина или ћерку проводио кроз огањ, ко би се бавио гатањем, чарањем, тумачењем знамења, чаробњаштвом, 11нико ко би бацао врачке, призивао духове, ни видовњак, или онај што за савет пита мртве. 12Јер, Господу се гади сваки који чини ово. Због ових гнусних дела их Господ, Бог твој, тера испред тебе. 13А ти буди беспрекоран пред Господом, Богом својим. 14Наиме, ови народи које ћеш ти изгнати слушају врачаре и гатаре. Ти не чини то, јер ти то не дозвољава Господ, Бог твој.

Пророк

15Господ, Бог твој, подићи ће ти пророка међу вама, од ваше браће, као што сам ја. Њега слушајте! 16То је оно што си тражио од Господа, Бога свога, на гори Хорив на дан збора: ’Нећу више да слушам глас Господа, Бога свога, нити да гледам овај велики огањ, да не умрем!’

17Господ ми је на то рекао: ’Добро је то што су рекли. 18Зато ћу подићи пророка између твоје браће као што си ти; ја ћу ставити своје речи у његова уста, па ће говорити све што му заповедим. 19Ако неко не послуша оно што пророк буде рекао у моје име, тога ћу ја сматрати одговорним. 20А ако се неки пророк дрзне да у моје име каже нешто што нисам заповедио, или да говори у име других богова, тај пророк нека се погуби.’

21Ти се можда питаш у себи: ’Како да препознамо реч коју Господ није саопштио?’ 22Ако пророк објави нешто у име Господње, а то се не оствари, нити се испуни, то је реч коју Господ није саопштио. Пророк је то говорио из сопствене дрскости; не бој га се.