Deuteronomo 17 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 17:1-20

1Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.

2Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake, 3ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba, 4ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli, 5mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala. 6Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi. 7Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.

Mabwalo a Milandu

8Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. 9Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita. 10Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo. 11Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere. 12Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli. 13Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.

Mfumu

14Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,” 15mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli. 16Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.” 17Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.

18Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi. 19Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa. 20Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.

New Serbian Translation

5. Мојсијева 17:1-20

1Не жртвуј Господу, Богу своме, вола или јагње које има неку ману или какав други недостатак, јер је то мрско Господу, Богу твоме.

2Ако се у једном од твојих градова, које ти даје Господ, Бог твој, нађе мушкарац или жена који учини зло у очима Господа, Бога свога и крши његов савез, 3одлазећи да служи другим боговима и да им се клања, сунцу, месецу, или било чему од војске небеске, а што сам ја забранио, 4па ти то јаве или чујеш за то, ти онда добро испитај ствар. Ако се утврди да је истина да се таква мрска ствар догодила у Израиљу, 5онда тог мушкарца или жену, који је починио такво опако дело, изведи изван града, па их каменуј да умру. 6Тај човек нека се погуби на сведочење два или три сведока. На сведочење једног сведока не сме да се погуби. 7Нека прво сведоци дигну руку на њега да га погубе, а онда цели народ нека је дигне. Тако ћеш истребити зло из своје средине.

Суд

8Ако ти буде претешко да пресудиш у случају различитих врста убистава, спорења око права, повреда, или свађе у твојим градовима, ти се онда спреми и иди у место које одабере Господ, Бог твој. 9Обрати се свештеницима – Левитима и судији који буде у служби у то време. Њих питај, они ће ти рећи како ваља пресудити. 10Поступи онако како су ти рекли на месту које Господ изабере. Гледај да урадиш баш онако како те упуте. 11Поступи према упутству које су ти дали, и према пресуди коју су ти саопштили. Не одступај ни лево ни десно од онога што ти кажу. 12Ако се неко дрзне да не послуша свештеника који стоји тамо да служи Господу, Богу твоме, или судију, тај нека се погуби. Тако ћеш истребити зло из Израиља. 13Кад сав народ то чује, бојаће се, те се неће више понашати дрско.

Цар

14Кад дођеш у земљу коју ти даје Господ, Бог твој, и ти је заузмеш и настаниш се у њој, па онда кажеш: ’Поставићу цара нада мном, као што га имају сви народи око мене’, 15постави себи за цара човека кога изабере Господ, Бог твој. Себи за цара постави једног од своје браће; не смеш да поставиш странца над собом, који ти није брат. 16Само нека не држи много коња и не шаље народ у Египат да добави себи још коња, јер вам је Господ рекао: ’Никада се више не враћајте овим путем!’ 17Такође, нека не узима себи много жена, да му срце не застрани, и нека не гомила себи злата и сребра.

18А кад седне на свој царски престо, нека на свитку препише за себе овај Закон од свештеника Левита. 19Нека га држи уз себе; нека га чита целог свог живота, да научи да се боји Господа, Бога свога, држећи све речи овог Закона и вршећи све ове одредбе; 20да се не понаша надмено према својој браћи, и да не одступа ни десно ни лево од заповести, како би он и његови синови дуго владали над Израиљем.