Deuteronomo 14 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 14:1-29

Zoletsedwa pa Maliro

1Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira, 2pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.

3Musamadye chinthu chilichonse chonyansa. 4Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi, 5mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale. 6Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya. 7Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye. 8Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.

9Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba. 10Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.

11Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya. 12Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba, 13nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba, 14mtundu uliwonse wa khwangwala, 15kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi, 16kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi, 17tsekwe, vuwo, dembo, 18indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.

19Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi. 20Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.

21Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu.

Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.

Za Chakhumi

22Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse. 23Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu. 24Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri), 25ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. 26Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera. 27Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.

28Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu, 29kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.

Bibelen på hverdagsdansk

5. Mosebog 14:1-29

Om at være indviet til Herren

1I er Guds børn. Derfor må I ikke snitte jer selv til blods eller barbere ansigtshåret14,1 Ifølge Jer. 41,5 var det et tegn på sorg at snitte sig selv og barbere skægget af, muligvis også øjenbrynene. Skikken var forbundet med afgudsdyrkelse og derfor forbudt for Israels folk. Teksten her taler ikke direkte om skægget, men om håret foran på hovedet, altså på ansigtet. af for at vise jeres sorg over en, der er død, sådan som de andre folkeslag gør. 2Nej, I skal være et helligt folk, indviet til Herren alene, for han har udvalgt jer blandt alle folk på jorden til at være hans ejendomsfolk.

3I må ikke spise urene dyr, 4men I må gerne spise okser, får, geder, 5hjorte, gazeller, antiloper, rådyr, stenbukke og bjerggeder.

6Alle dyr, der tygger drøv og har spaltede klove, må I spise, 7men alle andre dyr må I ikke spise. Derfor må I ikke spise kameler, harer og klippegrævlinger, for de tygger drøv, men de har ikke spaltede klove.

8I må heller ikke spise svin, for de har spaltede klove, men de tygger ikke drøv og er derfor urene. I må ikke engang røre den slags dyr, når de er døde.

9Alle fisk med finner og skæl må I spise, 10alle andre dyr, der lever i vandet, skal I regne for urene.

11-18Alle fugle må I spise, bortset fra følgende som er urene: ørne, gribbe, fiskeørne, de forskellige falke- og høgearter, krager og ravne, strudse, måger, skarver, ibiser, rørhøns, ørkenugler, storke, de forskellige hejrearter og hærfugle.14,11-18 Betydningen af nogle af de hebraiske navne for fuglearter kendes ikke med sikkerhed. Flagermus må I heller ikke spise.

19Alle insekter med vinger er urene og må derfor ikke spises, 20men de dyr med vinger, som er rene, må I gerne spise.14,20 Ifølge 3.Mos. 11,20-23 er alle insekter urene og må ikke spises, bortset fra græshopper, der ikke regnes for insekter, men vingede væsener på linie med de småfugle, der ikke er rovdyr.

21Spis ikke selvdøde dyr, men sælg dem eventuelt til de fremmede iblandt jer, så de kan spise dem. Men I må ikke selv spise den slags, for I er et helligt folk, indviet til Herren jeres Gud.

Kog ikke et gedekid i mælk fra dets mor.

Om tiende

22Hvert år skal I give en tiendedel af jeres høst til Herren. 23Bring din tiende til det sted, som Herren vil udvælge til sin helligdom og hold festmåltid der. Det gælder tiende af korn, ny vin og olivenolie samt de førstefødte husdyr. Formålet med at give tiende er, at I derved skal lære at sætte Gud på førstepladsen i jeres liv. 24Hvis helligdommen ligger så langt borte, at det er for besværligt at bringe tienden dertil, 25kan I sælge de varer, I ellers skulle have givet i tiende, og rejse op til helligdommen med pengene 26og dér købe en okse, et får, noget vin eller øl, så I sammen med jeres husstand kan feste for Herrens ansigt. 27Glem ikke levitterne iblandt jer. Inviter dem med og del maden med dem, for de har ikke fået tildelt jord som jer andre.

28Hvert tredje år skal I samle tienden på et bestemt sted i byen 29og dele den ud mellem de jordløse levitter, de fremmede, enkerne og de forældreløse iblandt jer, så de kan komme og spise sig mætte. Da vil Herren, jeres Gud, velsigne jer i jeres arbejde.