Deuteronomo 10 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 10:1-22

Miyala Ngati Yoyamba Ija

1Pa nthawi imeneyo Yehova anati kwa ine, “Sema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija ndipo ubwere nayo kwa Ine ku phiri. Upangenso bokosi lamatabwa. 2Ndidzalembapo mawu amene anali pa miyala yoyamba ija, imene unayiphwanya. Ndipo iwe ukuyenera kuyika miyalayo mʼbokosimo.”

3Choncho ndinapanga bokosi lamatabwa amtengo wa mkesha ndi kusema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija, ndipo ndinapita ku phiri nditanyamula miyala iwiri mʼmanja mwanga. 4Yehova analemba pa miyala iwiriyo zimene analemba poyamba, Malamulo Khumi amene analengeza kwa inu pa phiri paja, mʼmoto, pa tsiku la msonkhano. Ndipo Yehova anawapereka kwa ine. 5Tsono ndinatsika ku phiri kuja ndi kuyika miyalayo mʼbokosi ndinapanga lija monga Yehova anandilamulira, ndipo panopa ili mʼmenemo.

6Aisraeli anayenda kuchokera ku Beeroti Beni Yaakani mpaka ku Mosera. Kumeneko Aaroni anamwalira nayikidwa mʼmanda, ndipo mwana wake Eliezara anakhala wansembe mʼmalo mwake. 7Kuchokera kumeneko Aisraeli anapita ku Gudigoda, napitirira mpaka ku Yotibata, ku dziko la mitsinje ya madzi. 8Pa nthawi imeneyo Yehova anapatula fuko la Levi kuti anyamule bokosi la pangano la Yehova lija, kuti ayimirire pamaso pa Yehova, kutumikira ndi kunena madalitso pa dzina lake monga amachitira mpaka lero. 9Nʼchifukwa chake Alevi alibe gawo kapena cholowa pakati pa abale awo. Yehova ndiye cholowa chawo monga momwe Yehova Mulungu wanu anawawuzira.

10Tsopano ndinakhala ku phiri kuja kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku monga ndinachitira poyamba, ndipo Yehova anandimveranso nthawi iyi. Sichinali chifuniro chake kuti akuwonongeni. 11Yehova anati kwa ine, “Pita ndi kutsogolera anthuwa pa njira yawo, kuti alowe ndi kulandira dziko limene ndinalumbira kwa makolo awo kuti ndiwapatse.”

Kuopa Yehova

12Tsopano inu Aisraeli, nʼchiyani chimene Yehova afuna kwa inu? Iye akufuna kuti muzimuopa poyenda mʼnjira zake zonse ndi kumamukonda Iye, kumutumikira Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, 13ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene ndikukupatsani lero kuti zizikuyenderani bwino.

14Yehova Mulungu wanu ndiye mwini wake kumwamba ngakhale mmwambamwamba, dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo. 15Yehova anayika mtima wake pa makolo anu okha ndipo anawakondadi nasankha adzukulu awo mwa mitundu yonse pa dziko lapansi, kunena inuyo monga mulili lero. 16Motero chitani mdulidwe wa mitima yanu ndipo musakhalenso opulupudza. 17Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa milungu, Ambuye wa ambuye, Mulungu wamkulu, wamphamvu ndi woopsa, amene sakondera ndipo salandira ziphuphu. 18Iye amatchinjiriza ana amasiye ndi akazi amasiye, ndipo amakonda mlendo namupatsa chakudya ndi chovala. 19Muzikonda alendo popeza inuyo munali alendo mʼdziko la Igupto. 20Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye. Mumukakamire Iyeyo ndi kuchita malumbiro anu mʼdzina lake. 21Iye ndiye matamando anu, Mulungu wanu amene anakuchitirani zodabwitsa zazikulu ndi zoopsa zimene munaona ndi maso anu zija. 22Makolo anu amene anapita ku Igupto analipo makumi asanu ndi awiri onse pamodzi, ndipo tsopano Yehova Mulungu wanu wakuchulukitsani ngati nyenyezi zakumwamba.

New Serbian Translation

5. Мојсијева 10:1-22

Нове плоче

1У то време ми је Господ рекао: ’Исклеши себи две камене плоче као што су биле оне прве, па се попни к мени на гору; направи и дрвени Ковчег. 2Ја ћу, онда, написати на плочама речи које су биле написане на првим плочама које си разбио. Стави их у Ковчег.’

3Тако сам направио Ковчег од багремовог дрвета, исклесао две камене плоче, као што су биле оне прве, па сам се попео на гору са две камене плоче у рукама. 4Бог је написао на плочама оно што је написао први пут; десет заповести које вам је Господ саопштио на гори из огња на дан збора, и предао ми их. 5Затим сам се окренуо и сишао с горе. Плоче сам ставио у Ковчег који сам направио, као што ми је Господ заповедио, и тамо су још увек.

6(Из Вирота који припада Јаканцима, Израиљци су наставили према Мосери. Тамо је Арон умро и био сахрањен. На његово место су поставили за свештеника његовог сина, Елеазара. 7Одатле су наставили за Гудгод, а из Гудгода за Јотвату, у земљу многих потока. 8У то време је Господ издвојио Левијево племе да носи Ковчег савеза Господњег, да стоји пред Господом, да му служи и да благосиља у његово име, као што је то данас. 9Зато Леви нема свој део баштине са његовом браћом. Сам Господ је његова баштина, баш као што му је рекао Господ, Бог твој.)

10Ја сам остао на гори четрдесет дана и четрдесет ноћи, као први пут. Господ ме је послушао и овај пут, те није хтео да те уништи. 11Господ ми рече: ’Спреми се и крени на пут на челу народа, да оду и освоје земљу за коју сам се заклео да ћу је дати њиховим оцима.’

Бој се Господа

12А сад, Израиљу, шта то Господ, Бог твој, тражи од тебе? Само то да се бојиш Господа, Бога свога, да следиш све његове путеве, да га волиш; да служиш Господу, Богу своме, свим срцем својим и свом душом својом, 13и да држиш заповести и уредбе Господње, које ти данас налажем, за твоје добро.

14Гле, Господу, Богу твоме, припада небо, и небо над небесима, те земља и све што је на њој. 15Једино су твоји оци прионули Господу за срце; он их је заволео и изабрао њихово потомство после њих између свих народа, као што је то данас. 16Зато обрежите своје срце и не укрућујте више вратове. 17Јер, Господ, Бог ваш, је Бог над боговима и Господар над господарима, Бог велики, моћни и страшни, који није пристрасан, ни подмитљив. 18Он додељује правду сиромаху и удовици; воли странца и даје му храну и одећу. 19Зато волите странца, јер сте и сами били странци у Египту. 20Бојте се Господа, Бога свога, њему служите и његовим се именом куните. 21Он је твоја слава и Бог твој, који је учинио за тебе ова велика и страшна дела која си својим очима видео. 22Јер, твоји преци одоше у Египат са седамдесет душа, а сада вас је Господ, Бог твој, размножио као звезде на небу.