Deuteronomo 11 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 11:1-32

Kukonda ndi Kumvera Yehova

1Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake. 2Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka; 3zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse; 4zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero. 5Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu, 6ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo. 7Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.

8Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani, 9ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi. 10Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba. 11Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba. 12Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.

13Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, 14pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta. 15Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.

16Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira. 17Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani. 18Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu. 19Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka. 20Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu, 21kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.

22Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye 23Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu. 24Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo. 25Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.

26Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu, 27dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero. 28Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe. 29Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala. 30Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala. 31Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo, 32mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.

New Serbian Translation

5. Мојсијева 11:1-32

Награда за послушност

1Зато воли Господа, Бога свога, и увек држи његове наредбе, прописе, уредбе и заповести. 2Знајте данас, да ваши синови нису ти што су искусили карање Господа, Бога вашег, и видели његово величанство, његову моћну руку и испружену мишицу, 3знакове и његова дела која је учинио усред Египта против фараона, цара египатскога, и свег његовог народа; 4шта је учинио са египатском војском, њиховим коњима и бојним колима, како их је подавио у водама Црвеног мора, док су вам били за петама, и како их је затро Господ до данашњега дана. 5Они нису видели шта је учинио за вас у пустињи док нисте дошли на ово место; 6шта је учинио Датану и Авирону, синовима Елијава, потомка Рувимовог, кад се отворила земља усред Израиља и прогутала и њих и њихове домове, њихове шаторе и сву њихову имовину.

7Не, то су ваше очи виделе сва велика дела која је Господ учинио. 8Зато држите све заповести које вам данас налажем, да будете јаки, да уђете и освојите земљу у коју идете да је заузмете, 9те да дуго проживите на земљи за коју се Господ заклео вашим оцима да ће је дати вама и вашем потомству – земљу којом теку млеко и мед. 10Јер, земља у коју улазиш да је заузмеш није као египатска земља из које си изашао, где си сејао своје семе и наводњавао га својом ногом, као што се наводњава повртњак. 11Земља у коју улазите да је заузмете земља је брда и долина која се наводњава кишом са неба. 12То је земља о којој се сам Господ, Бог твој, стара; земља над којом очи Господа, Бога твог, стално бдију, од почетка до краја године.

13Ако послушате заповести које вам данас заповедам, и будете волели Господа, Бога свога, и служили му свим својим срцем и свом својом душом, 14он ће давати рану и позну кишу вашој земљи у право време, па ћете сабирати своје жито, своје вино и своје уље; 15даваће вам траву на вашем пољу за вашу стоку, те ћете јести и наситити се.

16Пазите да се не преварите у своме срцу, па застраните служећи и клањајући се другим боговима. 17Тада ће гнев Господњи планути против вас: небеса ће се затворити и неће давати кишу, земља неће давати свој род, а ви ћете брзо нестати са добре земље коју вам Господ даје. 18Зато усадите ове моје речи у срце своје и у душу своју; привежите их као знак на своју руку; нека вам буду као запис међу очима. 19Поучите њима своју децу; говорите им о њима; кад седиш у кући, кад идеш путем, кад лежиш и кад устајеш. 20Напиши их на доврацима своје куће и на твојим вратима, 21да би ти се умножили дани и дани твоје деце на земљи за коју се Господ заклео твојим оцима да ће им је дати, докле год буде неба над земљом.

22Ако будете предано држали ове заповести које вам заповедам да вршите, волели Господа, Бога свога, следили све његове путеве и чврсто се држали уз њега, 23Господ ће потерати све ове народе испред вас, па ћете развластити народе који су већи и бројнији од вас. 24Свако место где буде ступила ваша нога, биће ваше; ваша граница ће се протезати од пустиње до Ливана и од реке Еуфрата до Западног мора11,24 Средоземно море.. 25Нико неће моћи да вам се одупре, јер ће Господ, Бог ваш, улити страх и трепет по целој земљи у коју ступите, баш као што вам је рекао.

Благослов или проклетство

26Види! Постављам данас пред вас благослов и проклетство: 27благослов ако послушате заповести Господа, Бога свога, које вам ја данас налажем, 28а проклетство ако не послушате заповести Господа, Бога свога, те скренете са пута на који вас ја данас упућујем и кренете за другим боговима које нисте познавали. 29А када те Господ, Бог твој, уведе у земљу у коју идеш да је заузмеш, постави благослов на гору Геризим, а проклетство на гору Евал. 30Нису ли те горе с друге стране Јордана, на путу што води на запад, у земљи Хананаца који живе у Арави, насупрот Галгалу, близу храста Море? 31Јер ви сад прелазите преко Јордана да уђете и заузмете земљу коју вам даје Господ, Бог ваш. Ви ћете је заузети и живети у њој. 32Зато држи и врши прописе и уредбе које данас постављам пред вас.