Chivumbulutso 1 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 1:1-20

Mawu Oyamba

1Vumbulutso lochokera kwa Yesu Khristu, limene Mulungu anamupatsa kuti aonetse atumiki ake zimene zinayenera kuchitika posachedwa. Iye anatuma mngelo wake kuti adziwitse mtumiki wake Yohane, 2amene akuchitira umboni chilichonse chimene anachiona. Awa ndi Mawu a Mulungu ndi umboni wa Yesu Khristu. 3Ngodala munthu amene awerenga mawu oneneratu zamʼtsogolo ndi iwo amene amamva ndi kusunga zolembedwa mʼbukuli pakuti nthawi yayandikira.

Malonje kwa Mipingo Isanu ndi Iwiri

4Ndine Yohane,

Kupita ku mipingo isanu ndi iwiri ya mʼchigawo cha Asiya.

Chisomo ndi mtendere kwa inu, kuchokera kwa Iye amene ali, amene analipo ndi amene akubwera ndi kwa mizimu isanu ndi iwiri yokhala patsogolo pa mpando wake waufumu, 5ndiponso kuchokera kwa Yesu Khristu mboni yokhulupirika, woyamba kuukitsidwa, ndi wolamulira mafumu a dziko lapansi.

Kwa Iye amene amatikonda ndipo watimasula ku machimo athu ndi magazi ake, 6ndipo watisandutsa mafumu ndi ansembe kuti tizitumikira Mulungu ndi Atate ake. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu ku nthawi zosatha, Ameni.

7“Onani akubwera ndi mitambo,”

ndipo “Aliyense adzamuona,

ndi amene anamubaya omwe.”

Ndipo anthu a mitundu yonse ya pa dziko lapansi “adzalira chingʼangʼadza chifukwa cha Iye.”

Zidzakhaladi momwemo, Ameni.

8“Ine ndine Alefa ndi Omega,” akutero Ambuye Mulungu Wamphamvuzonseyo “amene muli, amene munalipo, ndi amene mudzakhalapo.”

Wina Wokhala ngati Mwana wa Munthu

9Ine Yohane mʼbale wanu ndi mnzanu mʼmasautso ndi mu ufumu ndi mukupirira kwambiri, zomwe ndi zathu mwa Yesu, ndinali pa chilumba cha Patimo chifukwa cha Mawu a Mulungu ndi umboni wa Yesu. 10Pa tsiku la Ambuye ndinanyamulidwa ndi Mzimu ndipo ndinamva kumbuyo kwanga mawu ofuwula ngati lipenga, 11amene anati, “Lemba mʼbuku zimene ukuziona ndipo uzitumize ku mipingo isanu ndi iwiri ya ku Efeso, Simurna, Pergamo, Tiyatira, Sarde, Filadefiya ndi ku Laodikaya.”

12Nditatembenuka kuti ndione amene amandiyankhulayo, ndinaona zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide. 13Pakati pa zoyikapo nyalezo ndinaona wina wooneka ngati Mwana wa Munthu atavala mkanjo wofika kumapazi ake ndipo anamangirira lamba wagolide pa chifuwa pake. 14Tsitsi lake linali loyera ngati thonje, kuyera ngati matalala, ndipo maso ake amawala ngati malawi amoto. 15Mapazi ake anali ngati chitsulo choti chili mʼngʼanjo yamoto, ndipo mawu ake anali ngati mkokomo wamadzi othamanga. 16Mʼdzanja lake lamanja ananyamula nyenyezi zisanu ndi ziwiri, ndipo mʼkamwa mwake munali lupanga lakuthwa konsekonse. Nkhope yake imawala ngati dzuwa lowala kwambiri.

17Nditamuona ndinagwa pa mapazi ake ngati wakufa. Kenaka Iye anasanjika dzanja lake lamanja pa ine nati, “Usachite mantha. Ndine Woyamba ndi Wotsiriza. 18Ine ndine Wamoyo; ndinali wakufa ndipo taona ndine wamoyo mpaka muyaya! Ndipo ndili ndi makiyi a imfa ndi Hade.

19“Chomwecho, lemba zimene waona, zimene zilipo panopa ndi zimene zidzachitike mʼtsogolo. 20Tanthauzo la nyenyezi zisanu ndi ziwiri zimene waziona mʼdzanja langa lamanja ndi la zoyikapo nyale zagolide zisanu ndi ziwiri ndi ili: Nyenyezi zisanu ndi ziwiri ndi angelo a mipingo isanu ndi iwiri ija, ndipo zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zija ndi mipingo isanu ndi iwiri ija.”

Knijga O Kristu

Otkrivenje 1:1-20

Uvod

1Ovo je otkrivenje Isusa Krista, koje mu je Bog dao da pokaže svojim slugama što se ima uskoro dogoditi. Bog je poslao anđela svojemu sluzi Ivanu da bi mogao otkrivenje prenijeti drugima. 2Ivan izvješćuje o Božjoj riječi i svjedočanstvu Isusa Krista—o svemu što je vidio.

3Blago onome koji čita ovo proroštvo i onima koji slušaju njegove riječi te vrše što je u njemu napisano. Jer vrijeme kad će se ono ispuniti je blizu.

Ivan pozdravlja sedam crkava

4Ovo pismo piše Ivan sedmerim crkvama u Maloj Aziji. Neka vam je milost i mir od onoga koji jest, koji je oduvijek bio i koji će doći; od sedam duhova pred njegovim prijestoljem 5te od Isusa Krista koji vjerno svjedoči o tomu, koji je prvi ustao od mrtvih i vladar je nad svim zemaljskim kraljevima.

Neka je slava njemu koji nas ljubi i koji nas je oslobodio od grijeha prolivši za nas svoju krv. 6Učinio nas je kraljevstvom i svećenstvom Boga, svojega Oca. Neka mu je slava i vlast uvijeke! On vlada zauvijek. Amen.

7Gle! On dolazi s oblacima nebeskim. I vidjet će ga svi, čak i oni koji su ga proboli. Svi će narodi na zemlji proplakati zbog njega. Da. Amen.

8“Ja sam Alfa i Omega, Početak i Svršetak”, kaže Gospodin Bog. “Ja sam Svemogući, onaj koji jest, koji je oduvijek bio i koji će doći.”

Viđenje Sina Čovječjega

9Ja, Ivan, vaš brat, kao i vi u Kristu sam dionik patnji i kraljevstva te postojanosti. Izgnan sam na otok Patmos zbog propovijedanja Božje riječi i svjedočenja o Isusu. 10Bio je Dan Gospodnji. Ponio me Duh i odjednom sam iza sebe začuo glas snažan poput zvuka trublje. 11“Zapiši što ti kažem”, reče mi glas, “i pošalji sedmerim crkvama: u Efez, Smirnu, Pergam, Tijatiru, Sard, Filadelfiju i Laodiceju.”

12Okrenem se da vidim tko mi govori, ali ugledam sedam zlatnih svijećnjaka, 13a među svijećnjacima nekoga sličnog čovjeku.1:13 U grčkome: sličnoga sinu čovječjemu. Ne odnosi se na Isusa Krista, već znači sličan ljudskome biću, čovjeku. Bio je odjeven u dugu haljinu, sa zlatnim pasom oko prsa. 14Kosa mu je bila bijela poput bijele vune, poput snijega, oči kao ognjeni plamen, 15noge sjajne poput mjedi u peći užarene, a glas poput šuma golemih morskih valova. 16U desnoj je ruci držao sedam zvijezda, a u ustima oštar dvosjekli mač. Lice mu je blistalo poput sunca u punome sjaju.

17Kad sam ga opazio, pao sam do njegovih nogu kao mrtav. Ali on stavi na mene desnu ruku i reče mi: “Ne boj se! Ja sam Prvi i Posljednji. 18Živ sam! Bio sam mrtav, ali živim zauvijek. Imam ključeve smrti i podzemlja. 19Zapiši što si vidio: što se sada događa i što će se dogoditi poslije. 20Evo što znače sedam zvijezda koje si vidio u mojoj desnoj ruci i sedam zlatnih svijećnjaka: sedam su zvijezda anđeli1:20 Ili: glasnici. sedam crkava, a sedam svijećnjaka sedam crkava.