Chivumbulutso 2 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 2:1-29

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Efeso

1“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Efeso kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri zija mʼdzanja lake lamanja amene akuyenda pakati pa zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide. 2Ine ndimadziwa zochita zako, ntchito yako yowawa ndi kupirira kwako. Ine ndimadziwa kuti sungalekerere anthu oyipa amene amadzitcha atumwi pamene sichoncho, unawayesa, ndipo unawapeza kuti ndi abodza. 3Iwe wapirira ndipo wakumana ndi zovuta chifukwa cha dzina langa, ndipo sunatope.

4Komabe ndili ndi chotsutsana nawe: Wataya chikondi chako chapoyamba. 5Kumbukirani kuti munagwa kuchokera patali. Lapa ndikuchita zinthu zimene unkachita poyamba. Ngati sulapa ndidzabwera ndikukuchotsera choyikapo nyale chako pamalo pake. 6Komabe chokomera chako ndi chakuti umadana ndi zochita za Anikolai, zimene Inenso ndimadana nazo.

7Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wakudya zipatso za mtengo wopatsa moyo umene uli ku paradizo wa Mulungu.

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Simurna

8“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Simurna kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi Woyamba ndi Wotsiriza, amene anafa nʼkukhalanso ndi moyo. 9Ine ndimadziwa masautso ako ndi umphawi wako, chonsecho ndiwe wolemera! Ndikudziwa zimene amakusinjirira anthu amene amati ndi Ayuda pamene sizili choncho, koma ndi a mpingo wa Satana. 10Musachite mantha ndi zimene muti musauke nazo posachedwapa. Ndithu, Satana adzayika ena a inu mʼndende pofuna kukuyesani, ndipo mudzazunzika kwa masiku khumi. Khalani okhulupirika ngakhale zitafika pa imfa, ndipo Ine ndidzakupatsani chipewa cha ulemerero wamoyo.

11Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana sadzapwetekedwa ndi pangʼono pomwe ndi imfa yachiwiri.

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Pergamo

12“Lembera mngelo wa mpingo wa ku Pergamo kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi lupanga lakuthwa konsekonse. 13Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa kumene mumakhala, kumene kuli mpando waufumu wa Satana. Komabe inu ndinu okhulupirika kwa Ine. Simunataye chikhulupiriro chanu pa Ine, ngakhale mʼmasiku a Antipa, mboni yanga yokhulupirika, amene anaphedwa mu mzinda wanu, kumene amakhala Satana.

14Komabe, ndili ndi zinthu zingapo zotsutsana nanu. Kumeneko muli ndi anthu ena amene amatsata ziphunzitso za Balaamu, uja amene anaphunzitsa Baraki kukopa Aisraeli kuti azidya nsembe zoperekedwa ku mafano ndi kumachita chigololo. 15Chimodzimodzinso inuyo muli ndi ena amene amatsatira ziphunzitso za Anikolai. 16Tsono tembenukani mtima. Mukapanda kutero, ndidzabwera kwanuko posachedwa ndipo ndidzachita nanu nkhondo ndi lupanga lotuluka mʼkamwa mwanga lija.

17Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Kwa amene adzapambane ndidzamupatsa chakudya chobisika cha mana. Ndidzamupatsanso mwala woyera wolembedwapo dzina latsopano, lodziwa iye yekha amene walandirayo.’ ”

Kalata Yolembera Mpingo wa ku Tiyatira

18“Lembera mngelo wampingo wa ku Tiyatira kuti:

Awa ndi mawu ochokera kwa Mwana wa Mulungu, amene maso ake ali ngati moto woyaka ndi mapazi ake ngati chitsulo chonyezimira. 19Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zanu, chikondi chanu ndi chikhulupiriro chanu, kutumikira kwanu ndi kupirira kwanu. Ndikudziwa tsopano kuti ntchito zanu ndi zabwino kuposa zoyamba zija.

20Komabe ndili ndi chinthu chokudzudzula nacho. Umamulekerera mkazi uja Yezebeli amene amadzitcha yekha kuti ndi mneneri. Iye amaphunzitsa atumiki anga kuti azichita zadama ndi kumadya zansembe zoperekedwa ku mafano. 21Ndamupatsa nthawi kuti aleke zachigololo zake koma sakufuna. 22Tsono ndidzamugwetsa mʼmasautso ndipo amene amachita naye zadama zakezo ndidzawasautsa kwambiri akapanda kulapa ndi kuleka njira za mkaziyo. 23Ana ake ndidzawakantha ndi kuwapheratu. Kotero mipingo yonse idzadziwa kuti Ine ndine uja amene ndimafufuza mʼmitima mwa anthu ndi mʼmaganizo mwawo. Aliyense wa inu ndidzachita naye monga mwa ntchito zake.

24Tsopano ndikunena kwa enanu a ku Tiyatira, kwa inu amene simunatsate chiphunzitso cha mkaziyo ndipo simunaphunzire zimene iwo amati ndi ‘zinsinsi zonama’ za Satana. Kwa inu mawu anga ndi akuti sindikuwunjikirani malamulo ena. 25Inu mungogwiritsa zimene munaphunzira basi, mpaka Ine ndidzabwere.

26Amene adzapambana ndi kuchita chifuniro changa mpaka kumapeto, ndidzamupatsa ulamuliro pa mitundu yonse ya anthu. 27Adzayilamulira ndi ndodo yachitsulo ndipo nadzayiphwanyaphwanya ngati mbiya. Ulamuliro umenewu ndi omwe ndinalandira kwa Atate anga. 28Ine ndidzamupatsanso nthanda, nyenyezi yowala mʼmamawa ija. 29Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.

Knijga O Kristu

Otkrivenje 2:1-29

Poruka Crkvi u Efezu

1Anđelu2:1 Ili: glasniku. Crkve u Efezu napiši:

‘Ovo govori Onaj koji drži sedam zvijezda u desnici, Onaj koji hodi između sedam zlatnih svijećnjaka: 2Znam za tvoja dobra djela. Vidio sam tvoj trud i postojanost. Ne podnosiš opake. Iskušao si one koji tvrde da su apostoli, a nisu, i otkrio da su lažljivci. 3Strpljivo si za mene trpio i nisi posustao.

4Ali imam i prigovor na tebe. Napustio si prvu ljubav: ne voliš me i ne volite se međusobno žarko kao u početku! 5Prisjeti se dakle kako si volio u početku i pogledaj na što si spao! Obrati se ponovno k meni i čini opet kao u početku. Ne učiniš li to, doći ću i ukloniti tvoj svijećnjak s njegova mjesta među crkvama. 6Ali dobro je što mrziš djela pokvarenih nikolaita jednako kao i ja.

7Slušajte, kad već imate uši, što Duh govori crkvama! Svakome tko pobijedi dat ću da jede sa stabla života u Božjemu raju.’

Poruka Crkvi u Smirni

8Anđelu Crkve u Smirni napiši:

‘Ovo govori Prvi i Posljednji, koji je bio mrtav i oživio: 9Znam za tvoje patnje i tvoje siromaštvo—ali bogat si! Trpiš pogrde od onih koji sebe nazivaju Židovima, ali to nisu. Sotonina su sinagoga! 10Ne boj se onoga što ćete pretrpjeti. Đavao će neke od vas baciti u tamnici da vas iskuša. Trpjet ćete nevolju deset dana. Ostanite vjerni i kad se suočite sa smrću pa ću vam dati vijenac života.

11Slušajte, kad već imate uši, što Duh govori crkvama! Nikome tko pobijedi neće nauditi druga smrt!’

Poruka Crkvi u Pergamu

12Anđelu Crkve u Pergamu napiši:

‘Ovo je poruka od onoga koji ima oštar dvosjekli mač: 13Znam da živiš u gradu u kojemu je Sotonino prijestolje, a ipak si ostao vjeran mojemu imenu. Nisi zanijekao vjeru u mene ni onda kad su kod vas, gdje Sotona prebiva, ubili mojega vjernog svjedoka Antipu.

14Ali imam ti ponešto prigovoriti. Trpiš ondje neke ljude nalik Bileamu, koji je poučio Balaka da izraelskome narodu postavi stupicu pa ih je naučio da blaguju meso žrtvovano idolima i odaju se bludu. 15Tako i ti u svojoj sredini imaš takvih koji slijede nikolaitsko učenje i počinjaju iste grijehe. 16Obrati se zato ili ću ubrzo doći k tebi i boriti se protiv njih mačem svojih usta.

17Slušajte, kad već imate uši, što Duh govori crkvama! Svaki koji pobijedi jest će manu skrivenu i dat ću mu bijel kamen na kojemu će pisati njegovo novo ime, koje ne zna nitko osim onoga koji ga prima.’

Poruka Crkvi u Tijatiri

18Anđelu Crkve u Tijatiri napiši:

‘Ovo govori Božji Sin, čije su oči poput ognjenog plamena a noge poput ulaštene mjedi: 19Znam za tvoja dobra djela, za tvoju ljubav i vjeru, služenje i postojanost. Znam i da si u tomu sve revniji.

20Ali imam i prigovor na tebe: dopuštaš onoj ženi Jezabeli, koja sebe naziva proročicom, da moje sluge odvlači na stranputicu te se odaju bludu, štuju idole i jedu meso njima žrtvovano. 21Dao sam joj vremena da se pokaje i obrati od svojega bluda, ali nije htjela. 22Bacit ću je zato na postelju, a i svi koji s njome bludno griješe mnogo će trpjeti ne odvrate li se od zlih djela. 23I djeca će joj umrijeti. Sve će crkve znati da sam ja onaj koji ispituje misli i nakane2:23 U grčkome: bubrege i srca. svakoga čovjeka. Svakome ću dati što zaslužuje.

24A od vas ostalih u Tijatiri, koji ne slijedite to lažno učenje (“duboke istine”, kako nazivaju te sotonske dubine), tražim samo 25da se čvrsto držite onoga što znate dok ne dođem.

26Svakome tko pobijedi, tko do konca bude vršio što mu kažem, dat ću vlast nad narodima. 27Vladat će nad njima željeznom palicom i razbijati ih kao glineno posuđe 28istom vlašću koju je meni dao moj Otac. Dat ću im i zvijezdu Danicu.

29Slušajte, kad već imate uši, što Duh govori crkvama!’