Aroma 11 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 11:1-36

Aisraeli Otsala

1Ine ndikufunsa kuti kodi Mulungu anakana anthu ake? Ayi. Ndi pangʼono pomwe! Inenso ndine Mwisraeli, mmodzi mwa zidzukulu za Abrahamu, ndiponso wa fuko la Benjamini. 2Mulungu sanawakane anthu ake amene Iye anawadziwiratu. Kodi inu simukudziwa zimene Malemba akunena pa ndime imene Eliya akudandaula kwa Mulungu kuneneza Aisraeli? Iye anati, 3“Ambuye, anthuwa apha aneneri anu ndi kugwetsa maguwa anu ansembe. Ndatsala ine ndekha wamoyo ndipo akufuna kundipha?” 4Ndipo yankho la Mulungu linali lotani? “Ine ndadzisungira ndekha anthu 7,000 amene sanapembedzepo Baala.” 5Chimodzimodzinso lero lino, alipo Aisraeli pangʼono osankhidwa mwachisomo. 6Ndipo ngati ndi mwachisomo, sikungakhalenso mwa ntchito. Ngati zikanatero, chisomo sichikanakhalanso chisomo ayi.

7Nʼchiyani tsopano? Chimene Aisraeli anachifuna ndi mtima wonse sanachipeze koma osankhidwawo anachipeza. Enawo anawumitsidwa mtima 8monga kwalembedwa kuti,

“Mulungu anawapatsa mzimu wosatha kumvetsa zinthu,

maso osatha kupenya;

makutu osatha kumva

mpaka lero lino.”

9Ndipo Davide akuti,

“Maphwando awo asanduke msampha ndi diwa lowakola

ndi chopunthwitsa kuti alandire chilango.

10Maso awo atsekedwe kuti asaone,

ndi misana yawo ikhale yokhota nthawi zonse.”

Nthambi Zomangiriridwa

11Ine ndikufunsanso kuti, kodi iwo anapunthwa ndi kugwa kotheratu? Ayi. Ndi pangʼono pomwe! Koma chifukwa cha kulakwa kwawo, chipulumutso chinafika kwa a mitundu ina kuti Aisraeli achite nsanje. 12Koma ngati kulakwa kwawo kwapindulitsa dziko lapansi ndi kulephera kwawo kwapindulitsa a mitundu ina, nanga kudzakhala kupindula kwakukulu chotani iwo akadzabwera chonse!

13Ine ndikuyankhula kwa inu a mitundu ina monga ine ndili mtumwi wa kwa a mitundu ina ndipo ndimawunyadira utumiki wangawu. 14Ine cholinga changa nʼchakuti ndichititse nsanje anthu a mtundu wanga kuti ena mwa iwo apulumutsidwe. 15Pakuti ngati kukanidwa kwawo kunayanjanitsa anthu a dziko lapansi ndi Mulungu, nanga kudzatani, Iye akadzawalandiranso? Kudzakhala monga ngati anthu akufa akuuka. 16Ngati chigawo chimodzi cha buledi woperekedwa monga zipatso zoyamba ndi choyera, ndiye kuti zonsezo ndi zoyera. Ngati muzu ndi oyera, nʼchimodzimodzinso nthambi zake.

17Ngati nthambi zina zinakhadzulidwa ndipo inu, inu ndiye nthambi za olivi wakuthengo, nʼkulumikizidwa pamalo pa nthambi zimenezo, ndipo tsopano mukulandira nawo zakudya zochokera ku mizu ya olivi, 18musadzitame kunyoza nthambi zinazo. Ngati mutero, ganizirani ichi kuti Inu simugwiriziza mizu, koma muzu ukugwiriziza inu. 19Tsono mudzati, “Nthambizo zinakhadzulidwa kuti ine ndilumikizidwepo.” 20Nʼzoona. Koma iwo anakhadzulidwa chifukwa chosakhulupirira ndipo inu mukuyima mwachikhulupiriro. Musadzitukumule, koma muchite mantha. 21Pakuti ngati Mulungu sanalekerere nthambi zachibadwidwe, Iye sadzakulekererani inunso.

22Nʼchifukwa chake ganizirani za kukoma mtima ndi za ukali wa Mulungu. Ukali uli kwa iwo amene anagwa koma kukoma mtima kwa inu, malinga ngati musamala kukoma mtima kwakeko kupanda kutero inunso mudzakhadzulidwanso. 23Ngati iwo asiya kukhala osakhulupirira, adzalumikizidwanso pakuti Mulungu akhoza kuwalumikizanso. 24Pakuti ngati inu, mwa chilengedwe munali mtengo wa olivi wa kuthengo, Mulungu anakukhadzulani nakulumikizani ku mtengo wa olivi wodzalidwa, zomwe ndi zotsutsana ndi chilengedwe, kodi sikudzakhala kwapafupi kwa Iye kuwalumikizanso mu mtengo wawowawo wa olivi?

Aisraeli Onse Adzapulumuka

25Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa za chinsinsi ichi, kuti mungadziyese nokha anzeru. Kuwuma mtima kumene Aisraeli akuchita ndi kwa kanthawi kufikira chiwerengero cha a mitundu chitalowa. 26Kotero tsono Aisraeli onse adzapulumuka, monga kwalembedwa kuti,

“Mpulumutsi adzachokera ku Ziyoni;

Iye adzachotsa zoyipa zonse za Yakobo.

27Ndipo ili lidzakhala pangano langa ndi iwo

pamene Ine ndidzachotsa machimo awo.”

28Chifukwa cha Uthenga Wabwino, Aisraeli asanduka adani a Mulungu kuti inu mupindule. Koma kunena za kusankhidwa, iwo ndi okondedwa ndi Mulungu chifukwa cha makolo awo aja. 29Pakuti Mulungu akayitana munthu ndi kumupatsa mphatso sangasinthenso. 30Monga mmene inu munalili, osamvera Mulungu pa nthawi ina, tsopano mwalandira chifundo chifukwa cha kusamvera kwawo. 31Chonchonso iwo akhala osamvera tsopano kuti iwonso alandire chifundo chifukwa cha chifundo cha Mulungu kwa inu. 32Pakuti Mulungu anasandutsa anthu onse a mʼndende ya kusamvera kuti Iye akaonetse chifundo kwa onse.

Kulemekeza Mulungu

33Aa! Nzeru za Mulungu ndi chidziwitso chake ndi zozama kwambiri!

Ndani angazindikire maweruzidwe ake,

ndipo njira zake angazitulukire ndani?

34“Kodi wadziwa ndani maganizo a Ambuye?

Kapena ndani anakhalapo mlangizi wake?”

35“Kodi ndani anapereka mphatso kwa Mulungu,

kuti Mulunguyo amubwezere iye?”

36Pakuti zinthu zonse nʼzochokera kwa Iye, nʼzolengedwa ndi Iye ndipo zimabweretsa ulemerero kwa Iye.

Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya! Ameni.

New Serbian Translation

Римљанима 11:1-36

Бог је милостив према Израиљу

1Питам дакле: да Бог можда није одбацио свој народ? Никако! Јер и ја сам Израиљац, потомак Аврахамов, из племена Венијаминовог. 2Није Бог одбацио свој народ, који је предвидео. Или, зар не знате шта пише у Писму о Илији – кад се жали Богу на Израиљце?

3„Господе, побили су твоје пророке,

срушили су твоје жртвенике,

а ја сам остао сам,

па и мене настоје да убију.“

4Међутим, шта му Бог одговара?

„Оставио сам себи седам хиљада људи,

који нису пали на колена пред Валом.“

5Према томе, и у садашње време постоји остатак изабран по милости. 6Дакле, ако се избор врши по милости, онда не може да се врши по делима. Иначе, милост не би више била милост.

7Шта онда? Народ израиљски није постигао оно за чим је тежио. То су достигли изабрани, а остали су отврднули. 8Као што је написано:

„Бог им даде дух тврдоглави,

да очима не виде,

и ушима не чују,

све до данашњега дана.“

9А Давид каже:

„Нек им сто постане замка и клопка,

препрека и одмазда,

10нек им очи потамне, да не виде,

и леђа им се заувек погрбе.“

Спасење незнабожачких народа

11Питам, дакле: зар су посрнули да би сасвим пали? Никако! У ствари, њиховим преступом спасење је дошло другим народима, да у њима изазове љубомору. 12Ако, дакле, њихов преступ значи богатство за свет, а њихов пораз богатство за остале народе, колико ли ће више значити њихово пуно укључење?

13А вама који нисте Јевреји, кажем: као апостол незнабожаца хвалим своју службу, 14не бих ли у њима, мом народу, побудио љубомору, те спасао неке од њих. 15Јер, ако њихово одбацивање значи помирење за свет, шта ће њихово поновно прихватање бити ако не живот из мртвих? 16Наиме, ако је први хлеб свет, онда је и све тесто свето; ако је корен свет, онда су и све гране свете.

17Па ако су неке гране и одломљене, а ти си се као дивља маслина накалемио на њих, те делиш са њима корен и сокове питоме маслине, 18не узноси се над гранама. Ако, пак, хоћеш да се узносиш, знај да не носиш ти корен, него корен тебе. 19Но, ти ћеш рећи: „Гране су одломљене да бих се ја накалемио.“ 20Добро, оне су одломљене због неверовања, а ти стојиш вером. Зато не мисли високо о себи, него се бој. 21Јер, ако Бог није поштедео природне гране, неће поштедети ни тебе.

22Стога, увиди Божију доброту, као и његову строгост: строгост над онима који су пали, а доброту Божију на себи ако останеш у тој доброти – иначе ћеш и сам бити одсечен. 23Чак ће и они Израиљци који не остану у неверовању бити накалемљени, јер је Бог у стању да их поново накалеми. 24Ако си ти, по природи грана дивље маслине, одсечен, те против природе накалемљен на питому маслину, колико ли ће лакше природне гране бити накалемљене на сопствену маслину?!

Обраћење Израиља

25Браћо, не желим да останете у незнању у погледу ове тајне, да се не бисте ослањали на сопствену мудрост: један део израиљског народа је отврднуо док се не употпуни број незнабожаца који ће доћи Богу. 26Тако ће се сав Израиљ спасти, као што је написано:

„Од Сиона ће доћи Избавитељ,

уклониће безбожност од Јакова.

27Ево, ово је мој савез с њима,

кад уклоним њихове грехе.“

28С обзиром да одбијају Радосну вест, они су непријатељи ради вас, али, с обзиром на изабрање, Бог их воли због њихових праотаца. 29Јер, Бог не мења своје мишљење у погледу свог избора и дарова. 30Као што сте ви некад били непослушни Богу, а сада сте услед њихове непослушности примили милосрђе од Бога, 31тако су и они сада, постали непослушни Богу ради вас, да би им Бог исказао милосрђе. 32Бог је, наиме, све затворио под непослушност да би свима исказао своје милосрђе.

33„О, дубино богатства, мудрости и знања Божијег!

Како ли су недокучиве његове одлуке

и неистраживи његови путеви!

34Јер, ко је упознао ум Господњи?

Ко ли му је био саветник?

35Зар му је ко икада дао шта,

да би му он то вратио?

36Јер, све потиче од њега,

и све је створено његовим посредством, и за њега.

Њему нек је слава довека! Амин.“