Aroma 10 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 10:1-21

1Abale, chokhumba cha mtima wanga ndi pemphero langa kwa Mulungu ndi chakuti Aisraeli apulumutsidwe. 2Popeza ndiwachitira umboni kuti ndi achangu pa zinthu za Mulungu koma osati mwachidziwitso. 3Pakuti sanadziwe chilungamo chochokera kwa Mulungu ndipo anafuna kukhazikitsa chawochawo. Iwo sanagonjere chilungamo cha Mulungu. 4Khristu ndiye mathero amalamulo kuti aliyense amene akhulupirira akhale olungama pamaso pa Mulungu.

5Mose akulemba motere zachilungamo cha malamulo, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.” 6Koma chilungamo cha chikhulupiriro chikuti, “Usanene mu mtima mwako kuti, ‘Kodi ndani amene akwere kumwamba?’ ” (ndiko, kukatsitsa Khristu) 7“kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’ ” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). 8Nanga akuti chiyani? “Mawu ali pafupi ndi inu. Ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu.” Ndiwo mawu achikhulupiriro amene ife tikuwalalikira, 9kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, “Yesu ndiye Ambuye,” ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka. 10Pakuti ndi mtima wanu mukhulupirira ndi kulungamitsidwa, ndipo ndi pakamwa panu muvomereza ndi kupulumutsidwa. 11Pakuti Malemba akuti, “Aliyense amene akhulupirira Iye, sadzachititsidwa manyazi.” 12Pakuti palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, pakuti Ambuye mmodzi yemweyo ndi Ambuye wa onse ndipo amadalitsa mochuluka onse amene ayitana pa Iye 13pakuti, “Aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.”

14Kodi adzayitana bwanji amene sanamukhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji asanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji popanda wina kulalikira kwa iwo? 15Ndipo iwo adzalalikira bwanji osatumidwa? Kwalembedwa kuti, “Akongoladi mapazi a iwo amene amabweretsa Uthenga Wabwino!”

16Koma si onse amene anavomereza Uthenga Wabwino. Pakuti Yesaya akuti, “Ambuye, ndani amene wakhulupirira uthenga wathu?” 17Motero, chikhulupiriro chimabwera pamene timva uthenga ndipo uthenga umamveka kuchokera ku mawu a Khristu. 18Koma ndikufunsa kuti kodi iwo anamva? Inde, iwo anamva kuti,

“Liwu lawo linamveka ponseponse pa dziko lapansi.

Mawu awo anafika ku malekezero a dziko lonse.”

19Ine ndifunsanso kuti, kodi Israeli sanazindikire? Poyamba Mose akuti,

“Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake.

Ine ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.”

20Ndipo Yesaya molimba mtima akuti,

“Anandipeza anthu amene sanali kundifunafuna.

Ndinadzionetsera kwa amene sanafunse za Ine.”

21Koma zokhudzana ndi Aisraeli akuti,

“Tsiku lonse ndinatambasulira manja anga

kwa anthu osandimvera ndi okanika.”

New Serbian Translation

Римљанима 10:1-21

1Браћо, жеља мога срца и молитва Богу за њих је да се они спасу. 2Ја, наиме, могу да им посведочим да имају ревности за Бога, али без правог разумевања. 3Али пошто нису познавали Божију праведност, желели су да успоставе своју сопствену, те се нису потчинили Божијој праведности. 4Јер, Христ је довршетак Закона, да свако ко верује у њега дође до праведности пред Богом. 5Јер, Мојсије пише о праведности која се темељи на Закону: „Ко их врши, по њима ће стећи живот.“ 6А праведност која се темељи на вери каже: „Немој рећи у своме срцу: ’Ко ће се попети на небо?’“ (то јест, да спусти Христа) 7„или: ’Ко ће сићи у бездан?’“ (то јест, да доведе Христа из мртвих). 8Оно што каже је ово: „Реч је близу тебе, у твојим устима и у твоме срцу“ – то јест, порука вере коју проповедамо. 9Јер, ако исповедиш да је Исус Господ и верујеш у своме срцу да га је Бог подигао из мртвих, бићеш спасен. 10Наиме, веровање срцем доноси праведност пред Богом, а исповедање усана спасење. 11Зато Писмо говори: „Ко год у њега поверује, неће се постидети.“

12Јер, нема разлике између Јеврејина и Грка, будући да је исти Господ над свима; он богато благосиља оне који га призивају. 13Наиме: „Свако ко зазове име Господње, биће спасен.“

14Али, како да призову онога у кога не верују? Како да верују у онога за кога нису чули? Како да чују без проповедника? 15А опет, како да весници проповедају ако нису послани? Јер, овако је написано:

„Како ли су дивне ноге оних

који доносе добре вести.“

16Ипак, нису сви послушали Радосну вест. Наиме, Исаија каже: „Господе, ко је поверовао нашој поруци?“ 17Дакле, вера долази преко поруке, а порука посредством Христове речи.

18Али, ја питам: зар нису чули? Наравно да су чули! Јер:

„Глас је целом одјекнуо земљом,

речи су им до накрај света стигле.“

19А ја питам: зар Израиљ није разумео? Понајпре Мојсије каже:

„Ја ћу вас учинити љубоморним

народом који није народ,

раздражићу вас народом безумним.“

20Исаија храбро каже:

„Нашли су ме који ме нису тражили,

објавио сам се онима

који нису питали за мене.“

21А Израиљу вели:

„Руке своје пружао сам ваздан

према народу непослушном и недоказаном.“