Aroma 10 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 10:1-21

1Abale, chokhumba cha mtima wanga ndi pemphero langa kwa Mulungu ndi chakuti Aisraeli apulumutsidwe. 2Popeza ndiwachitira umboni kuti ndi achangu pa zinthu za Mulungu koma osati mwachidziwitso. 3Pakuti sanadziwe chilungamo chochokera kwa Mulungu ndipo anafuna kukhazikitsa chawochawo. Iwo sanagonjere chilungamo cha Mulungu. 4Khristu ndiye mathero amalamulo kuti aliyense amene akhulupirira akhale olungama pamaso pa Mulungu.

5Mose akulemba motere zachilungamo cha malamulo, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.” 6Koma chilungamo cha chikhulupiriro chikuti, “Usanene mu mtima mwako kuti, ‘Kodi ndani amene akwere kumwamba?’ ” (ndiko, kukatsitsa Khristu) 7“kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’ ” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). 8Nanga akuti chiyani? “Mawu ali pafupi ndi inu. Ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu.” Ndiwo mawu achikhulupiriro amene ife tikuwalalikira, 9kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, “Yesu ndiye Ambuye,” ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka. 10Pakuti ndi mtima wanu mukhulupirira ndi kulungamitsidwa, ndipo ndi pakamwa panu muvomereza ndi kupulumutsidwa. 11Pakuti Malemba akuti, “Aliyense amene akhulupirira Iye, sadzachititsidwa manyazi.” 12Pakuti palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, pakuti Ambuye mmodzi yemweyo ndi Ambuye wa onse ndipo amadalitsa mochuluka onse amene ayitana pa Iye 13pakuti, “Aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.”

14Kodi adzayitana bwanji amene sanamukhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji asanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji popanda wina kulalikira kwa iwo? 15Ndipo iwo adzalalikira bwanji osatumidwa? Kwalembedwa kuti, “Akongoladi mapazi a iwo amene amabweretsa Uthenga Wabwino!”

16Koma si onse amene anavomereza Uthenga Wabwino. Pakuti Yesaya akuti, “Ambuye, ndani amene wakhulupirira uthenga wathu?” 17Motero, chikhulupiriro chimabwera pamene timva uthenga ndipo uthenga umamveka kuchokera ku mawu a Khristu. 18Koma ndikufunsa kuti kodi iwo anamva? Inde, iwo anamva kuti,

“Liwu lawo linamveka ponseponse pa dziko lapansi.

Mawu awo anafika ku malekezero a dziko lonse.”

19Ine ndifunsanso kuti, kodi Israeli sanazindikire? Poyamba Mose akuti,

“Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake.

Ine ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.”

20Ndipo Yesaya molimba mtima akuti,

“Anandipeza anthu amene sanali kundifunafuna.

Ndinadzionetsera kwa amene sanafunse za Ine.”

21Koma zokhudzana ndi Aisraeli akuti,

“Tsiku lonse ndinatambasulira manja anga

kwa anthu osandimvera ndi okanika.”

Luganda Contemporary Bible

Abaruumi 10:1-21

1Abooluganda, kye njagala mu mutima gwange era kye nsabira Abayisirayiri eri Katonda, kwe kulokolebwa. 210:2 Bik 21:20Kubanga nkakasa nga balina obunyiikivu eri Katonda, naye si mu kutegeera. 310:3 Bar 1:17Mu butamanya butuukirivu bwa Katonda, bagezaako okwenoonyeza obutuukirivu, nga bagondera amateeka mu kifo ky’okugondera obutuukirivu bwa Katonda. 410:4 a Bag 3:24; Bar 7:1-4 b Bar 3:22Kristo atuwa amakulu amajjuvu, buli amukkiriza n’amuwa obutuukirivu.

510:5 Lv 18:5; Nek 9:29; Ez 20:11, 13, 21; Bar 7:10Musa awandiika ku butuukirivu obuva mu mateeka nti, “Omuntu alikola ebintu ebyo aliba mulamu mu byo.” 610:6 a Bar 9:30 b Ma 30:12Naye okukkiriza okuva mu butuukirivu, kugamba nti, “Toyogeranga mu mutima gwo nti, ‘Ani alirinnya mu ggulu?’ (kwe kuggya Kristo mu ggulu) 7newaakubadde okugamba nti, ‘Ani alikka emagombe?’ (kwe kuggya Kristo mu bafu.)” 810:8 Ma 30:14Abo bonna abalina okukkiriza mu Kristo bagamba nti, “Ekigambo kiri kumpi naawe, kiri mu kamwa ko era kiri mu mutima gwo,” kye kigambo eky’okukkiriza kye tubuulira. 910:9 a Mat 10:32; Luk 12:8 b Bik 2:24Bw’oyatula n’akamwa ko nti, Yesu ye Mukama, n’okkiriza n’omutima gwo nga Katonda yamuzuukiza mu bafu, olokoka. 10Kubanga omuntu akkiriza na mutima gwe n’aweebwa obutuukirivu, era ayatula na kamwa ke n’alokoka. 1110:11 Is 28:16; Bar 9:33Kubanga Ebyawandiikibwa bigamba nti, “Buli amukkiriza taliswazibwa.” 1210:12 a Bar 3:22, 29 b Bik 10:36Tewali njawulo wakati wa Muyudaaya na Muyonaani, kubanga Mukama waabwe y’omu era ayanukula abo bonna abamukoowoola. 1310:13 a Bik 2:21 b Yo 2:32Buli alikoowoola erinnya lya Mukama alirokoka. 14Kale balikoowoola batya oyo gwe batakkiririzaamu? Era balikkiriza batya oyo gwe batawulirangako? Era baliwulira batya awatali abuulira? 1510:15 Is 52:7; Nak 1:15Era balibuulira batya nga tebatumiddwa? Ekyawandiikibwa nga bwe kigamba nti, “Ebigere by’abo abategeeza amawulire amalungi, nga birungi.” 1610:16 Is 53:1; Yk 12:38Naye si bonna abaagondera Enjiri. Isaaya agamba nti, “Mukama, waliwo akkirizza obubaka bwaffe?” 1710:17 a Bag 3:2, 5 b Bak 3:16Noolwekyo okukkiriza kujja olw’okuwulira ekigambo kya Kristo. 1810:18 Zab 19:4; Mat 24:14; Bak 1:6, 23; 1Bs 1:8Naye mulowooza Abayisirayiri tebaawulira? Weewaawo baawulira. Ebyawandiikibwa bigamba nti,

“Eddoboozi lyabwe lyabuna mu nsi zonna,

n’ebigambo byabwe byatuuka ku nkomerero z’ensi.”

1910:19 a Bar 11:11, 14 b Ma 32:21Abayisirayiri baabitegeera oba tebaabitegeera? Bw’ati Musa bw’addamu ekibuuzo ekyo:

“Ndibaleetera okukwatirwa obuggya abatali ggwanga,

ne mbasunguwaza olw’eggwanga eritalina kutegeera.”

2010:20 Is 65:1; Bar 9:30Ne Isaaya yali muvumu bwe yagamba nti,

“Nazuulibwa abo abatannoonya,

ne ndabika eri abo abatambuulirizaako.”

2110:21 Is 65:2Naye eri Isirayiri agamba nti,

“Olunaku lwonna nalumala nga ngolodde emikono gyange

eri eggwanga ekkakanyavu era abantu abeewaggula.”