Aroma 9 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 9:1-33

Chisankho Chopambana cha Mulungu

1Ine ndikunena zoona mwa Khristu. Sindikunama ndipo chikumbumtima changa kudzera mwa Mzimu Woyera chikundichitira umboni. 2Ndili ndi chisoni chachikulu ndipo ndikumva kupwetekeka kosalekeza mu mtima mwanga. 3Pakuti ndikanafuna ine mwini nditatembereredwa ndi kuchotsedwa mwa Khristu chifukwa cha abale anga, amene ndi a mtundu wanga, 4anthu Aisraeli. Iwo anasankhidwa kukhala ana. Mulungu anawapatsa ulemerero, anachita nawo mapangano, kuwapatsa Malamulo, Nyumba yopembedzeramo ndi malonjezano ake. 5Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni.

6Sikuti mawu a Mulungu analephera. Pakuti si onse obadwa mwa Israeli amene ndi Israeli. 7Kapena kuti ana ake chifukwa anachokera mwa Abrahamu. Koma zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake. 8Kutanthauza kuti, si ana obadwa mʼthupi amene ndi ana a Mulungu koma ndi ana a lonjezano amene amatengedwa kukhala zidzukulu za Abrahamu. 9Pakuti Mulungu analonjeza ponena kuti, “Pa nthawi yake ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.”

10Ndipo si pokhapo ayi. Ana awiri a Rebeka aja abambo awo anali mmodzi, kholo lathu Isake. 11Komabe, ana amapasawa asanabadwe kapena asanachite chilichonse chabwino kapena choyipa, nʼcholinga choti chifuniro cha Mulungu chosankhiratu munthu aliyense chipitirire, 12osati chifukwa cha ntchito za munthu koma chifuniro cha Iye mwini, anawuza Rebeka kuti, “Wamkulu adzatumikira wamʼngʼono.” 13Monga momwe kwalembedwa kuti, “Ine ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau.”

14Nanga tsono tidzanena chiyani? Kodi Mulungu ndi osalungama? Ayi, ndi pangʼono pomwe! 15Pakuti Mulungu anawuza Mose kuti,

“Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo,

ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”

16Nʼchifukwa chake, izi sizitengera zokhumba za munthu kapena kuyesetsa koma chifundo cha Mulungu. 17Malemba akuti Mulungu anamuwuza Farao kuti, “Ine ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga, kuti mwa iwe dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.” 18Choncho Mulungu amachitira chifundo munthu amene akufuna kumuchitira chifundo ndipo amawumitsa mtima munthu amene Iye akufuna kumuwumitsa mtima.

19Tsono mmodzi wa inu nʼkundifunsa kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mulungu amatipeza olakwa? Nanga ndani amene amakana chifuniro chake?” 20Koma ndiwe yani, munthu wamba, woti nʼkutsutsana ndi Mulungu? “Kodi chimene chinawumbidwa nʼkufunsa amene anachiwumba kuti, ‘Kodi unandiwumbiranji motere?’ ” 21Kodi wowumba alibe ufulu wowumba kuchokera ku dothi lomwelo mbiya yamtengowapatali ndi ina yamtengo wotsika?

22Koma Mulungu, anafuna kuonetsa mkwiyo wake ndi kuti mphamvu yake idziwike. Iye anapirira modekha mtima kwambiri zochita za anthu omwe anawakwiyirawo amene anayeneradi chiwonongeko. 23Iye anachita izi kufuna kuonetsa kulemera kwa ulemerero wake ndi kuti udziwike kwa amene analandira chifundo chake. Iye anawakonzeratu kuti alandire ulemerero wake 24ngakhale ifenso amene anatiyitana osati kuchokera kwa Ayuda okha komanso kwa a mitundu ina. 25Monga momwe Mulungu akunenera mʼbuku la Hoseya kuti,

“Amene sanali anthu anga ndidzawatcha ‘anthu anga;’

ndipo Ine ndidzatcha ‘wokondedwa wanga’ amene sali wokondedwa wanga,”

26ndipo,

“Pamalo omwewo pamene ananena kuti,

‘Sindinu anthu anga,’

pomweponso adzawatchula kuti, ‘Ana a Mulungu wamoyo.’ ”

27Yesaya anafuwula za Aisraeli kuti,

“Ngakhale chiwerengero cha Aisraeli chingakhale ngati mchenga wa ku nyanja,

otsala okha ndiye adzapulumuke.

28Pakuti Ambuye adzagamula milandu

ya anthu pa dziko lapansi mofulumira ndi kumaliziratu.”

29Monga momwe Yesaya ananena malo ena kuti,

“Ngati Yehova Wamphamvuzonse

akanapanda kutisiyira zidzukulu,

ife tikanawonongeka

ngati anthu a ku Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.”

Kusakhulupirira kwa Aisraeli

30Kodi nanga tidzati chiyani? Tidzati a mitundu ina amene sanafune chilungamo analandira chilungamo chachikhulupiriro 31koma Aisraeli, amene anafuna chilungamo cha lamulo sanachilandire. 32Chifukwa chiyani? Chifukwa iwo sanachifune ndi chikhulupiriro koma ngati mwa ntchito. Iwo anapunthwa pa “Mwala wopunthwitsa.” 33Monga momwe kwalembedwa kuti,

“Taonani, Ine ndikuyika mwala mu Ziyoni wopunthwitsa anthu,

thanthwe limene limagwetsa anthu.

Koma amene akhulupirira Iye sadzachititsidwa manyazi.”

Luganda Contemporary Bible

Abaruumi 9:1-33

Okulonda kwa Katonda

19:1 a 2Ko 11:10 b Bar 1:9Njogera amazima mu Kristo, sirimba, omwoyo gwange nga gunkakasa mu Mwoyo Mutukuvu, 2nga ndimunakuwavu nnyo era nga nnumwa mu mutima. 39:3 a Kuv 32:32 b 1Ko 12:3; 16:22 c Bar 11:14Nnali njagala nze mwene nkolimirwe Katonda era njawukanyizibwe ku Kristo olwa baganda bange, bwe tuli ab’omu mubiri, 49:4 a Kuv 4:22 b Lub 17:2; Bik 3:25 c Zab 147:19 d Beb 9:1 e Bik 13:32be Bayisirayiri, abantu ba Katonda abalonde. Katonda yabalaga ekitiibwa kye, n’akola nabo endagaano, n’abawa n’amateeka ge. Yeekaalu yagibawa, n’abawa n’ebyasuubizibwa. 59:5 a Mat 1:1-16 b Yk 1:1 c Bar 1:25Balina bajjajjaabwe abamanyiddwa, Kristo be yasibukamu mu mubiri. Nsaba Katonda afuga byonna atenderezebwenga emirembe gyonna, Amiina.

69:6 Bar 2:28, 29Naye si kuba nti Katonda yalemwa okutuukiriza kye yasuubiza. Si bonna ab’omu Isirayiri nti bantu ba Katonda ddala. 79:7 Lub 21:12Ate so si nti ly’ezzadde lya Ibulayimu bonna balyoke babeere abaana, naye ekisuubizo kyali ku Isaaka bwe kyagambibwa nti, “Mu Isaaka mwe ndituukiririza ebyo byonna bye nakusuubiza.” 89:8 Bar 8:14Kino kitegeeza nti abaana ab’omubiri si be baana ba Katonda, wabula abo ab’okusuubiza be babalibwa okuba ezzadde lya Ibulayimu. 99:9 Lub 18:10, 14Kubanga ekigambo ky’okusuubiza kye kino nti, “Mu kiseera nga kino Saala alizaala omwana owoobulenzi.”

109:10 Lub 25:21Ate si ekyo kyokka, naye ne Isaaka jjajjaffe yalina Lebbeeka eyali olubuto. 119:11 Bar 8:28Naye ng’abalongo tebannazaalibwa, era nga tebannabaako kye bakola kyonna ekirungi oba ekibi, okusiima kwa Katonda nga bwe kuli, 129:12 Lub 25:23si lwa bikolwa wabula ku bw’oyo eyabayita, kyategeezebwa Lebbeeka nti, “Omukulu y’aliba omuweereza w’omuto.” 139:13 Mal 1:2, 3Era nga bwe kyawandiikibwa nti, “Yakobo namwagala, naye Esawu namukyawa.”

149:14 2By 19:7Kale tunaagamba ki? Ddala ddala Katonda talina bwenkanya? Kikafuuwe. 159:15 Kuv 33:19Agamba Musa nti,

“Ndisaasira oyo gwe ndisaasira,

era ndikwatirwa ekisa oyo gwe ndikwatirwa ekisa.”

169:16 Bef 2:8Noolwekyo tekiva ku ebyo omuntu by’ayagala newaakubadde by’akola, wabula ku kusaasira kwa Katonda. 179:17 Kuv 9:16Ebyawandiikibwa kyebyava byogera ku Falaawo nti, “Kyennava nkuyimusa, ndyoke njolese amaanyi gange mu ggwe, erinnya lyange liryoke litegeezebwe mu nsi zonna.” 189:18 Kuv 4:21Noolwekyo Katonda asaasira oyo gw’ayagala okusaasira, ate n’akakanyaza omutima gw’oyo gw’ayagala okukakanyaza.

199:19 a Bar 11:19 b 2By 20:6; Dan 4:35Omu akyayinza okumbuuza nti, Lwaki Katonda atunenya, obanga y’atuleetera okukola nga bw’asiima? 209:20 a Is 64:8 b Is 29:16Naye ggwe omuntu obuntu, ggwe ani addamu ng’owakanya Katonda? Ekibumbe kiyinza okubuuza eyakibumba nti, “Lwaki wammumba bw’oti?” 219:21 2Ti 2:20Oba omubumbi talina buyinza ku bbumba, okubumbamu ekibya eky’omugaso, oba okubumbamu ekitali kya mugaso?

229:22 Bar 2:4Katonda yayagala okulaga obusungu bwe, n’amaanyi ge eri abo bonna abaali basaanira okuzikirizibwa, kyokka n’abalaga obugumiikiriza. 239:23 a Bar 2:4 b Bar 8:30Ekyo yakikola alyoke amanyise obugagga bw’ekitiibwa kye, eri abo bonna be yeerondera okugabanira awamu ekitiibwa kye. 249:24 a Bar 8:28 b Bar 3:29Naffe yatuyita, si Bayudaaya bokka naye n’Abaamawanga. 259:25 Kos 2:23; 1Pe 2:10Ne mu Koseya agamba nti,

“Abataali bantu bange ndibayita abantu bange,

Ne gwe nnali ssaagala, ndimwagala.”

269:26 Kos 1:10Mu kifo omwo mwe baayitirwa nti,

“Temuli bantu bange,

mwe baliyitirwa abaana ba Katonda omulamu.”

279:27 a Lub 22:17; Kos 1:10 b Bar 11:5Isaaya ayogera eri Isirayiri mu ddoboozi ery’omwanguka nti,

“Omuwendo gw’abaana ba Isirayiri ne bwe gulyenkana ng’omusenyu gw’ennyanja,

ekitundu ekirisigalawo kye kirirokolebwa.

289:28 Is 10:22, 23Kubanga Mukama alisalawo

era alituukiriza mangu ekyo kye yagamba okukola ku nsi.”

299:29 a Yak 5:4 b Is 1:9; Ma 29:23; Is 13:19; Yer 50:40Era nga Isaaya bwe yayogera edda nti,

“Singa Mukama ow’Eggye

teyatulekerawo zzadde,

twandifuuse nga Sodomu,

era twandifaananye nga Ggomola.”

Obutakkiriza bw’Abayudaaya

309:30 Bar 1:17; 10:6; Bag 2:16; Baf 3:9; Beb 11:7Kale tunaagamba ki? Tugambe nti Abaamawanga abataagobereranga butuukirivu, baafuna obutuukirivu, bwe butuukirivu obuva mu kukkiriza, 319:31 a Is 51:1; Bar 10:2, 3 b Bag 5:4naye Isirayiri mu kugobereranga amateeka ag’obutuukirivu, teyafuna butuukirivu obwo? 329:32 1Pe 2:8Lwaki? Ekyo baalema okukituukako kubanga tebaagoberera butuukirivu mu kukkiriza wabula mu bikolwa. Beesittala ku jjinja eryo eryesittalwako, 339:33 Is 28:16; Bar 10:11nga bwe kyawandiikibwa nti,

“Laba, nteeka mu Sayuuni ejjinja eryesittalwako9:33 Ejjinja eryesittalwako ye Kristo.

n’olwazi olulibasuula.

Oyo amukkiriza taliswazibwa.”