1Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu 2umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake. 3Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide. 4Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu, 5ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe. 6Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
7Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima.
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
Paulo Afunitsitsa Kukacheza ku Roma
8Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu. 9Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse. 10Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
11Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni 12ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake. 13Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
14Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe. 15Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
16Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene. 17Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
Mkwiyo wa Mulungu pa Mtundu wa Anthu
18Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa. 19Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo. 20Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula.
21Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima. 22Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa. 23Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
24Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo. 25Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni.
26Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo. 27Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
28Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo. 29Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche, 30osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo, 31alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza. 32Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.
سلام و درود از پولس
1من، پولس، كه غلام عيسی مسيح میباشم، اين نامه را برای شما مینويسم. خدا مرا برگزيده و فرستاده است تا مژدهٔ انجيل او را به همگان برسانم. 2انجيلی كه وعدهاش را از زمانهای دور توسط انبيای خود در كتاب آسمانی داده بود.
3اين مژده دربارهٔ فرزند خدا، يعنی خداوند ما عيسی مسيح میباشد كه همچون انسان از نسل داوود نبی به دنيا آمد؛ 4اما با زنده شدنش پس از مرگ، ثابت كرد كه فرزند نيرومند خدا و دارای ذات مقدس الهی است.
5بوسيلهٔ عيسی مسيح است كه خدا فيض و لطف بیپايان خود را شامل حال ما گناهكاران نالايق كرده و ما را به سراسر جهان فرستاده تا به همهٔ اقوام اعلام كنيم كه او چه لطف عظيمی نموده است، تا ايشان نيز به عيسی مسيح ايمان آورند و از او اطاعت كنند.
6-7برادران عزيز كه در شهر روم هستيد و اين نامه را میخوانيد، شما نيز جزو كسانی هستيد كه مورد مهر و محبت خدا میباشند، زيرا شما هم بوسيلهٔ عيسی مسيح دعوت شدهايد تا قوم مقدس خدا و از آن او باشيد. پس، از پدرمان خدا و خداوندمان عيسی مسيح، طالب رحمت و آرامش برای شما میباشم.
دعای شكرگزاری برای مسيحيان روم
8پيش از هر چيز، بايد بگويم كه خبر ايمانتان به تمام دنيا رسيده و همه جا صحبت از شماست. از این رو، برای اين خبر و برای وجود هر يک از شما، خدا را بوسيلهٔ عيسی مسيح شكر میكنم. 9خدا شاهد است كه من پيوسته برای شما دعا میكنم، و روز و شب احتياجاتتان را به حضور او میبرم، به حضور خدايی كه با تمام توانم او را خدمت میكنم و مژدهٔ انجيل او را كه دربارهٔ فرزندش عيسی مسيح است، به ديگران اعلام مینمايم.
10دعای ديگرم اينست كه اگر خدا بخواهد، پس از اين همه انتظار، سعادت ديدار شما نصيبم شود. 11زيرا بسيار مشتاق ديدارتان هستم تا بتوانم شما را از بركات خدا برخوردار سازم، و باعث تقويت ايمانتان شوم. 12از اين گذشته، من خود نيز نياز به كمک شما دارم تا بوسيلهٔ ايمانتان تقويت شوم. به اين ترتيب، هر يک از ما باعث تقويت ايمان يكديگر میگرديم.
13اما برادران عزيز، مايلم بدانيد كه بارها خواستهام نزد شما بيايم، اما هر بار مانعی پيش آمده است. قصد من از آمدن، اين بود كه خدمتی در ميان شما انجام دهم و عدهای را به سوی مسيح هدايت كنم، همانطور كه در جاهای ديگر نيز كردهام. 14زيرا من خود را مديون میدانم كه اين خبر خوش را به همه برسانم، چه به اشخاص متمدن و چه به اشخاص بیتمدن، چه به تحصيلكردهها و چه به بیسوادان. 15پس تا آنجا كه در توان دارم، خواهم كوشيد كه به «روم»، نزد شما بيايم و مژدهٔ انجيل را در ميان شما اعلام نمايم. 16زيرا من به انجيل عيسی مسيح افتخار میكنم چون قدرت خداست برای نجات تمام كسانی كه ايمان بياورند. پيغام انجيل در ابتدا فقط به يهوديان اعلام میشد، اما اكنون همه میتوانند با ايمان آوردن به آن، به حضور خدا راه يابند. 17اين پيغام اينست كه خدا فقط در يک صورت از سر تقصيرات ما میگذرد و به ما شايستگی آن را میدهد كه به حضور او برويم؛ و آن وقتی است كه به عيسی مسيح ايمان آوريم. بلی، فقط و فقط ايمان لازم است. همانطور كه كتاب آسمانی میفرمايد: «فقط كسی نجات پيدا میكند كه به خدا ايمان داشته باشد.»
خشم خدا نسبت به گناهان بشر
18اما از سوی ديگر، خدا خشم و غضب خود را بر تمام اشخاص گناهكار و نادرست كه از حقيقت گريزانند، نازل میكند. 19برای آنان حقيقت وجود خدا كاملاً روشن است، زيرا خدا وجدانهايشان را از اين حقيقت آگاه ساخته است. 20انسان از ابتدا، آسمان و زمين و چيزهايی را كه خدا آفريده، ديده است و با ديدن آنها میتواند به وجود خدا و قدرت ابدی او كه ناديدنی هستند پی ببرد. پس وقتی در روز داوری در حضور خدا میايستد، برای بیايمانی خود هيچ عذر و بهانهای ندارد.
21بلی، درست است كه مردم اين حقايق را میدانند، اما هيچگاه حاضر نيستند به آن اعتراف كنند و خدا را عبادت نمايند و يا حتی برای بركاتی كه هر روز عطا میكند، او را شكر گويند. در عوض دربارهٔ وجود خدا و ارادهٔ او، عقايد احمقانهای ابداع میكنند. به همين علت ذهن نادانشان، تاريک و مغشوش شده است. 22خود را دانا و خردمند میپنداشتند، اما همگی، نادان و بیخرد شدند. 23به جای اينكه خدای بزرگ و ابدی را بپرستند، بتهايی از چوب و سنگ به شكل انسان فانی، پرندگان، چارپایان و خزندگان ساختند و آنها را پرستيدند.
24بنابراين، خدا نيز ايشان را به حال خود رها كرده تا هر چه میخواهند بكنند و در آتش شهوات گناهآلود خود بسوزند و با بدنهای خود مرتكب گناهان شرمآور شوند. 25ايشان به جای اينكه به حقيقت وجود خدا ايمان بياورند، عمداً عقايد باطل را پذيرفتهاند و مخلوق خدا را به جای خالقی كه تا ابد مورد ستايش است، میپرستند و خدمت میكنند.
26به همين دليل است كه خدا مردم را به حال خود رها كرده است تا خويشتن را به گناهان زشت آلوده سازند، به طوری كه حتی زنها به جای روابط جنسی طبيعی، با زنان ديگر مرتكب اعمال قبيح میگردند، 27و مردها نيز به جای اينكه با زنان خود روابط طبيعی زناشويی داشته باشند، با مردهای ديگر مرتكب گناهان شرمآور میشوند. بنابراين، سزای كارهای كثيف خود را در روح و بدن خود میبينند.
28پس همانطور كه ايشان خدا را ترک كردهاند و حتی حاضر نيستند به وجود او اعتراف كنند، خدا نيز ايشان را به حال خود رها كرده است تا هر آنچه به ذهن ناپاكشان خطور میكند، به عمل آورند. 29زندگی آنان پر است از هر نوع شرارت و بدی، طمع و نفرت و حسادت، قتل و جدال، دروغ و كينه و سخنچينی. 30غيبت از زبانشان دور نمیشود. ايشان دشمنان خدا هستند. با غرور و گستاخی، خودستايی میكنند. هميشه به دنبال راههای تازه میگردند تا بيشتر گناه ورزند. هرگز مطيع والدين خود نمیشوند. 31بیاحساسند و بدقول و بیعاطفه و بیرحم. 32با اينكه میدانند خدا برای چنين اعمالی، مجازات مرگ تعيين كرده است، نه فقط خودشان مرتكب آنها میگردند، بلكه ديگران را نيز به انجام اين كارها تشويق میكنند!