Ahebri 8 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 8:1-13

Mkulu wa Ansembe wa Pangano Latsopano

1Fundo yayikulu pa zimene tikunenazi ndi iyi: Tili naye ife Mkulu wa ansembe, amene anakhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu Waulemerero kumwamba. 2Ndipo akutumikira mʼmalo opatulika, mu Tenti yeniyeni yoyikidwa ndi Ambuye, osati ndi munthu.

3Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuti azipereka mphatso ndi nsembe kwa Mulungu, ndipo kunali koyenera kuti wansembe wathunso akhale nʼkanthu kopereka. 4Ngati iye akanakhala pa dziko lapansi, sakanakhala wansembe pakuti alipo kale anthu amene amapereka mphatso zolembedwa mʼMalamulo. 5Iwo amatumikira pamalo opatulika amene ndi chithunzi ndi chifanizo cha zimene zili kumwamba. Ichi ndi chifukwa chake Mose anachenjezedwa pamene anali pafupi kumanga Tenti: “Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.” 6Koma Yesu analandira utumiki wopambana kuposa wawo monga Iyenso ali Nkhoswe ya pangano lopambana kuposa lakale lija, chifukwa pangano latsopano lakhazikika pa malonjezano opambana kwambiri.

7Ngati pangano loyamba lija likanakhala langwiro, sipakanafunikanso lina mʼmalo mwake. 8Koma Mulungu anapeza zolakwika pakati pa anthu ndipo anati,

“Masiku akubwera,” akutero Yehova,

“pamene ndidzachita pangano latsopano

ndi Aisraeli

ndiponso nyumba ya Yuda.

9Silidzakhala ngati pangano

limene ndinachita ndi makolo awo,

pamene ndinawagwira padzanja

nʼkuwatulutsa ku Igupto

chifukwa iwo sanasunge pangano langa lija

ndipo Ine sindinawasamalire,

akutero Ambuye.

10Tsono ili ndi pangano ndidzapangane ndi nyumba ya Israeli:

Atapita masiku amenewa, akutero Ambuye,

Ine ndidzayika malamulo anga mʼmaganizo mwawo,

ndi kulemba mʼmitima mwawo.

Ine ndidzakhala Mulungu wawo,

ndipo iwo adzakhala anthu anga.

11Sipadzafunikanso wina kuti aphunzitse mnzake,

kapena munthu kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, udziwe Ambuye

chifukwa onse adzandidziwa,

kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu.

12Pakuti Ine ndidzawakhululukira zoyipa zawo,

ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”

13Ponena kuti, pangano “latsopano” Mulungu wapanga pangano loyamba lija kukhala lotha ntchito, ndipo chilichonse chimene chayamba kutha ntchito ndi kukalamba, chili pafupi kuchokeratu.

New Russian Translation

Евреям 8:1-13

Иисус – Первосвященник нового завета

1Главное из того, о чем мы вам говорим, – это то, что у нас есть такой Первосвященник, Который находится на небесах по правую сторону от престола Всемогущего8:1 См. Пс. 109:1., 2служитель в святилище, в истинной скинии8:2 Скиния – шатер, служивший походным святилищем израильтянам во время их странствия по пустыне., воздвигнутой не людьми, а Господом. 3Каждый первосвященник определен на то, чтобы приносить приношения и жертвы, поэтому и наш Первосвященник должен был иметь что-то, что можно было бы принести в жертву. 4Если бы Он был сейчас на земле, Он не был бы даже священником, потому что уже существуют священники, приносящие жертвы в соответствии с Законом. 5Они совершают служение в святилище, которое служит лишь подобием и тенью небесного. Поэтому Моисей, перед тем как строить скинию, был предупрежден: «Смотри, – сказал Бог, – сделай все точно по образцу, который был тебе показан на горе»8:5 См. Исх. 25:40.. 6Но сейчас Христу поручено служение, которое намного превосходит служение земных священников, потому что Он – посредник лучшего завета Бога с человеком, основанного на лучших обещаниях.

7Если бы первый завет8:7 Первый завет – см. Исх. 19:3-8; Втор. 5. был без недостатков, то не было бы нужды во втором. 8Но Бог, видя недостатки людей, говорит:

«Вот приходят дни, – говорит Господь, –

когда Я заключу новый завет

с домом Израиля и с домом Иуды.

9Этот завет будет не таким,

какой Я заключил с их праотцами,

когда Я за руку вывел их из Египта,

потому что они не были верны завету со Мной,

и Я отвернулся от них, –

говорит Господь. –

10Поэтому Я в будущем заключу с домом Израиля

такой завет, – говорит Господь. –

Законы Мои Я вложу в их разум

и запишу в их сердцах.

Я буду их Богом,

а они будут Моим народом.

11И уже не будет друг учить друга,

и брат – брата,

говоря ему: „Познай Господа“,

потому что Меня будут знать все

от мала до велика.

12Ведь Я прощу их беззакония

и больше не вспомню их грехов»8:8-12 См. Иер. 31:31-34..

13Он назвал этот завет «новым» и тем самым показал, что первый завет устарел. А то, что устарело и обветшало, – скоро исчезнет.