Yakobo 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yakobo 1:1-27

1Yakobo, mtumiki wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Khristu,

kulembera mafuko khumi ndi awiri obalalikana ku mayiko osiyanasiyana.

Landirani moni.

Masautso ndi Mayesero

2Abale, muchiyese ngati chimwemwe chenicheni nthawi zonse pamene mukukumana ndi mayesero amitundumitundu. 3Inu mukudziwa kuti kuyesedwa kwa chikhulupiriro chanu kumabweretsa chipiriro. 4Chipiriro chiyenera kugwira ntchito yake kuti mukhale okhwima ndi angwiro, osasowa kanthu kalikonse. 5Ngati wina pakati panu akusowa nzeru, apemphe kwa Mulungu amene amapereka kwa onse mwaulere ndi mosatonzera, ndipo adzapatsidwa. 6Koma pamene mupempha, muyenera kukhulupirira osakayika, chifukwa amene amakayika ali ngati mafunde pa nyanja amene amawinduka nakankhika ndi mphepo. 7Munthu wotere asayembekezere kulandira kalikonse kuchokera kwa Ambuye. 8Iyeyu ndi munthu wa mitima iwiri, wosakhazikika pa zimene akuchita.

9Abale omwe ndi anthu wamba anyadire pamene akwezedwa. 10Koma olemera anyadire pamene atsitsidwa, chifukwa adzatha ngati duwa lakuthengo. 11Pakuti dzuwa limatuluka nʼkutentha kwake, ndipo limafotetsa zomera. Duwa lake limathothoka ndipo kukongola kwake kumatheratu. Momwemonso munthu wachuma adzazimirira ngakhale atamachitabe malonda ake.

12Wodala ndi munthu amene amapirira mʼmayesero, chifukwa akapambana adzalandira chipewa cha ulemerero chimene Mulungu analonjeza anthu amene amamukonda.

13Munthu akayesedwa asanene kuti, “Mulungu akundiyesa.” Pakuti Mulungu sangayesedwe ndi choyipa kapena Iyeyo kuyesa munthu aliyense. 14Koma munthu aliyense amayesedwa akakokedwa ndi zilakolako zake zoyipa ndi kukopedwa nazo. 15Pamenepo, chilakolako chikakula chimabala tchimo; ndipo tchimo likakhwima limabereka imfa.

16Musanyengedwe abale anga okondedwa. 17Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera kumwamba, kwa Atate mwini kuwala, amene sasintha ngati mthunzi woyendayenda. 18Iye anasankha kutibereka ife kudzera mʼmawu a choonadi, kuti pakati pa zolengedwa zake zonse, tikakhale ngati zipatso zoyamba.

Kumva ndi Kuchita

19Abale anga okondedwa, gwiritsitsani mawu awa: munthu aliyense azifulumira kumva, koma asamafulumire kuyankhula, ndipo asamafulumirenso kupsa mtima. 20Pakuti mkwiyo wa munthu subweretsa chilungamo chimene amafuna Mulungu. 21Choncho chotsani chizolowezi choyipa ndi khalidwe loyipa pakati panu, ndipo modzichepetsa landirani mawu amene anadzalidwa mwa inu, amene akhoza kukupulumutsani.

22Musamangomvetsera chabe mawu, ndi kumadzinyenga nokha. Chitani zimene mawuwo amanena. 23Munthu aliyense amene amangomva mawu koma osachita zimene mawuwo amanena, ali ngati munthu amene amayangʼana nkhope yake pa galasi. 24Akadziyangʼana amachoka, nthawi yomweyo nʼkuyiwala mmene akuonekera. 25Koma munthu amene amayangʼana mwachidwi lamulo langwiro limene limapatsa ufulu ndi kupitiriza kutero, osayiwala chimene wamva koma kuchita adzadalitsika pa zimene amachita.

26Ngati wina amadziyesa ngati ndi wachipembedzo, koma chonsecho saletsa lilime lake, amadzinyenga yekha ndipo chipembedzo chakecho ndi cha chabechabe. 27Chipembedzo chimene Mulungu Atate athu amachivomereza kuti ndi changwiro ndi chopanda zolakwika ndi ichi: kusamalira ana amasiye ndi akazi amasiye pa mavuto awo, ndi kudzisunga bwino kuopa kudetsedwa ndi dziko lapansi.

New Russian Translation

Иакова 1:1-27

1Двенадцати родам иудеев, рассеянным среди народов.

Вас приветствует Иаков, слуга Бога и Господа Иисуса Христа.

Мудрость и вера

2Братья, когда вы сталкиваетесь с различного рода испытаниями1:2 Испытаниями – или «искушениями»., считайте это великой радостью. 3Вы знаете, что испытание вашей веры вырабатывает стойкость, 4а стойкость должна настолько возрасти в вас, чтобы вы стали зрелыми и цельными, без всяких недостатков. 5Если кому-то из вас недостает мудрости, пусть просит у Бога, Который, не упрекая, щедро наделяет ею всех, – и ему будет дано. 6Но тот, кто просит, должен верить, нисколько не сомневаясь, потому что сомневающийся похож на морскую волну, носимую и разбиваемую ветром. 7Пусть такой человек не рассчитывает получить что-либо от Господа. 8Это двоедушный человек, нетвердый во всем, что бы он ни делал.

Богатство не вечно

9Брат из низшего сословия, на самом деле, может хвалиться своим высоким положением. 10А богатый может хвалиться своим унижением, потому что он исчезнет, как полевой цветок. 11Восходит солнце и своим жаром сушит растение, его цветок опадает, и вся красота исчезает1:10-11 См. Ис. 40:6-7; 1 Пет. 1:24.. Так же и богатый человек увянет за своими делами.

12Блажен тот, кто, перенеся испытание, выдержит его до конца – он получит венец жизни1:12 Венец жизни – дар вечной жизни после смерти, но, вероятно, это может быть и полная, совершенная жизнь здесь на земле., который Бог обещал всем, кто любит Его. 13Когда вас постигает искушение, не говорите: «Это Бог меня искушает». Бог Сам не может быть искушен злом и не искушает никого. 14Каждого человека искушают его же собственные желания, они увлекают и соблазняют его. 15Затем желание зачинает и порождает грех, а сделанный грех порождает смерть.

16Любимые мои братья, не заблуждайтесь. 17Все добрые и совершенные дары исходят свыше, от Отца светил, у Которого нет ни изменения, ни тени перемены. 18Он Сам по Своей воле родил нас словом истины, чтобы нам быть первыми плодами1:18 Первые плоды – первый урожай, первенцы животных и людей в древности считались священными и посвящались Богу (см., напр., Исх. 13:1-2; Лев. 23:9-14; Чис. 3:12; 15:20-21; Втор. 15:19-23; 26:1-11). В данном тексте может быть четыре варианта толкования выражения «первые плоды»: 1) верующие в Иисуса Христа – это люди, которые посвящены Богу; 2) последователи Христа являются первыми (хронологически) среди «нового творения» (см. Рим. 8:19-21; Отк. 21:1-5); 3) первые плоды – это признак будущего урожая, и возможно в этом смысле ранние (первые) последователи Иисуса Христа названы первыми плодами; 4) у верующих в Христа особое положение в глазах Бога. Вполне вероятно, что правильными могут быть сразу несколько из приведенных выше вариантов. среди Его созданий.

Слова и поступки

19Любимые мои братья, поймите: пусть каждый будет склонен скорее слушать, чем говорить или проявлять гнев. 20В гневе человек не делает угодного Богу. 21Поэтому оставьте всякую нечистоту и остаток злобы и в кротости примите насаждаемое слово, которое имеет силу спасти ваши души.

22При этом будьте не только слушателями слова, но и исполнителями его, иначе вы просто обманываете себя. 23Кто слушает слово, но не исполняет его, тот похож на человека, который смотрит в зеркало: 24он посмотрел на себя, отошел и сразу же забыл, как выглядит. 25Но человек, который постоянно вникает в совершенный Закон, Закон, дающий свободу, и поступает согласно ему, не забывая о том, что слышал, будет блажен в своих делах.

26Кто считает себя благочестивым, но не может управлять своим языком, тот обманывает самого себя, и благочестие такого человека бесполезно. 27Чистое и непорочное благочестие перед Богом, нашим Отцом, заключается в том, чтобы помогать сиротам и вдовам в их нуждах и хранить себя чистым от этого мира.