Ahebri 6 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 6:1-20

1Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu, 2za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. 3Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.

4Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera. 5Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. 6Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.

7Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa. 8Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.

9Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso. 10Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano. 11Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera. 12Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.

Kukhazikika kwa Malonjezo a Mulungu

13Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti, 14“Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.” 15Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.

16Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse. 17Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro. 18Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira. 19Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga. 20Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.

New Russian Translation

Евреям 6:1-20

1Поэтому давайте перейдем от основ учения о Христе к тому, что предназначено для зрелых. Мы не станем опять обосновывать необходимость покаяния в делах, которые ведут к смерти, необходимость веры в Бога, 2учения о крещениях6:2 Крещения – или «обряды омовения». См., напр., Мк. 7:3-4; Лк. 3:3, 16-17; Ин. 2:6; Деян. 22:16., о возложении рук6:2 Возложение рук – ритуал возложения рук преследовал различные цели в зависимости от обстоятельств. Этот ритуал включал в себя и благословение другого лица, и передачу кому-либо власти, и наделение авторитетом, и исцеление, и др. (напр., Быт. 48:13-20; Мат. 19:13-15; Мк. 6:5; Деян. 6:6; 8:16-17; 13:3; 19:5-6; 28:8; 1 Тим. 5:22 (со сноской); 2 Тим. 1:6)., о воскресении мертвых и вечном суде. 3И мы сделаем это, если Бог позволит.

4Потому что тех, кто уже был один раз просвещен, кто лично познал вкус небесного дара и стал сопричастен Святому Духу, 5кто также лично познал вкус доброго Божьего слова и действие силы будущего века 6и после этого отпал от веры, – невозможно опять обновлять покаянием, потому что6:6 Потому что – или «когда». они сами заново распинают Сына Божьего, предавая Его публичному позору.

7Земля, которая пьет часто выпадающий на нее дождь и приносит урожай тому, кто ее обрабатывает, благословенна Богом. 8А та, на которой растут лишь сорняки и колючки, ни на что не годна. Ей грозит проклятие, и концом ее будет сожжение.

9Но, любимые, хоть мы и говорим так, мы уверены, что вы находитесь в лучшем состоянии и держитесь спасения6:9 Или: «вы на лучшем пути, на пути спасения»; или: «вы имеете благословения, которые сопровождают спасение».. 10Бог не может быть несправедлив. Он не забудет ни ваших трудов, ни вашей любви к Нему, которую вы проявили и продолжаете проявлять, служа святым. 11Однако мы хотим, чтобы каждый из вас проявлял такую же прилежность до конца, ради исполнения вашей надежды. 12Мы хотим, чтобы вы не ленились, а подражали тем, кто своей верой и терпением наследует обещанное.

Верность Бога Своим обещаниям

13Когда Бог давал обещание Аврааму, Он клялся Самим Собой, так как нет никого большего, кем Он мог бы клясться6:13 См. Быт. 22:16.. 14Он сказал: «Я непременно благословлю тебя и сделаю твое потомство многочисленным»6:14 См. Быт. 22:17.. 15И таким образом Авраам, терпеливо ожидая, получил обещанное.

16Люди клянутся чем-то большим, чем они сами; клятва подтверждает сказанное и кладет конец всякому спору. 17Так и Бог, когда хотел ясно показать наследникам Своего обещания, что намерения Его неизменны, то подтвердил их клятвой. 18И в этих двух неизменных вещах – в обещании и в клятве, которые у Бога не могут быть ложными, – мы, нашедшие у Него убежище и ухватившиеся за предстоящую нам надежду, получаем сильное ободрение. 19Эта надежда – крепкий и надежный якорь для нашей души. Она позволяет нам войти во внутреннюю часть святилища, за разделяющую его завесу6:19 Ср. Лев. 16:12., 20туда, куда вошел наш предшественник Иисус, став навеки Первосвященником по чину Мелхиседека6:19-20 См. Пс. 109:4; Евр. 9:1-12..