Ahebri 4 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 4:1-16

Mpumulo wa Anthu a Mulungu

1Popeza lonjezo lakuti tidzalowe mu mpumulo umene anatilonjeza lilipobe, tiyeni tisamale kuti pasakhale wina aliyense mwa inu wodzalephera kulowamo. 2Pakuti Uthenga Wabwino unalalikidwa kwa ife, monganso iwo aja; koma iwo sanapindule nawo uthengawo chifukwa anangomva koma osakhulupirira. 3Tsono ife amene takhulupirira talowa mu mpumulo, monga momwe Mulungu akunenera kuti,

“Ndili wokwiya ndinalumbira kuti,

‘Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.’ ”

Ananena zimenezi ngakhale anali atatsiriza kale ntchito yolenga dziko lapansi. 4Pena pake wayankhula za tsiku lachisanu ndi chiwiri mʼmawu awa: “Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, Mulungu anapumula ku ntchito zake zonse.” 5Pa ndime inonso akunena za zomwezo pamene akuti, “Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.”

6Popeza kwatsalabe kuti ena adzalowe mu mpumulowo, koma aja anayamba kumva Uthenga Wabwino sanalowe chifukwa cha kusamvera kwawo. 7Nʼchifukwa chake Mulungu anayikanso tsiku lina limene analitcha “Lero.” Patapita nthawi yayitali Iye anayankhula za tsiku lomweli kudzera mwa Davide, monga ndinanena kale kuti,

“Lero mukamva mawu ake,

musawumitse mitima yanu.”

8Ngati Yoswa akanalowetsa anthu mu mpumulo, Mulungu sakananena pambuyo pake za tsiku lina. 9Kotero tsono kwatsala mpumulo wa Sabata kwa anthu a Mulungu; 10Pakuti aliyense amene analowa mu mpumulo wa Mulungu anapuma pa ntchito zake, monga momwe Mulungu anachitira. 11Tiyeni tsono tiyesetse kulowa mu mpumulo, kuti pasapezeke wina aliyense wolephera potsatira chitsanzo chawo cha kusamvera.

12Paja Mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu. Ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse. Amalowa mpaka molumikizirana moyo ndi mzimu, ndiponso molumikizirana fundo ndi mafuta a mʼmafupa. Amaweruza malingaliro ndi zokhumba za mʼmitima. 13Palibe kanthu kobisika pamaso pa Mulungu. Zinthu zonse zili poyera ndi zovundukuka pamaso pa Iye amene tiyenera kumufotokozera zonse zimene tachita.

Yesu Mkulu wa Ansembe Wopambana

14Popeza kuti tili ndi Mkulu wa ansembe wopambana, amene analowa kale kumwamba, Yesu Mwana wa Mulungu, tiyeni tigwiritsitse chikhulupiriro chathu chimene timavomereza. 15Pakuti sitili ndi Mkulu wa ansembe amene sangathe kutimvera chifundo chifukwa cha zofowoka zathu. Koma tili naye amene anayesedwa mʼnjira zonse monga ife, koma sanachimwe. 16Tiyeni tsono tiyandikire ku mpando waufumu, wachisomo mopanda mantha, kuti tilandire chifundo ndi kupeza chisomo chotithandiza pa nthawi yeniyeni.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

希伯來書 4:1-16

信的人得享安息

1因此,上帝既然仍舊應許讓人進入祂的安息,我們就該戰戰兢兢,免得有人失去這福分。 2因為我們和他們一樣聽到了福音,只是他們聽了道後沒有憑信心領受,結果沒有得到益處。 3正如上帝曾說:

「我在憤怒中起誓說,

『他們絕不可進入我的安息。』」

但我們這些已經信的人能夠進入祂的安息。其實造物之工自創世以來就已經完成了, 4因為聖經論到第七日時說:「第七日,上帝歇了一切的工。」 5又說:「他們絕不可進入我的安息。」 6既然最終會有人進入安息,而那些從前聽過福音的人因為不信沒能進去, 7上帝就另定了一個日子,稱之為「今日」。正如多年後,祂藉著大衛說:

「你們今日若聽見祂的聲音,

不可心裡頑固。」

8如果當初約書亞已經讓他們得到了安息,上帝就不必另定一個日子了。 9這樣說來,必定另有一個安息日為上帝的子民存留,使他們可以真正安歇。 10因為人進入上帝的安息,就是歇了自己的工作,好像上帝歇了祂的工作一樣。 11因此,我們要竭力進入那安息,免得重蹈他們的覆轍,因不順服而倒斃。

12上帝的話有生命、有功效,鋒利無比,勝過一切兩刃的利劍,甚至能夠剌入並分開魂與靈、關節與骨髓,辨明人一切的思想和動機。 13受造物在上帝面前都無法隱藏,因為萬物都是赤裸裸地暴露在上帝眼前,我們必須向祂交帳。

大祭司耶穌

14我們既然有一位已經升上高天的尊貴大祭司——上帝的兒子耶穌,就應當持守我們所認定的信仰。 15因為我們這位大祭司並非不能體恤我們的軟弱,祂與我們一樣曾經面對各樣的試探,卻從來沒有犯罪。 16所以,讓我們坦然無懼地到祂賜恩的寶座前,好領受憐憫和恩典,作隨時的幫助。