Ahebri 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 3:1-19

Yesu ndi Wamkulu Kuposa Mose

1Nʼchifukwa chake abale oyera mtima, amenenso munayitanidwa ndi kumwamba, lingalirani za Yesu amene ndi Mtumwi ndi Mkulu wa ansembe wa chikhulupiriro chimene timavomereza. 2Iye anali wokhulupirika kwa Mulungu amene anamupatsa udindowo, monga momwe Mose anali wokhulupirika mʼnyumba yonse ya Mulungu. 3Yesu anapezeka woyenera kulandira ulemu waukulu kuposa Mose, monga momwemonso womanga nyumba amalandira ulemu waukulu kuposa nyumbayo. 4Pakuti nyumba iliyonse imamangidwa ndi munthu wina, koma amene anapanga zonse ndi Mulungu. 5Mose anali wokhulupirika monga mtumiki mʼnyumba yonse ya Mulungu, kuchitira umboni zimene zidzayankhulidwe mʼtsogolo. 6Koma Khristu ndi wokhulupirika monga mwana pa nyumba ya Mulungu. Ndipo ndife nyumba yake ngati tipitirire kulimbika mtima ndi kunyadira zomwe tikuyembekerazo.

Chenjezo pa Kusakhulupirira

7Tsono monga Mzimu Woyera akuti,

“Lero mukamva mawu ake,

8musawumitse mitima yanu

ngati munachitira pamene munawukira,

pa nthawi yoyesedwa mʼchipululu.

9Pamene makolo anu anandiputa ndi kundiyesa,

ndipo kwa zaka makumi anayi anaona zimene Ine ndinachita.

10Nʼchifukwa chake ndinawukwiyira mʼbadowo,

ndipo Ine ndinati, ‘Nthawi zonse mitima yawo imasochera,

ndipo iwo sadziwa njira zanga.’

11Kotero Ine ndinalumbira nditakwiya kuti,

‘Iwo sadzalowa mu mpumulo wanga.’ ”

12Abale samalani, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woyipa ndi wosakhulupirira, womulekanitsa ndi Mulungu wamoyo. 13Koma muzilimbikitsana tsiku ndi tsiku, ikanalipo nthawi imene imatchedwa kuti “Lero” kuti aliyense wa inu mtima wake usawumitsidwe ndi chinyengo cha tchimo. 14Pakuti timakhala anzake a Khristu, ngati tigwiritsitsa mpaka potsiriza chitsimikizo chimene tinali nacho pachiyambi. 15Monga kunanenedwa kuti,

“Lero ngati mumva mawu ake,

musawumitse mitima yanu

ngati momwe munachitira pamene munawukira.”

16Nanga amene anamva ndi kuwukira anali ndani? Kodi si onse amene Mose anawatulutsa mu Igupto? 17Nanga amene Mulungu anawakwiyira zaka makumi anayi anali ndani? Kodi si anthu amene anachimwa, amene mitembo yawo inatsala mʼchipululu muja? 18Nanga Mulungu ankanena za ndani kuti sadzalowa mu mpumulo wake? Pajatu ankanena za anthu amene sanamvere aja. 19Tsono ife tikuona kuti sanalowe chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

希伯來書 3:1-19

耶穌超越摩西

1因此,同蒙天召的聖潔的弟兄姊妹,你們應當仔細思想那位我們公認為特使和大祭司的耶穌。 2祂向委任祂的上帝盡忠,就好像摩西向上帝的全家盡忠一樣。 3然而祂卻比摩西配得更大的榮耀,因為建造房子的人當然比房子更尊貴。 4所有的房子都有建造者,但建造萬物的是上帝。 5摩西以僕人的身分向上帝的全家盡忠,為將來要宣告的事做見證。 6但基督是以兒子的身分忠心治理上帝的家。我們若堅強勇敢,持定引以為榮的盼望,我們就是祂的家了。

不可存剛硬的心

7因此,正如聖靈說:

「你們今天若聽見祂的聲音,

8不可心裡頑固,

像從前在曠野試探祂、悖逆祂一樣。

9當時,你們的祖先試我、探我,

觀看我的作為達四十年之久。

10所以,我向那世代的人發怒,

說,『他們總是執迷不悟,

不認識我的道路。』

11我就在憤怒中起誓說,

『他們絕不可進入我的安息。』」

12弟兄姊妹,要謹慎,免得你們當中有人心存惡念,不肯相信,背棄了永活的上帝。 13趁著還有今日,要天天互相勸勉,免得有人被罪迷惑,心裡變得剛硬。 14如果我們將起初的信念堅持到底,便在基督裡有份了。

15聖經上說:

「你們今日若聽見祂的聲音,

不可像從前那樣硬著心悖逆祂。」

16聽見祂的聲音卻又悖逆祂的是誰呢?不就是摩西埃及領出來的那些人嗎? 17四十年之久惹上帝發怒的是誰呢?不就是那些犯罪作惡並倒斃在曠野的人嗎? 18上帝起誓不准誰進入祂的安息呢?不就是那些不肯信從的人嗎? 19可見,他們不能進入上帝的安息是因為不信的緣故。