Ahebri 2 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 2:1-18

Kusamalira Chipulumutso

1Nʼchifukwa chake, ife tiyenera kusamalira kwambiri zimene tinamva, kuopa kuti pangʼono ndi pangʼono tingazitaye. 2Popeza uthenga umene unayankhulidwa kudzera mwa angelo unali okhazikika ndithu, choncho aliyense amene ananyozera ndi kusamvera analandira chilango choyenera. 3Nanga ife tidzapulumuka bwanji tikapanda kusamala chipulumutso chachikulu chotere? Ambuye ndiye anayamba kuyankhula za chipulumutsochi, kenaka amenenso anamvawo anatitsimikizira. 4Mulungu anachitiranso umboni pochita zizindikiro, zinthu zodabwitsa ndi zamphamvu zamitundumitundu ndi powapatsa mphatso za Mzimu Woyera monga mwachifuniro chake.

Yesu Wofanana ndi Abale ake

5Mulungu sanapereke kwa angelo ulamuliro wa dziko limene likubwerali, limene ife tikulinena. 6Koma palipo pena pamene wina anachitira umboni kuti,

“Kodi munthu ndani kuti muzimukumbukira,

kapena mwana wa munthu kuti muzimusamalira?

7Munamuchepetsa pangʼono kusiyana ndi angelo;

munamupatsa ulemerero ndi ulemu.

8Munamupatsa ulamuliro pa zinthu zonse.”

Poyika zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, Mulungu sanasiye kanthu kamene sikali mu ulamuliro wake. Koma nthawi ino sitikuona zinthu pansi pa ulamuliro wake. 9Koma tikuona Yesu, amene kwa kanthawi kochepa anamuchepetsa pangʼono kwa angelo, koma tsopano wavala ulemerero ndi ulemu chifukwa anamva zowawa za imfa, kuti mwachisomo cha Mulungu, Iye afere anthu onse.

10Mulungu amene analenga zinthu zonse ndipo zinthu zonse zilipo chifukwa cha Iye ndi mwa Iye, anachiona choyenera kubweretsa ana ake ambiri mu ulemerero. Kunali koyenera kudzera mʼnjira ya zowawa, kumusandutsa Yesu mtsogoleri wangwiro, woyenera kubweretsa chipulumutso chawo. 11Popeza iye amene ayeretsa ndi oyeresedwa onse ndi abanja limodzi. Nʼchifukwa chake Yesu sachita manyazi kuwatcha iwo abale ake. 12Iye akuti,

“Ine ndidzawuza abale anga za dzina lanu.

Ndidzakuyimbirani nyimbo zamatamando pamaso pa mpingo.”

13Ndiponso,

“Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.”

Ndiponso Iye akuti,

“Ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Mulungu wandipatsa.”

14Tsono popeza kuti anawo ndi anthu, okhala ndi mnofu ndi magazi, Yesu nayenso anakhala munthu ngati iwowo kuti kudzera mu imfa yake awononge Satana amene ali ndi mphamvu yodzetsa imfa. 15Pakuti ndi njira yokhayi imene Iye angamasule amene pa moyo wawo wonse anali ngati akapolo chifukwa choopa imfa. 16Pakuti tikudziwanso kuti sathandiza angelo, koma zidzukulu za Abrahamu. 17Chifukwa cha zimenezi, Iye anayenera kukhala wofanana ndi abale ake pa zonse, kuti akhale mkulu wa ansembe wachifundo ndi wokhulupirika potumikira Mulungu, kuti potero achotse machimo a anthu. 18Popeza Iye mwini anamva zowawa pamene anayesedwa, Iyeyo angathe kuthandiza amene akuyesedwanso.

Persian Contemporary Bible

عبرانيان 2:1-18

توجه به پيام نجاتبخش انجيل

1پس حال كه پی برديم عيسی مسيح دارای چه مقام والايی است، بايد به پيغام و كلامی كه شنيده‌ايم، به دقت توجه نماييم، مبادا ايمان خود را از دست بدهيم. 2زيرا اگر پيغام و كلامی كه بوسيلهٔ فرشتگان آورده شد، دارای اعتبار و لازم‌الاجرا بود، و هر كه از آن تخلف و نافرمانی می‌كرد، به حق مجازات می‌شد، 3چگونه امكان دارد كه ما از مجازات بگريزيم، اگر نسبت به چنين نجات عظيمی بی‌اعتنا باشيم؟ زيرا اين مژده را ابتدا عيسای خداوند اعلام نمود، و بعد كسانی كه آن را از دهان او شنيدند، آن را برای ما تائيد كردند.

4خدا نيز با علامات، كارهای شگفت‌انگيز، معجزات گوناگون و عطايايی كه روح‌القدس مطابق اراده خود می‌بخشد، صحت كلام ايشان را ثابت نمود.

فرزند خدا به شكل انسان درآمد

5به ياد داشته باشيد كه دنيای آينده كه از آن سخن می‌گوييم، بوسيلهٔ فرشتگان اداره نخواهد شد، بلكه مسيح آن را اداره خواهد كرد. 6زيرا داوود پيغمبر در كتاب زبور به خدا می‌گويد: «انسان چيست كه تا اين اندازه او را مورد توجه قرار می‌دهی؟ اين پسر انسان كيست كه تا اين حد او را سرافراز می‌گردانی؟ 7زيرا هر چند برای مدتی كوتاه او را پایینتر از فرشتگان قرار دادی، اما اكنون تاج جلال و افتخار را بر سر او گذارده‌ای، 8و همه چيز را تحت فرمان او درآورده‌ای.»

ما تا به حال نديده‌ايم كه همه چيز تحت فرمان انسان درآمده باشد؛ 9اما عيسی را می‌بينيم كه اندک زمانی پایینتر از فرشتگان قرار گرفت و اكنون در اثر فدا كردن جان خود در راه ما، خدا تاج جلال و افتخار را بر سر او گذاشته است. بلی، به سبب رحمت عظيم خدا، عيسی به جای تمام مردم جهان، طعم مرگ را چشيد. 10و اين درست و بجا بود كه خدا، همان خدايی كه همه چيز را برای جلال خود آفريد، اجازه دهد كه عيسی عذاب ببيند، زيرا با اين كار، بسياری از فرزندان خدا را به سوی جلال آسمان هدايت می‌نمايد. در واقع، عذابی كه عيسی كشيد، باعث شد او پيشوايی كامل گردد، پيشوايی كه می‌تواند ايشان را به سوی نجات رهبری نمايد.

11حال كه ما بوسيلهٔ عيسی، مقدس شده‌ايم، پدر او، پدر ما نيز محسوب می‌شود. به همين علت، عيسی عار ندارد كه ما را برادران خود بخواند؛ 12چنانكه در كتاب زبور نيز فرموده است: «دربارهٔ پدرم خدا، با برادرانم سخن خواهم گفت، و همگی با هم او را حمد و سپاس خواهيم گفت». 13در جای ديگر نيز فرموده است: «من با برادران خود، بر خدا توكل خواهم نمود.» همچنين در جای ديگر گفته است: «ببينيد، اين من و اين هم فرزندانی كه خدا به ما عطا فرموده است.»

14از آنجا كه اين فرزندان خدا، انسان هستند و دارای گوشت و خون می‌باشند، او نيز گوشت و خون شد و به شكل انسان درآمد؛ زيرا فقط با انسان شدن می‌توانست جانش را در راه ما فدا كند و بميرد، و با مرگ خود، قدرت شيطان را نابود سازد، شيطانی كه صاحب اختيار مرگ بود. 15تنها از اين راه بود كه می‌توانست آنانی را كه در تمام عمرشان در وحشت مرگ به سر می‌بردند و اسير ترس بودند، رهايی بخشد.

16همهٔ ما می‌دانيم كه او برای كمک به فرشتگان نيامد، بلكه به اين جهان آمد تا انسانهايی را كه به گفتهٔ كتاب آسمانی، از «نسل ابراهيم» می‌باشند، دستگيری نمايد. 17به همين جهت لازم بود كه او نيز از هر لحاظ مانند برادران خود گردد تا در حضور خدا، برای انسانها كاهن اعظمی دلسوز و وفادار باشد و به هنگام كفارهٔ گناهان، بتواند در همان حال كه نسبت به انسان رحيم و كريم می‌باشد، نسبت به خدا نيز وفادار بماند. 18زيرا از آنجا كه او خود عذاب ديد و وسوسه شد، قادر است درد انسان را به هنگام عذاب و وسوسه درک كند و به كمک او بشتابد.