Ahebri 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 1:1-14

Khristu Mwana wa Mulungu Aposa Angelo

1Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri. 2Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. 3Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero. 4Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.

5Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,

“Iwe ndiwe mwana wanga;

Ine lero ndakhala Atate ako.”

Kapena kunenanso kuti,

“Ine ndidzakhala abambo ake;

iye adzakhala mwana wanga.”

6Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,

“Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”

7Iye ponena za angelo akuti,

“Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo,

amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”

8Koma za Mwana wake akuti,

“Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya,

ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu.

9Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu

pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”

10Mulungu akutinso,

“Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi;

ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.

11Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.

Izo zidzatha ngati zovala.

12Mudzazipindapinda ngati chofunda;

ndipo zidzasinthidwa ngati chovala.

Koma Inu simudzasintha,

ndipo zaka zanu sizidzatha.”

13Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti,

“Khala kudzanja langa lamanja

mpaka nditapanga adani ako

kukhale chopondapo mapazi ako.”

14Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?

Persian Contemporary Bible

عبرانيان 1:1-14

عيسی مسيح فرزند خداست

1در زمانهای گذشته، خدا بوسيلهٔ پيامبران، اراده و مشيت خود را به تدریج بر اجداد ما آشكار می‌فرمود. او از راههای گوناگون، گاه در خواب و رؤيا، گاه حتی روبرو، با پيامبران سخن می‌گفت. 2اما در اين ايام آخر، او توسط فرزندش با ما سخن گفت. خدا در واقع، اختيار همه چيز را به فرزند خود سپرده و جهان و تمام موجودات را به‌وسیله او آفريده است. 3فرزند خدا، منعكس كننده جلال خدا و مظهر دقيق وجود اوست. او با كلام نيرومند خود تمام عالم هستی را اداره می‌كند. او به اين جهان آمد تا جانش را فدا كند و ما را پاک ساخته، گذشتهٔ گناه‌آلود ما را محو نمايد؛ پس از آن، در بالاترين مكان افتخار، يعنی به دست راست خدای متعال نشست.

برتری مسيح بر فرشتگان

4به اين طريق، او از فرشته‌ها برتر گرديد. نام او نيز گواه بر اين برتری است: «پسر خدا!» اين نامی است كه خدای پدر به او داده، و از نام و لقب همه فرشته‌ها بالاتر است؛ 5زيرا خدا خطاب به عيسی فرمود: «تو پسر من هستی؛ امروز اين نام را با تمام افتخاراتش به تو می‌بخشم.» اما دربارهٔ هيچيک از فرشتگان چنين نگفت. در جای ديگری از كتاب آسمانی، خدا فرمود: «من پدر او هستم، و او پسر من است.» 6همچنين، در جای ديگر، هنگامی كه فرزند ارشد او به جهان می‌آمد، فرمود: «همهٔ فرشتگان خدا او را پرستش نمايند!»

7خدا دربارهٔ فرشتگان می‌فرمايد: «همچون باد، به سرعت پيغام می‌برند، و چون شعله‌های آتش، با شور و حرارت خدمت می‌كنند.»

8اما دربارهٔ فرزندش می‌گويد: «ای خدا، سلطنت تو تا ابد برقرار است؛ اساس حكومت تو، بر عدل و راستی است؛ 9راستی را دوست می‌داری، و از ناراستی تنفر داری. بنابراين، خدا، يعنی خدای تو، بيش از هر کس ديگر تو را از شادی لبريز كرده است.»

10خدا همچنين او را «خداوند» ناميده است. از اين جهت در كتاب آسمانی آمده است: «خداوندا، تو در ابتدا زمين را آفريدی، و آسمانها ساختهٔ دستهای توست. 11آنها نيست و نابود خواهند شد، اما تو تا ابد باقی هستی. آنها همچون لباسی كهنه، پوسيده و مندرس خواهند شد؛ 12روزی آنها را در هم خواهی پيچيد و تغيير خواهی داد. اما تو هرگز تغيير نخواهی يافت و سالهای عمر تو پايان نخواهد پذيرفت.»

13خدا به فرزندش فرمود: «در كنار من بنشين تا دشمنانت را زير پايهايت بيفكنم.» اما خطاب به هيچ فرشته‌ای چنين نگفت. 14زيرا فرشته‌ها فقط روح‌هايی خدمتگزار هستند، و برای كمک و مراقبت از كسانی فرستاده می‌شوند كه مايلند نجات الهی را دريافت نمايند.