Ahebri 12 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 12:1-29

Yesu Chitsanzo Chathu

1Tsono popeza ifenso tazunguliridwa ndi gulu lalikulu la mboni, tiyeni titaye chilichonse chimene chimatitchinga, makamaka tchimo limene limatikola mosavuta, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu. 2Tiyeni tiyangʼanitsitse Yesu, amene ndi woyamba ndi wotsiriza wa chikhulupiriro chathu. Chifukwa cha chimwemwe chimene chimamudikira anapirira zowawa zapamtanda. Iye ananyoza manyazi a imfa yotere ndipo tsopano akukhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu. 3Muzilingalira za Iye amene anapirira udani waukulu chotere wochokera kwa anthu ochimwa, kuti musafowoke ndi kutaya mtima. 4Polimbana ndi uchimo, simunafike mpaka pokhetsa magazi.

Mulungu Amalanga Ana ake

5Kodi mwayiwala mawu olimbitsa mtima aja, amene Mulungu anayankhula kwa inu ngati ana ake? Mawuwo ndi awa:

“Mwana wanga, usapeputse kulanga kwa Ambuye

ndipo usataye mtima pamene akukudzudzula.

6Chifukwa Ambuye amadzudzula amene amawakonda

ndipo amalanga aliyense amene amamulandira.”

7Pamene mukupirira masautso monga chilango, Mulungu achitira inu monga ana ake. Kodi ndi mwana wotani amene abambo ake samulanga? 8Ngati inu simulangidwa, komatu aliyense amalangidwa, ndiye kuti sindinu ana enieni koma amʼchigololo. 9Komanso, tonsefe tinali ndi abambo athu otibala amene amatilanga ndipo timawapatsa ulemu. Nanga kodi sitidzagonjera Atate a mizimu yathu kuti tikhale ndi moyo? 10Abambo athu ankatilanga kwa kanthawi kochepa monga amaonera kufunika kwake, koma Mulungu amatilanga kuti tipindule, kuti tikhale oyera mtima. 11Palibe chilango chimene chimaoneka kuti ndi chabwino pa nthawiyo, komatu chowawa. Koma pambuyo pake, chimabweretsa chipatso chachilungamo ndi mtendere kwa iwo amene aleredwa mwa njira imeneyi.

12Nʼchifukwa chake limbitsani manja anu otopa ndi mawondo anu ogowoka. 13Muziyenda mʼnjira zowongoka, kuti iwo amene akukutsatirani ngakhale ndi olumala ndi ofowoka asapunthwe ndi kugwa koma adzilimbikitsidwa.

Chenjezo kwa Okana Mulungu

14Yesetsani kukhala pa mtendere ndi anthu onse ndi kukhala oyera mtima, pakuti popanda chiyero palibe ndi mmodzi yemwe adzaona Ambuye. 15Yangʼanitsitsani kuti wina aliyense asachiphonye chisomo cha Mulungu ndiponso kuti pasaphuke muzu wamkwiyo umene udzabweretsa mavuto ndi kudetsa ambiri. 16Yangʼanitsitsani kuti pasakhale wina wachigololo. Kapena wosapembedza ngati Esau, amene chifukwa cha chakudya cha kamodzi kokha anagulitsa ukulu wake. 17Monga inu mukudziwa, pambuyo pake pamene anafuna kuti adalitsidwe anakanidwa. Sanapezenso mpata woti asinthe maganizo, ngakhale anafuna madalitsowo ndi misozi.

18Inu simunafike ku phiri limene mungathe kulikhudza, loyaka moto wa mdima bii, la mphepo yamkuntho; 19limene pali kulira kwa lipenga, ndiponso kumveka kwa mawu. Anthu amene amamva mawuwo anapempha kuti asawayankhulenso mawu ena. 20Iwo anachita mantha ndi lamulo lija lakuti, “Ngakhale nyama ikangokhudza phirilo, iphedwe ndi miyala.” 21Maonekedwenso a Mose anali woopsa kwambiri, ngakhale Mose yemwe anati, “Ine ndinachita mantha ndi kunjenjemera.”

22Koma inu mwafika ku Phiri la Ziyoni, ku mzinda wa Mulungu wamoyo, Yerusalemu wakumwamba. Mwafika mu msonkhano wa angelo osangalala osawerengeka. 23Mwafika mu mpingo wa ana oyamba kubadwa, amene mayina awo analembedwa kumwamba. Inu mwafika kwa Mulungu, woweruza anthu onse, ndiponso kwa mizimu ya anthu olungama ndi osandutsidwa kukhala angwiro. 24Kwa Yesu mʼkhalapakati wa pangano latsopano, ndiponso mwafika ku magazi owazidwa amene amayankhula mawu abwino kuposa magazi a Abele.

25Chenjerani kuti musakane kumvera amene akuyankhula nanu. Anthu amene anakana kumvera iye amene anawachenjeza uja pa dziko lapansi pano, sanapulumuke ku chilango ayi, nanga tsono ife tidzapulumuka bwanji ngati tikufulatira wotichenjeza wochokera kumwamba? 26Pa nthawiyo mawu ake anagwedeza dziko lapansi, koma tsopano Iye walonjeza kuti, “Kamodzi kenanso ndidzagwedeza osati dziko lapansi lokha komanso thambo.” 27Mawu akuti, “Kamodzi kenanso,” akuonetsa kuchotsedwa kwa zimene zitha kugwedezeka, zonse zolengedwa, kotero kuti zimene sizingatheke kugwedezeka zitsale.

28Popeza tikulandira ufumu umene sungagwedezeke, tiyeni tikhale oyamika ndi kupembedza Mulungu movomerezeka ndi mwaulemu ndi mantha. 29Pakuti Mulungu wathu ndi moto wonyeketsa.

New Russian Translation

Евреям 12:1-29

Бог воспитывает нас

1Итак, нас окружает целое облако свидетелей! Поэтому давайте сбросим с себя все, что мешает нам бежать, а также грех, легко запутывающий нас в свои сети, и будем терпеливо преодолевать отмеренную нам дистанцию. 2Будем неотрывно смотреть на Иисуса. От начала до конца наша вера зависит от Него. Он ради предстоящей радости претерпел смерть на кресте, пренебрегши позор, и сейчас сидит по правую сторону от Божьего престола12:2 См. Пс. 109:1.. 3Подумайте о Нем, испытавшем такую вражду со стороны грешников, и это поможет вам не изнемочь душою и не потерять присутствия духа.

4Вам еще не приходилось сражаться с грехом до крови. 5Вы забыли слова ободрения, обращенные к вам как к сыновьям:

«Сын мой, не отвергай наказания Господнего,

не теряй присутствия духа, когда Он тебя обличает,

6ведь Господь наказывает того, кого любит,

и бьет каждого, кого принимает как сына»12:5-6 См. Прит. 3:11-12..

7Переносите страдания как часть вашего воспитания. Бог относится к вам как к сыновьям. Разве есть такой сын, которого бы отец не наказывал? 8Если вы не бывали наказаны (а каждый подвергается наказанию), то вы незаконные дети, а не подлинные сыновья. 9У нас у всех были земные отцы, которые наказывали нас, и мы уважали их. Насколько же больше мы должны быть послушны Отцу наших духов, ведь это послушание дает нам жизнь! 10Наши отцы воспитывали нас некоторое время, и так, как им это казалось правильным, но Бог воспитывает нас ради нашего блага, чтобы нам стать участниками Его святости. 11Любое наказание кажется нам скорее причиняющим боль, чем несущим радость. Но впоследствии те, кто был научен наказанием, пожинают урожай праведности и мира.

12Поэтому укрепите опустившиеся руки и дрожащие колени12:12 См. Ис. 35:3.. 13Идите по прямому пути12:13 См. Прит. 4:26., чтобы тому, кто хромает, не покалечиться больше, но опять стать здоровым.

Призыв не отвергать Бога

14Старайтесь жить в мире со всеми людьми и быть святыми: без святости никто не увидит Господа. 15Смотрите, чтобы никто из вас не был лишен благодати Божьей, и чтобы никто не причинил бы вам вреда, подобно горькому корню, который пророс среди вас, и чтобы им не осквернились многие12:15 См. Втор. 29:18.. 16Смотрите, чтобы никто из вас не предавался распутству и не был таким далеким от Бога, как Исав, который за одну миску еды продал свои права старшего сына12:16 См. Быт. 25:29-34. Права старшего сына включали в себя двойное наследство (см. Втор. 21:15-17) и особое отцовское благословение (см. Быт. 27:1-40).. 17Вы знаете, что потом он хотел унаследовать благословение, но был отвергнут. Хотя он горько плакал, было слишком поздно для раскаяний. 18А ведь вы подошли не к горе Синай, к которой можно притронуться и которая пылает огнем, не ко тьме, не к мраку и не к буре. 19Вы пришли не на звук трубы и не на голос, говорящий такие слова, что слушающие просили о том, чтобы больше он не говорил им. 20Люди были не в силах вынести то, что им было повелено: «Если и животное прикоснется к этой горе, оно должно быть побито камнями». 21Это было так ужасно, что даже Моисей сказал: «Я в страхе и трепете»12:18-21 См. Исх. 19:9-25; Втор. 4:11-12; 5:22-26; 9:19..

22Нет! Вы пришли к горе Сион, к городу живого Бога, к Небесному Иерусалиму. Вы пришли к тысячам ангелов, собранным на радостное торжество. 23Вы пришли в собрание первенцев12:23 Собрание первенцев – имеются в виду все верующие, последователи Иисуса Христа. Первенцы занимали важное место в семье и принимали особое благословение родителей. Верующие в Иисуса имеют то же положение в глазах Бога., чьи имена записаны на небесах. Вы пришли к Богу, Судье всех людей, и к духам праведников, ставших совершенными. 24Вы пришли к Иисусу, посреднику нового завета, и к окропляющей крови, которая говорит лучше крови Авеля12:24 См. Быт. 4:10; Евр. 9:13-14..

25Смотрите, не отвергайте Того, Кто к вам обращается. Если те, которые отказались слушать говорящего на земле, не избежали своего наказания, то тем более не избежим его и мы, к которым Бог обращается с небес. 26Тогда Его голос потрясал землю, но сейчас Он обещает: «Я еще раз сотрясу землю, и не только землю, но и небеса»12:26 См. Агг. 2:6.. 27Слова «еще раз» говорят о том, что все, что может быть сотрясено, все сотворенное, временное, исчезнет, останется только то, что непоколебимо.

28Поэтому, получая Царство, которое не может быть поколеблено, будем благодарны и в благодарности будем поклоняться Богу так, как Ему приятно, в почтении и страхе, 29потому что наш Бог – это пожирающий огонь12:29 См. Втор. 4:24; 9:3; Ис. 33:14..