Agalatiya 6 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Agalatiya 6:1-18

Kuchita Zabwino kwa Onse

1Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe. 2Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu. 3Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha. 4Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake, 5pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.

6Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.

7Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa. 8Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. 9Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa. 10Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.

Osati Mdulidwe koma Kulengedwa Mwatsopano

11Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.

12Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu. 13Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo. 14Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi. 15Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano. 16Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.

17Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.

18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.

New Serbian Translation

Галатима 6:1-18

1Браћо, ако се неко затекне у каквом преступу, ви духовни исправите таквог у духу кроткости, пазећи да и сами не подлегнете искушењу. 2Носите бремена један другога, па ћете тако испунити Христов закон. 3Јер ако неко мисли да је нешто, а није ништа, самога себе вара. 4Свако нека преиспита своје понашање, не поредећи се са другима. Тада нека се хвали пред собом. 5Јер свако треба да носи терет одговорности за себе.

6Ко прима поуку из Божије речи, нека сва добра дели са својим учитељем. 7Не варајте се; Бог се не да исмејавати. Јер шта ко сеје, то ће и жети. 8Наиме, ко сеје у своју грешну природу, од грешне природе ће пожњети пропаст. А ко сеје у Дух, од Духа ће пожњети вечни живот. 9Нека вам не дојади да чините добро, јер ћемо у своје време пожњети жетву, ако не малакшемо. 10Стога, дакле, док још имамо времена, чинимо добро свим људима, а поготову своме роду по вери.

Закључак и поздрав

11Видите коликим вам словима својеручно пишем. 12Они који хоће да се хвале сами собом, терају вас да се обрежете, само да не би били прогоњени због Христовог крста. 13Наиме, чак ни они који су обрезани, не извршавају Закон, него само хоће да се хвале тиме што сте се на њихов наговор обрезали. 14А од мене далеко било да се хвалим нечим другим осим крстом нашега Господа Исуса Христа, чијим је посредством свет умро за мене, и ја за свет. 15Јер, није важно ни обрезање ни необрезање, него ново створење. 16А свима који се држе овог правила, мир и милосрђе, заједно са свим Божијим Израиљем. 17Убудуће нека ме нико не узнемирава, јер ја на свом телу носим ознаке6,17 Ознаке се односе на ране, или ожиљке на телу апостола Павла, које је задобио проповедајући еванђеље. Исусове. 18Браћо, милост Господа нашега Исуса Христа нека буде са вашим духом! Амин.