Aefeso 1 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 1:1-23

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu.

Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:

2Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Madalitso Auzimu mwa Khristu

3Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu. 4Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake, 5Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake. 6Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda. 7Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu 8chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso, 9Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake. 10Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.

11Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake, 12nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake. 13Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza. 14Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.

Kuyamika ndi Kupemphera

15Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse, 16ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga. 17Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni. 18Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima. 19Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija 20imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba. 21Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. 22Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo, 23umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.

New Serbian Translation

Ефесцима 1:1-23

1Од Павла, вољом Божијом изабраног за апостола Христа Исуса, светима у Ефесу, вернима у Христу Исусу:

2Милост вам и мир од Бога, Оца нашега, и Господа Исуса Христа.

3Нека је благословен Бог, Отац Господа нашег Исуса Христа, који нас је у Христу благословио сваким духовним благословом на небесима. 4У њему нас је изабрао пре постанка света, да будемо свети и без мане пред њим. Он нас је у љубави 5предодредио, благонаклоношћу своје воље, да постанемо његова деца посредством Исуса Христа, 6и да хвалимо његову славну милост коју нам је даровао у Љубљеноме. 7У њему имамо откупљење, опроштење преступа посредством његове крви, што показује богатство милости. 8Њу је Бог изобилно излио на нас, заједно са свом мудрошћу и разумевањем. 9Својом благонаклоношћу нам је обзнанио тајну своје воље, коју је по свом науму унапред одредио у њему. 10Овај наум, који ће се остварити у право време, ујединиће све што је на небесима и на земљи с Христом као главом.

11У њему смо изабрани, пошто смо предодређени намером Бога који све чини у складу с одлуком своје воље, 12да хвалимо његову славу – ми који смо се претходно поуздали у Христа. 13Чувши истиниту поруку – Радосну вест о вашем спасењу, ви сте поверовали у Христа, а Бог је утиснуо свој печат на вас, тако што вам је дао обећаног Духа Светог. 14Он је залог добара која нас очекују, јемство да ће Бог ослободити свој народ. Величајмо зато његову славу!

Павлова молитва

15Стога, чувши за вашу веру у Господа Исуса и за вашу љубав према свим светима, 16непрестано захваљујем Богу за вас. Сећам вас се у својим молитвама, молећи се 17Богу Господа нашег Исуса Христа, славноме Оцу, да вам да Духа мудрости и откривења којим ћете га упознати; 18да вам Бог просветли очи срца да бисте видели у чему се састоји нада на коју сте позвани, како је величанствено богатство добара које је он припремио светима, 19и како је неизмерно велика његова сила према нама који верујемо. Његова сила одговара делотворности оне силне моћи 20коју је показао на Христу, када га је подигао из мртвих и поставио себи с десне стране на небесима 21изнад свих поглаварстава и власти, сила, господстава, и изнад сваког имена које се зазива, не само на овом свету, него и у будућем. 22Бог је све покорио под његове ноге и поставио га над свиме, за главу Цркве. 23Она је његово тело, пунина онога који све испуњава у свему.