Agalatiya 6 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Agalatiya 6:1-18

Kuchita Zabwino kwa Onse

1Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe. 2Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu. 3Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha. 4Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake, 5pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.

6Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.

7Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa. 8Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. 9Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa. 10Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.

Osati Mdulidwe koma Kulengedwa Mwatsopano

11Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.

12Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu. 13Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo. 14Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi. 15Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano. 16Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.

17Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.

18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.

La Bible du Semeur

Galates 6:1-18

Travailler au bien de tous

1Frères et sœurs, si quelqu’un s’est laissé surprendre par quelque faute6.1 Autre traduction : si quelqu’un vient à être surpris en faute., vous qui vivez selon l’Esprit, ramenez-le dans le droit chemin avec un esprit de douceur. Et toi qui interviens, fais attention de ne pas te laisser toi-même tenter.

2Aidez-vous les uns les autres à porter vos fardeaux. De cette manière, vous accomplirez la loi de Christ.

3Celui qui s’imagine être quelqu’un d’important – alors qu’en fait il n’est rien – s’abuse lui-même. 4Que chacun examine ce qu’il accomplit lui-même. S’il y découvre quelque aspect louable, alors il pourra en éprouver de la fierté par rapport à lui-même et non pas par comparaison avec les autres, 5car chacun aura à répondre pour lui-même de ses propres actions.

6Que celui à qui l’on enseigne la Parole donne une part de tous ses biens à celui qui l’enseigne.

7Ne vous faites pas d’illusions : Dieu ne se laisse pas traiter avec mépris. On récolte ce que l’on a semé. 8Celui qui sème pour satisfaire ses propres désirs d’homme livré à lui-même récoltera ce que produit cet homme, c’est-à-dire la corruption. Mais celui qui sème pour l’Esprit moissonnera ce que produit l’Esprit : la vie éternelle.

9Faisons le bien sans nous laisser gagner par le découragement. Car si nous ne relâchons pas nos efforts, nous récolterons au bon moment.

10Ainsi donc, tant que nous en avons l’occasion, faisons du bien à tout le monde, et en premier lieu à ceux qui appartiennent à la famille des croyants.

Derniers avertissements et salutation

11Vous remarquez ces grandes lettres ; c’est bien de ma propre main que je vous écris. 12Ceux qui vous imposent la circoncision sont des gens qui veulent faire bonne figure devant les hommes. Ils n’ont qu’un seul but : éviter d’être persécutés à cause de la mort de Christ sur la croix6.12 Prêcher la circoncision mettait à l’abri de la persécution à la fois des Juifs et des Romains (puisque le judaïsme était une « religion licite »)..

13Car ceux qui pratiquent la circoncision, n’observent pas la Loi, eux non plus. S’ils veulent vous faire circoncire, c’est pour pouvoir se vanter de vous avoir imposé cette marque dans votre corps.

14En ce qui me concerne, je ne veux à aucun prix placer ma fierté ailleurs que dans la mort de notre Seigneur Jésus-Christ sur la croix. Par elle, en effet, le monde dominé par le mal a été crucifié pour moi, de même que moi je l’ai été pour ce monde. 15Peu importe d’être circoncis ou non. Ce qui compte, c’est la nouvelle création6.15 Autre traduction : c’est d’être une nouvelle créature..

16Que la paix et la compassion de Dieu soient accordées à tous ceux qui suivent cette règle de vie, et à l’Israël de Dieu.

17Désormais, que personne ne me cause plus de peine, car je porte sur mon corps les cicatrices des blessures que j’ai reçues pour la cause de Jésus.

18Chers frères et sœurs, que la grâce de notre Seigneur Jésus-Christ soit avec vous tous.

Amen.