Aefeso 1 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 1:1-23

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu.

Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:

2Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Madalitso Auzimu mwa Khristu

3Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu. 4Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake, 5Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake. 6Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda. 7Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu 8chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso, 9Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake. 10Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.

11Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake, 12nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake. 13Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza. 14Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.

Kuyamika ndi Kupemphera

15Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse, 16ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga. 17Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni. 18Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima. 19Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija 20imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba. 21Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. 22Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo, 23umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.

La Bible du Semeur

Ephésiens 1:1-23

Salutation

1Paul, apôtre de Jésus-Christ par la volonté de Dieu, salue ceux qui [à Ephèse1.1 Les mots : à Ephèse sont absents de plusieurs manuscrits.] font partie du peuple saint, et croient en Jésus-Christ.

2Que la grâce et la paix vous soient accordées par Dieu notre Père et par le Seigneur Jésus-Christ.

Le salut en Christ

La grâce de Dieu en Christ

3Béni soit Dieu,

le Père de notre Seigneur

Jésus-Christ,

car il nous a comblés

de toute bénédiction de l’Esprit

dans le monde céleste

en raison de notre union avec Christ.

4En lui,

bien avant de poser

les fondations du monde,

il nous avait choisis

pour que nous soyons saints

et sans reproche devant lui.

Puisqu’il nous a aimés,

5il nous a destinés d’avance

à être ses enfants

qu’il voulait adopter

par Jésus-Christ.

Voilà ce que, dans sa bonté,

il a voulu pour nous

6afin que nous célébrions

la gloire de sa grâce

qu’il nous a accordée

en son Fils bien-aimé.

7En Christ,

parce qu’il s’est offert en sacrifice,

nous avons obtenu la délivrance,

le pardon de nos fautes.

Dieu a ainsi manifesté sa grâce

dans toute sa richesse,

8et il l’a répandue sur nous

avec surabondance,

en nous donnant pleine sagesse

et pleine intelligence,

9nous ayant fait connaître

le secret de son plan.

Ce plan, il l’a fixé d’avance,

dans sa bonté,

en Christ,

10pour conduire les temps

vers l’accomplissement.

Selon ce plan,

tout ce qui est au ciel

et tout ce qui est sur la terre

doit être harmonieusement réuni1.10 Paul emploie ici un verbe qui signifie résumer, récapituler. Il est difficile de savoir ce qu’il voulait dire exactement. Certains traduisent : doit être restauré. D’autres comprennent : doit être réuni sous le gouvernement de Christ.

en Christ.

11Et c’est aussi en Christ

qu’il nous a accordé

notre part d’héritage1.11 Autre traduction : que nous sommes devenus sa possession.

conformément à ce qu’avait fixé

celui qui met en œuvre toutes choses,

selon l’intention qui inspire

sa décision.

Ainsi, nous avons été destinés d’avance

12à célébrer sa gloire

nous qui, les tout premiers,

avons placé notre espérance

dans le Messie.

13Et en Christ, vous aussi,

vous avez entendu

le message de vérité,

cet Evangile

qui vous apportait le salut ;

oui, c’est aussi en Christ

que vous qui avez cru,

vous avez obtenu de Dieu

l’Esprit Saint qu’il avait promis

et par lequel

il vous a marqués de son sceau1.13 Le sceau apposé sur une marchandise marquait le changement de propriétaire.

en signe que vous lui appartenez.

14Cet Esprit constitue

l’acompte de notre héritage

en attendant la délivrance

du peuple que Dieu s’est acquis1.14 Autre traduction : la délivrance par laquelle nous entrerons en possession de notre héritage..

Ainsi tout aboutit

à célébrer sa gloire.

Prière de Paul pour les Ephésiens

15Pour toutes ces raisons, moi aussi, après avoir entendu parler de votre foi au Seigneur Jésus et de votre amour pour tous les membres du peuple saint, 16je ne cesse de dire ma reconnaissance à Dieu à votre sujet quand je fais mention de vous dans mes prières.

17Je demande que le Dieu de notre Seigneur Jésus-Christ, le Père qui possède la gloire, vous donne, par son Esprit, sagesse et révélation, pour que vous le connaissiez ; 18qu’il illumine ainsi votre intelligence afin que vous compreniez en quoi consiste l’espérance à laquelle vous avez été appelés, quelle est la glorieuse richesse de l’héritage que Dieu vous fera partager avec les membres du peuple saint, 19et quelle est l’extraordinaire grandeur de la puissance qu’il met en œuvre en notre faveur, à nous qui plaçons notre confiance en lui. Cette puissance, en effet, il l’a déployée dans toute sa force 20en la faisant agir en Christ lorsqu’il l’a ressuscité et l’a fait siéger à sa droite1.20 Ps 110.1., dans le monde céleste. 21Là, Christ est placé bien au-dessus de toute Autorité, de toute Puissance, de toute Domination et de toute Souveraineté1.21 Ces expressions se rapportent à des êtres surnaturels (angéliques ou démoniaques) auxquels les erreurs que certains répandaient dans les Eglises d’Asie Mineure donnaient une grande importance (voir 3.10 ; Col 1.16 ; 2.15). : au-dessus de tout nom qui puisse être cité, non seulement dans le monde présent, mais aussi dans le monde à venir. 22Dieu a tout placé sous ses pieds1.22 Voir Ps 8.7., et Christ qui domine toutes choses, il l’a donné pour chef à l’Eglise 23qui est son corps, lui en qui habite la plénitude du Dieu qui remplit tout en tous1.23 Autre traduction : à l’Eglise 23 qui est son corps, où se manifeste pleinement celui qui remplit tout en tous (cf. 3.19)..