Agalatiya 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Agalatiya 3:1-29

Chikhulupiriro Kapena Ntchito za Lamulo

1Agalatiya opusa inu, anakulodzani ndani? Tinamuonetsa poyera pamaso panu Yesu Khristu monga wopachikidwa pa mtanda. 2Ine ndikufuna ndiphunzire kuchokera kwa inu chinthu chimodzi ichi: Kodi munalandira Mzimu pochita ntchito za lamulo, kapena pokhulupirira zimene munamva? 3Kani ndinu opusa chotere? Inu mutayamba ndi Mzimu, kodi mukufuna kutsiriza ndi ntchito zathupi? 4Kodi munavutika kwambiri pachabe, ngati kunali kwachabedi? 5Kodi Mulungu amene anakupatsani Mzimu wake ndi kuchita zodabwitsa pakati panu, amachita zimenezi chifukwa mumachita ntchito za lamulo kapena chifukwa mumakhulupirira zimene munamva? 6Nʼchimodzimodzinso Abrahamu, “Iye anakhulupirira Mulungu, ndipo Mulungu anamutenga kukhala wolungama.”

7Tsono zindikirani kuti amene akhulupirira, ndi ana a Abrahamu. 8Malemba anaonetseratu kuti Mulungu adzalungamitsa anthu a mitundu ina mwachikhulupiriro, ndipo ananeneratu Uthenga Wabwino kwa Abrahamu kuti, “Mitundu yonse ya anthu idzadalitsika kudzera mwa iwe.” 9Choncho iwo amene ali ndi chikhulupiriro ndi odalitsidwa pamodzi ndi Abrahamu, munthu wachikhulupiriro.

10Onse amene amadalira ntchito za lamulo ndi otembereredwa, pakuti zalembedwa mʼBuku la Malamulo kuti, “Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita zonse zimene zalembedwa mʼBuku la Malamulo.” 11Chodziwikiratu nʼchakuti palibe amene amalungamitsidwa pamaso pa Mulungu ndi lamulo, chifukwa, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.” 12Koma chikhulupiriro si Malamulo, chifukwa Malemba akuti, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.” 13Khristu anatiwombola ku temberero la lamulo pokhala temberero mʼmalo mwathu, pakuti analemba kuti, “Aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa.” 14Iye anatiwombola ife ndi cholinga chakuti madalitso woperekedwa kwa Abrahamu abwere kwa anthu a mitundu ina kudzera mwa Khristu Yesu, kuti ndi chikhulupiriro tilandire lonjezo la Mzimu.

Lamulo ndi Lonjezo

15Abale, ndiloleni ndipereke chitsanzo cha zochitika mʼmoyo wa tsiku ndi tsiku. Pangano likakhazikitsidwa palibe amene angachotsepo kapena kuwonjezerapo, choncho ndi chimodzimodzi pa nkhani iyi. 16Malonjezo awa anaperekedwa kwa Abrahamu ndi kwa mbewu yake. Malemba sakunena kuti, “kwa mbewu zake,” kutanthauza anthu ambiri, koma, “kwa mbewu yako,” kutanthauza munthu mmodzi, amene ndi Khristu. 17Chimene ndikutanthauza ine ndi ichi: Malamulo amene anabwera patatha zaka 430, sangathetse pangano limene linakhazikitsidwa kale ndi Mulungu ndi kuliwononga lonjezolo. 18Ngati madalitso athu akudalira ntchito za lamulo ndiye kuti madalitsowo sakupatsidwa chifukwa cha lonjezo. Koma Mulungu mwachisomo chake anadalitsa Abrahamu kudzera mu lonjezo.

19Nanga tsono cholinga cha lamulo chinali chiyani? Linaperekedwa chifukwa cha zolakwa mpaka itafika mbewu imene lonjezo limanena. Malamulowo anaperekedwa ndi angelo kudzera mwa mʼkhalapakati. 20Ngakhale zili chomwecho, mʼkhalapakati sayimira mbali imodzi yokha, koma Mulungu ndi mmodzi.

21Kodi ndiye kuti lamulo limatsutsana ndi malonjezo a Mulungu? Ayi. Nʼkosatheka! Pakuti ngati tikanapatsidwa malamulo opatsa moyo ndiye kuti mwa lamulo tikanakhala olungama. 22Koma Malemba akunenetsa kuti dziko lonse lili mu ulamuliro wauchimo, kuti mwachikhulupiriro mwa Yesu Khristu, chimene chinalonjezedwa chiperekedwe kwa amene akhulupirira.

23Chikhulupiriro ichi chisanabwere, ife tinali mʼndende ya lamulo, otsekeredwa mpaka pamene chikhulupiriro chikanavumbulutsidwa. 24Choncho lamulo linayikidwa kukhala lotiyangʼanira kuti lititsogolere kwa Khristu kuti tilungamitsidwe mwachikhulupiriro. 25Tsopano pakuti chikhulupiriro chabwera, ife sitilinso mu ulamuliro wa lamulo.

Ana a Mulungu

26Nonse ndinu ana a Mulungu kudzera mʼchikhulupiriro mwa Khristu Yesu, 27pakuti nonse amene munalumikizana ndi Khristu mu ubatizo munavala Khristu. 28Palibe Myuda kapena Mgriki, kapolo kapena mfulu, mwamuna kapena mkazi, pakuti nonse ndinu amodzi mwa Khristu Yesu. 29Ngati inu muli ake a Khristu, ndiye kuti ndinu mbewu ya Abrahamu, ndi olowamʼmalo molingana ndi lonjezo.

New Russian Translation

Галатам 3:1-29

Соблюдение Закона или вера

1Глупые галаты! Кто это так заворожил вас, вас, которым так ясно был представлен распятый Христос? 2Ответьте мне на один вопрос: вы получили Духа благодаря соблюдению Закона или же по вере в то, что вы услышали? 3Неужели вы так глупы? Вы начали Духом, а сейчас вы хотите достичь цели человеческими усилиями? 4Неужели все, через что вы прошли, было напрасно? Не может быть, чтобы все это было напрасным! 5Разве Бог дает вам Духа и совершает среди вас чудеса потому, что вы соблюдаете Закон, или же потому, что вы поверили тому, о чем вы услышали?

6Вспомните Авраама, он «поверил Богу, и это было вменено ему в праведность»3:6 См. Быт. 15:6.. 7Так поймите же, что те, кто верит, – сыны Авраама!

8В Писании было предсказано, что Бог будет оправдывать людей из всех народов по их вере, и уже тогда была возвещена Радостная Весть, когда было сказано Аврааму: «Через тебя получат благословение все народы»3:8 См. Быт. 12:3; 18:18; 22:18.. 9Поэтому те, кто верит, получают благословение вместе с верующим Авраамом.

10Все, кто полагается на соблюдение Закона, находятся под проклятием. Ведь написано: «Проклят каждый, кто не исполняет всего, что записано в книге Закона»3:10 См. Втор. 27:26. Перечень проклятий, которые могут постигнуть того, кто не исполняет повелений Бога, находится во Втор. 28:15-68.. 11Ясно ведь, что никто не получает оправдания перед Богом исполнением Закона, потому что «праведный верой жив будет»3:11 См. Авв. 2:4.. 12Закон же основывается не на вере, потому что написано: «Исполняющий их будет жив благодаря им»3:12 См. Лев. 18:5.. 13Так вот, Христос искупил нас от проклятия Закона. Он Сам понес проклятие вместо нас (как об этом и сказано: «Проклят каждый, кто повешен на дереве»3:13 См. Втор. 21:23. Если человек висел на дереве, то это было знаком того, что он проклят Богом. Иисус взял на Себя наши грехи, будучи распят на деревянном кресте.), 14чтобы все народы могли получить через Иисуса Христа благословение, данное Аврааму, и чтобы мы получили обещанного Духа по вере3:14 Или: «чтобы посредством веры в Иисуса Христа все народы могли получить оправдание перед Богом, которое Дух обещал через Авраама»..

Превосходство обещания над Законом

15Братья, возьмем пример из повседневной жизни, ведь даже завещание3:15 С языка оригинала это слово можно перевести двояко: «завещание» и «договор». В данном отрывке это слово имеет оба эти значения. человека, которое должным образом утверждено, никто не вправе изменять или дополнять. 16Точно так же и с обещанием, данным Аврааму и его потомку. Заметьте, что в Писании не сказано «его семенам», а «его семени»3:16 См. Быт. 12:7 со сноской; 13:15; 21:12; 22:18; 24:7., то есть имеется в виду один его потомок – Христос. 17Я хочу сказать, что Закон, данный четыреста тридцать лет спустя, не мог отменить завет с Авраамом, установленный Богом прежде, и тем самым сделать недействительным данное Аврааму обещание. 18Если бы наследство зависело от Закона, то оно не могло бы основываться на обещании, но Бог, в Своей благодати, дал его Аврааму по обещанию!

19В чем же тогда назначение Закона? Закон был добавлен позже из-за людских грехов3:19 Букв.: «по причине преступлений» или «для преступлений». и действовал до тех пор, пока не пришел Потомок, к Которому относится обещание. Закон был дан через ангелов, рукой посредника. 20Нет нужды в посреднике, если кто-то действует один, а Бог один.

21Так что же, Закон противоречит обещаниям Божьим? Ни в коем случае! Если бы данный нам Закон был в силах давать жизнь, то оправдание действительно зависело бы от Закона. 22Но Писание говорит, что весь мир находится в рабстве греха, а значит, обещанное может быть дано только по вере в Иисуса Христа и лишь тем, кто верит. 23Пока не пришла вера, мы были узниками, охраняемыми Законом, до того времени, когда эта вера будет нам открыта. 24Итак, Закон воспитывал нас до прихода Христа3:24 Или: «Закон был нашим воспитателем, ведущим ко Христу»., чтобы, когда Он придет, получить оправдание по вере. 25Но вера уже пришла, и нам больше не нужно воспитание Закона.

Не рабы, а сыновья

26Благодаря вере во Христа Иисуса все вы стали сынами Бога. 27Ведь все крещеные во Христа «облеклись» в Христа. 28Нет больше ни иудея, ни грека, ни раба, ни свободного, ни мужчины и ни женщины, вы все одно во Христе Иисусе! 29А если вы принадлежите Христу, то тогда вы и являетесь потомством3:29 Букв.: «семенем». Авраама и наследниками Божьего обещания.