Aefeso 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 1:1-23

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu.

Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:

2Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Madalitso Auzimu mwa Khristu

3Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu. 4Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake, 5Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake. 6Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda. 7Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu 8chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso, 9Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake. 10Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.

11Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake, 12nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake. 13Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza. 14Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.

Kuyamika ndi Kupemphera

15Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse, 16ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga. 17Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni. 18Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima. 19Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija 20imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba. 21Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. 22Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo, 23umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.

New Russian Translation

Эфесянам 1:1-23

1От Павла, апостола Иисуса Христа, избранного по воле Бога.

Святым в Эфесе, живущим по вере в Иисуса Христа.

2Благодать и мир вам от Бога, нашего Отца, и от Господа Иисуса Христа.

Духовные благословения

3Благословен Бог и Отец нашего Господа Иисуса Христа. Он во Христе благословил нас всеми духовными благословениями небес. 4Ведь Он избрал нас в Нем еще до создания мира, чтобы нам быть святыми и непорочными перед Ним. Он, по Своей любви, 5по Своему доброму желанию и воле, предопределил нам через Иисуса Христа стать усыновленными Им детьми. 6В этом проявлена вся слава Его благодати, которую Он дал нам во Христе, возлюбленном Им. 7В Нем мы получили искупление Его кровью и прощение грехов по Его безграничной благодати, 8которой Он щедро наделил нас. Со всякой мудростью и знанием 9Он открыл нам тайну Своей воли. Он сделал это по Своему доброму желанию, изначально воплощенному во Христе, 10чтобы в определенное время объединить все на небесах и на земле под властью Христа.

11В Нем мы стали наследниками, как это и было предопределено замыслом Бога, совершающего все в мире согласно Своей воле и Своим целям, 12чтобы мы, первыми возложившие надежду на Христа, послужили к Его восхвалению.

13В Нем и вы, услышав слово истины – Радостную Весть, несущую вам спасение, – и поверив во Христа, были отмечены печатью обещанного Святого Духа, 14Который является залогом нашего будущего наследия и искупления тех, кто принадлежит Ему, для похвалы Его славы.

Молитва Павла

15Поэтому и я, услышав о вашей вере в Господа Иисуса и о вашей любви ко всем святым, 16не перестаю благодарить за вас Бога, вспоминая вас в своих молитвах. 17Я молюсь, чтобы Бог нашего Господа Иисуса Христа, прославленный Отец, дал вам Духа мудрости и откровения1:17 Или: «дал вам духовную мудрость и откровение»., чтобы вы лучше познали Его. 18Я молюсь и о том, чтобы Бог просветил очи вашего сердца, и вы увидели, что представляет собой та надежда, к которой Он вас призвал, сколь велико богатство славы, которую получат в наследство святые, 19и каково безмерное величие Его силы в нас, верующих под действием Его безграничной силы. 20Этой же силой Бог произвел действие и во Христе, когда воскресил Его из мертвых и посадил по правую руку1:20 См. Пс. 109:1. от Себя на небесах, 21выше всяких начальств, властей, сил и господств и выше всякого имени, упоминаемого не только в этом веке, но и в будущем. 22Бог все покорил под ноги Христа1:22 См. Пс. 8:7., поставил Его, Владыку всего, главой Церкви, 23которая является Его телом, полнотой Того, Кто наполняет все во всем.