Afilipi 2 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 2:1-30

Kutsanzira Kudzichepetsa kwa Khristu

1Ngati muli ndi chilimbikitso chilichonse chifukwa cholumikizana ndi Khristu, ngati muli ndi chitonthozo chifukwa cha chikondi chake, ngati muli ndi mtima umodzi mwa Mzimu, ndipo ngati mumakomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, 2tsono tsirizani chimwemwe changa pokhala amaganizo ofanana, achikondi chimodzimodzi, amodzi mu mzimu ndi acholinga chimodzinso. 3Musachite kalikonse ndi mtima odzikonda chabe kapena odzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa ndipo aliyense aziona mnzake ngati womuposa iyeyo. 4Musamangofuna zokomera inu nokha koma aliyense azifuna zokomeranso ena.

5Pa ubale wanu wina ndi mnzake, mukhale ndi mtima wofanana ndi wa Khristu Yesu:

6Iyeyu, pokhala Mulungu ndithu,

sanatenge kufanana ndi Mulungu kukhala chinthu choyenera kuchigwiritsa.

7Koma anadzichepetsa kotheratu

nakhala ndi khalidwe ngati la kapolo

ndi kukhala munthu ngati anthu ena onse.

8Ndipo pokhala munthu choncho

anadzichepetsa yekha

ndipo anamvera mpaka imfa yake,

imfa yake ya pamtanda!

9Choncho Mulungu anamukweza Iye kukhala wapamwamba kwambiri,

ndipo anamupatsa dzina loposa dzina lina lililonse

10kuti pakumva dzina la Yesu, bondo lililonse limugwadire,

kumwamba ndi pa dziko lapansi ndi pansi pa dziko,

11ndipo lilime lililonse livomereze kuti Yesu Khristu ndi Ambuye

kuchitira ulemu Mulungu Atate.

Kuwala monga Nyenyezi

12Tsono, abwenzi anga okondedwa, monga mwakhala omvera nthawi zonse, osati pamene ndinali nanu pokha, koma tsopano koposa pamene ndili kutali. Pitirizani kugwira ntchito ya chipulumutso chanu mwa mantha ndi kunjenjemera, 13pakuti ndi Mulungu amene amagwira ntchito mwa inu kuti mufune ndi kuchita zimene zimamukondweretsa Iyeyo.

14Muzichita zonse mosawiringula kapena mosatsutsapo, 15kuti mukhale wopanda cholakwa ndi angwiro, ana a Mulungu wopanda cholakwika mu mʼbado uno wachinyengo ndi wosocheretsa. Mukatero mudzawala pakati pawo ngati nyenyezi zakumwamba 16powawuza mawu amoyo. Ndipo ine ndidzatha kunyadira pa tsiku la Khristu kuti sindinathamange kapena kugwira ntchito pachabe. 17Koma ngakhale ndikuthiridwa ngati nsembe ya chakumwa yoperekedwa pa nsembe ndi pa utumiki wochokera mʼchikhulupiriro chanu, ndine wokondwa ndi wosangalala pamodzi ndi inu nonse. 18Chomwechonso, inu khalani okondwa ndi osangalala nane pamodzi.

Timoteyo ndi Epafrodito

19Ngati Ambuye Yesu alola, ndikukhulupirira kuti ndidzamutuma Timoteyo msanga kwanuko, kuti mwina ndingadzasangalale ndikadzamva za moyo wanu. 20Ndilibenso wina monga iyeyu amene ali ndi chidwi chenicheni pa za moyo wanu. 21Pakuti aliyense amangofuna zokomera iye yekha osati zokomera Yesu Khristu. 22Koma inu mukudziwa kuti Timoteyo wadzionetsa yekha, chifukwa watumikira ndi ine pa ntchito ya Uthenga Wabwino monga mwana ndi abambo ake. 23Choncho ndikuyembekezera kumutuma msanga ndikangodziwa mmene zinthu zanga ziyendere. 24Ndipo ndikukhulupirira kuti Ambuye akalola ine mwini ndidzafikanso kwanuko posachedwapa.

25Koma ndikuganiza kuti nʼkofunika kuti ndikutumizireni mʼbale wanga Epafrodito, mtumiki mnzanga ndi msilikali mnzanga, amenenso ndi mtumiki wanu amene munamutumiza kuti adzandithandize pa zosowa zanga. 26Pakuti akukulakalakani nonsenu ndipo akusauka mu mtima chifukwa munamva kuti akudwala. 27Zoonadi ankadwala ndipo anatsala pangʼono kumwalira. Koma Mulungu anamuchitira chifundo, ndipo sanangomuchitira chifundo iye yekhayu komanso ine, kuti chisoni changa chisachuluke. 28Choncho khumbo langa lofulumiza kumutumiza lakula, kuti pamene mumuonenso musangalale komanso kuti nkhawa yanga ichepe. 29Mulandireni mwa Ambuye ndi chimwemwe chachikulu, ndipo anthu onga iyeyu muziwachitira ulemu. 30Iyeyu anatsala pangʼono kufa chifukwa cha ntchito ya Khristu, anayika moyo pa chiswe kuti akwaniritse thandizo limene inu simukanatha.

Knijga O Kristu

Filipljanima 2:1-30

Jedinstvo u poniznosti

1Ima li dakle u Kristu kakva ohrabrenja? Ima li utjehe u njegovoj ljubavi? Ima li zajedništva u Duhu? Ima li nježnosti i samilosti? 2Usrećite me onda: budite složni, volite se uzajamno, budite jednodušni u osjećajima i mislima. 3Ne budite sebični ni umišljeni. Budite ponizni i smatrajte jedni druge većima od sebe. 4Ne starajte se samo za vlastitu korist već i za korist drugih.

Kristova poniznost i uzvišenost

5Vaše bi motrište trebalo biti jednako Isusovu. 6Iako je bio Bog, nije zahtijevao svoje pravo da bude Bogom, 7nego je odložio svoju moćnu snagu i slavu te, uzevši na sebe lik sluge, postao ljudskim bićem. I kao ljudsko biće 8ponizio je samoga sebe, poslušan do smrti, i to do smrti na križu. 9Zato ga je Bog uzdignuo iznad svega i darovao mu ime uzvišenije od svakoga drugog imena, 10da pred Isusovim imenom prignu koljena sva bića na nebu, na zemlji i pod zemljom 11i da svaki jezik prizna: “Isus Krist je Gospodin” na slavu Boga Oca.

Sjajno svijetlite za Krista

12Najdraži moji, uvijek ste bili poslušni dok sam bio s vama. Ali sada dok me nema, morate se još više, sa strahom i drhtanjem, truditi oko svojega spasenja. 13Jer Bog djeluje budeći u vama želju da mu budete poslušni i dajući vam snage da činite ono što mu je ugodno.

14Ma što činili, ne prigovarajte i ne svađajte se 15da vas nitko ne može osuditi. Živite besprijekornim i čistim životom, kao neporočna Božja djeca usred izopačenog i pokvarenog naraštaja. Svijetlite u njihovoj tami poput zvijezda u svemiru. 16Čvrsto se držite Riječi života, tako da se na dan Kristova povratka mogu ponositi da nisam uzalud trčao trku niti uzalud se trudio. 17Štoviše, ako se i moja krv mora proliti poput žrtve za vašu vjeru i požrtvovno Božje djelo, sretan sam i radujem se s vama. 18I vi se zato veselite i radujte sa mnom.

Preporuka Timoteju

19Nadam se da ću, bude li volja Gospodina Isusa, ubrzo poslati k vama Timoteja, da me razveseli vijestima o vama. 20Nemam nikoga drugog poput njega tko bi se tako brinuo za vašu dobrobit, 21jer se svi drugi brinu samo o sebi, a ne o onomu što je Kristovo. 22Ali znate da je Timotej prokušan. Pomagao mi je u naviještanju Radosne vijesti kao sin ocu. 23Njega vam se nadam poslati čim doznam što će ovdje biti sa mnom. 24A pouzdajem se u Gospodina da ću vam i sam ubrzo doći.

Preporuka Epafroditu

25U međuvremenu mi se činilo potrebnim da vam pošaljem natrag Epafrodita, svojega brata, suradnika i suborca, kojega ste poslali da mi pomogne u potrebi. 26Šaljem ga doma jer čezne za vama i jer je žalostan što ste čuli da je obolio. 27Zaista je bio bolestan, gotovo je umro. Ali Bog mu se—a i meni—smilovao da me ne snađe žalost na žalost.

28Zato ga što prije šaljem jer znam da ćete se razveseliti kad ga vidite, a onda ću i ja biti manje žalostan. 29Primite ga dakle s ljubavlju Gospodnjom2:29 U grčkome: u Gospodinu. i poštujte takve ljude. 30Izložio se životnoj pogibli radi Kristova djela i umalo je umro čineći za mene ono što vi niste mogli jer ste bili daleko.