Aefeso 1 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 1:1-23

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu.

Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:

2Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Madalitso Auzimu mwa Khristu

3Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu. 4Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake, 5Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake. 6Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda. 7Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu 8chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso, 9Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake. 10Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.

11Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake, 12nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake. 13Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza. 14Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.

Kuyamika ndi Kupemphera

15Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse, 16ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga. 17Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni. 18Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima. 19Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija 20imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba. 21Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. 22Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo, 23umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.

Knijga O Kristu

Efežanima 1:1-23

Pavlovi pozdravi

1Dragi sveti u Efezu, uvijek odani Isusu Kristu, ovo vam piše Pavao, kojega je Bog izabrao za apostola Isusa Krista.

2Neka vam je milost i mir od našega Boga Oca i Gospodina Isusa Krista.

Duhovni blagoslovi

3Slava neka je Bogu, Ocu našega Gospodina Isusa Krista, jer nas je, zato što pripadamo Kristu, blagoslovio svakim duhovnim blagoslovom u nebesima. 4Bog nas je, još prije nego što je stvorio svijet, izabrao da u Kristu budemo sveti i neporočni u njegovim očima. U ljubavi 5je njegov nepromjenjivi naum oduvijek bio da nas posvoji u vlastitu obitelj kroz Isusa Krista. Rado je to učinio.

6Slavimo zato Boga za milost koju nam je iskazao, da pripadamo njegovu ljubljenom Sinu 7u kojemu imamo otkupljenje njegovom krvlju i oproštenje grijeha po njegovoj izobilnoj milosti. 8S milošću nam je obilno udijelio mudrost i razumijevanje.

9Bog nam je otkrio tajni naum s Kristom, koji je odavno dobrohotno smislio. 10Nakanio je sve—na nebesima i na zemlji—podložiti Kristu kad se za to napuni vrijeme. 11U njemu smo i mi postali baštinicima, predodređeni prema nakani onoga koji sve čini u skladu sa svojom voljom. 12Božja je nakana bila da mi, koji smo se prvi pouzdali u Krista, proslavljamo svojega slavnog Boga. 13I vi ste čuli istinu, Radosnu vijest, da vas Bog spašava. A kad ste povjerovali u Krista, Bog vam je dao Svetoga Duha i tako vas zapečatio da ste njegovi. 14Duh je Božje jamstvo da će nam dati sve što je obećao te da nas je otkupio sebi na slavu.

Pavlova molitva za duhovnu mudrost

15Zato i ja, otkako sam čuo za vašu snažnu vjeru u Gospodina Isusa i ljubav koju iskazujete prema svetima posvuda, 16ne prestajem zahvaljivati Bogu za vas. Stalno se molim za vas 17iskajući od Boga, slavnoga Oca našega Gospodina Isusa Krista, da vam udijeli Duha mudrosti i razumijevanja kako bi ga što bolje spoznali. 18Molim Boga da vam srca obasja svjetlošću da možete razumjeti kakvo je bogato i slavno naslijeđe dao svojem narodu. 19Molim se da razumijete nevjerojatnu silinu njegove moći za nas koji vjerujemo. Jednako je djelotvorna i silna 20kao i sila koja je uskrisila Krista i posjela ga na počasno mjesto, Bogu zdesna na nebesima— 21iznad svakoga poglavarstva, vlasti, moći i gospodstva ne samo u ovome svijetu nego i u svijetu koji će doći. 22Bog je sve podložio Kristovoj vlasti, a njega je—iznad svih—postavio za poglavara Crkve, 23koja je njegovo Tijelo, punina Onoga koji ispunja sve u svima.