2 Samueli 5 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 5:1-25

Davide Adzozedwa Kukhala Mfumu ya Israeli

1Mafuko onse a Israeli anabwera kwa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife mafupa ndi mnofu wanu. 2Kale lija, pamene Sauli anali mfumu yathu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova anakuwuzani kuti, ‘Udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’ ”

3Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, mfumu inachita nawo pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli.

4Davide anali ndi zaka makumi atatu pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka makumi anayi. 5Analamulira Yuda ali ku Hebroni kwa zaka zisanu ndi ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi, ndipo ali ku Yerusalemu analamulira Israeli yense ndi Yuda kwa zaka 33.

Davide Alanda Mzinda wa Yerusalemu

6Mfumu ndi ankhondo ake anapita ku Yerusalemu kukathira nkhondo Ayebusi amene ankakhala kumeneko. Ayebusiwo anamuwuza Davide kuti, “Inu simulowa muno. Ngakhale osaona ndi olumala akhoza kukuthamangitsani.” Iwo ankaganiza kuti, “Davide sangathe kulowa momwemo.” 7Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.

8Pa tsiku limenelo Davide anati, “Aliyense wogonjetsa Ayebusi ayenera kudzera mʼngalande ya madzi kuti akafike kwa iwo amene ndi ‘olumala ndi osaona,’ amene ndi adani a Davide.” Nʼchifukwa chake amanena kuti, “Olumala ndi osaona sadzalowa mʼnyumba yaufumu.”

9Tsono Davide anakhazikika mu lingamo ndipo mzindawu anawutcha, Mzinda wa Davide. Iye anamanga malo onse ozungulira kuyambira ku matsitso ozungulira khoma. 10Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

11Tsono Hiramu mfumu ya Turo inatumiza amithenga ake kwa Davide, pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndi amisiri a matabwa ndi amisiri a miyala, ndipo anamumangira Davide nyumba yaufumu. 12Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.

13Davide atafika ku Yerusalemu kuchokera ku Hebroni, anakwatira azikazi natenganso akazi ena kumeneko, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri. 14Mayina a ana amene anabereka ku Yerusalemu ndi awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni, 15Ibihari, Elisua, Nefegi, Yafiya, 16Elisama, Eliada ndi Elifeleti.

Davide Agonjetsa Afilisti

17Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anakalowa mu linga. 18Ndipo Afilisti anabwera ndi kukhala momwazika mʼChigwa cha Refaimu. 19Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?”

Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka ndithu mʼmanja mwako.”

20Choncho Davide anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Yehova waphwanya adani anga ine ndikuona.” Choncho anawatcha malowa Baala Perazimu. 21Afilisti anasiya mafano awo kumeneko ndipo Davide ndi ankhondo ake anawatenga.

22Nthawi inanso Afilisti anabweranso namwazikana mʼChigwa cha Refaimu; 23Davide anafunsa Yehova ndipo Yehovayo anayankha kuti, “Usapite molunjika koma uzungulire kumbuyo kwawo ndipo ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku. 24Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukayende mofulumira, chifukwa izi zikasonyeza kuti Yehova ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.” 25Kotero Davide anachita zimene Yehova anamulamulira ndipo anakantha Afilisti njira yonse kuchokera ku Geba mpaka ku Gezeri.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

撒母耳記下 5:1-25

大衛統治全以色列

1以色列各支派都來希伯崙大衛,對他說:「我們是你的骨肉同胞。 2從前掃羅做王的時候,率領以色列人出征打仗的是你,耶和華也曾應許讓你做祂以色列子民的牧者和首領。」 3以色列的長老都到希伯崙大衛王,大衛與他們在耶和華面前立約,他們膏立大衛以色列的王。 4大衛三十歲登基,執政共四十年。 5他在希伯崙統治猶大七年半,在耶路撒冷統治以色列猶大三十三年。

6大衛率領軍隊來到耶路撒冷,要攻打那裡的耶布斯人。耶布斯人對大衛說:「你攻不進來,就連我們這裡的瞎子、瘸子都可以把你趕走。」他們以為大衛攻不進去。 7結果大衛的軍隊攻取了錫安的堡壘,即後來的大衛城。 8那天,大衛下令軍隊從地下水道爬進城去,攻打那些「瞎子、瘸子」,他憎惡這些耶布斯人。後來便有一句俗語:「瞎子、瘸子不得進殿!」 9大衛住在錫安的堡壘裡,並稱之為大衛城,他又從米羅興建環城圍牆。 10大衛日漸強盛,因為萬軍之上帝耶和華與他同在。

11泰爾希蘭差遣使者帶著香柏木、木匠和石匠去為大衛建造宮殿。 12那時,大衛知道耶和華已立他做以色列王,並因祂以色列子民的緣故而使他國家興旺。

13大衛希伯崙遷到耶路撒冷以後,又選立妃嬪,生了更多的兒女。 14以下是他在耶路撒冷生的兒子:沙姆亞朔罷拿單所羅門15益轄以利書亞尼斐雅非亞16以利沙瑪以利雅大以利法列

大衛戰勝非利士人

17非利士人聽說大衛已被膏立為以色列王,就全軍出動,要搜尋大衛大衛得到消息便退到堅城裡。 18非利士人大軍壓境,散佈在利乏音谷。 19大衛求問耶和華:「我可以去迎戰非利士人嗎?你會把他們交在我手裡嗎?」耶和華說:「去吧,我必把他們交在你手裡。」 20大衛前往巴力·毗拉心,在那裡打敗了敵人。他說:「耶和華像洪水決堤一樣為我沖垮了仇敵。」於是他稱那地方為巴力·毗拉心5·20 巴力·毗拉心」意思是「沖垮之主」。21大衛和他的軍隊帶走了非利士人所丟棄的神像。

22後來非利士人又捲土重來,散佈在利乏音谷。 23大衛又求問耶和華,耶和華說:「你不要正面出擊,要繞到他們後面,從桑林對面攻打他們。 24當你聽見桑樹梢上響起腳步聲時,就要快速進攻,因為那表示耶和華已在你前頭去攻擊非利士的軍隊了。」 25大衛遵命而行,打敗非利士人,由迦巴一直殺到基色