2 Mbiri 7 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 7:1-22

Mwambo Wopereka Nyumba kwa Yehova

1Solomoni atamaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kutentha nsembe zopsereza ndi nsembe zina, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulunguyo. 2Ansembe sanathe kulowa mʼNyumba ya Mulungu chifukwa munadzaza ulemerero wa Yehova. 3Aisraeli onse ataona moto ukuchokera kumwamba ndi ulemerero wa Yehova pamwamba pa Nyumba ya Mulungu, anagwada poyalidwa miyalapo ndipo anagunditsa nkhope zawo pansi, ndi kulambira ndi kutamanda Yehova, ponena kuti,

“Iye ndi wabwino;

chikondi chake chikhala chikhalire”

4Tsono mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova. 5Ndipo mfumu Solomoni anapereka nsembe ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Kotero mfumu ndi anthu onse anachita mwambo wopereka Nyumba kwa Mulungu. 6Ansembe anayimirira mʼmalo mwawo, monganso anachitira Alevi ndi zida zoyimbira za Yehova, zimene Davide anapanga zotamandira Yehova ndipo zimagwiritsidwa ntchito pamene amatamanda, ponena kuti, “Chikondi chake chikhale chikhalire.” Moyangʼanizana ndi Alevi, ansembe amaliza malipenga, ndipo Aisraeli onse anali atayimirira.

7Solomoni anapatula malo a pakati pa bwalo kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndipo pamenepo anapereka nsembe zopsereza ndi mafuta, zopereka za chiyanjano, chifukwa guwa lansembe lamkuwa limene anapanga panalibe malo woti nʼkuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe za ufa ndi mafuta.

8Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero kwa masiku asanu ndi awiri pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku chigwa cha ku Igupto. 9Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panali msonkhano, pakuti anachita mwambo wopereka guwa lansembe kwa masiku asanu ndi awiri ndi masiku enanso asanu ndi awiri achikondwerero. 10Pa tsiku la 23 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Solomoni anawuza anthu aja kuti apite kwawo. Anthu anali achimwemwe ndi okondwa mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira Davide ndi Solomoni ndiponso anthu ake Aisraeli.

Yehova Aonekera Solomoni

11Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene zinali mu mtima mwake pa Nyumba ya Yehova ndi nyumba yake yaufumu, 12Yehova anamuonekera usiku ndipo anati:

“Ine ndamva pemphero lako ndipo ndadzisankhira malo ano kukhala Nyumba yanga yoperekeramo nsembe.

13“Ine ndikatseka kumwamba kuti mvula isagwe, kapena kulamulira dzombe kuti liwononge dziko, kapena kutumiza mliri pakati pa anthu, 14ngati anthu anga, amene amatchedwa ndi dzina langa adzichepetsa ndi kupemphera ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zawo zoyipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwamba ndipo ndidzakhululuka tchimo lawo ndi kuchiritsa dziko lawo. 15Ndipo maso anga adzatsekuka ndi makutu anga adzakhala tcheru kumva mapemphero a pamalo pano. 16Ine ndasankha ndipo ndapatula Nyumba yangayi kotero kuti ndidzakhala mʼmenemo kwamuyaya. Maso ndi mtima wanga zidzakhala pano nthawi zonse.

17“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula, ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga, 18Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu, monga ndinachitira pangano ndi abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu wolamulira Israeli.’

19“Koma ngati iwe udzapatuka ndi kutaya malangizo ndi malamulo amene ndakupatsa ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, 20pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko langa limene ndinawapatsa, ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndadzipatulira. Ndipo udzakhala ngati mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse. 21Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’ 22Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’ ”

New Serbian Translation

2. Књига дневника 7:1-22

Посвећење Дома

1Кад је Соломон завршио молитву, огањ сиђе са небеса и спали жртву свеспалницу и друге жртве, а Господња слава испуни Дом. 2Свештеници нису могли да уђу у Дом Господњи јер је био испуњен славом Господњом 3А када је сав Израиљев народ видео како је огањ сишао и да је слава пала на Господњи Дом, поклонили су се лицем до земље, до каменог пода захваљујући Господу

„јер је добар,

јер је милост његова довека.“

4Затим су цар и сав народ принели жртве пред Господом. 5Цар Соломон је принео двадесет две хиљаде говеда и стотину двадесет хиљада оваца. Тако су цар и сав народ посветили Дом Божији. 6Свештеници су стајали на својим дужностима, Левити су певали Господу са инструментима које је направио цар Давид за хваљење Господа. Захваљивали су Давидовом песмом Господу јер је милост његова довека – Давид је тако преко њих захваљивао – а свештеници су дували у трубе док је пред њима стајао сав Израиљ.

7Соломон је посветио средиште дворишта, које је испред Дома Господњег. Онде је принео жртве свеспалнице и сало жртава мира јер на бронзаном жртвенику, што га је направио, није било места. Толико је било жртава – свеспалница, жита и сала – да нису могле да стану на жртвеник.

8У то време је Соломон седам дана приредио свечаност. Са њим је био сав Израиљ, велико мноштво је дошло од Лево-Амата до Египатског потока. 9Осмог дана славља су имали свечани сабор, јер су седам дана посвећивали жртвеник и још седам дана празновали. 10Двадесет трећег дана трећег месеца цар је отпустио народ, па су отишли својим кућама, веселећи се и радујући се у срцу због свег добра што је Господ учинио своме слузи Давиду и своме народу Израиљу.

Бог се јавља Соломону

11Тако је Соломон завршио Дом Господњи и царев двор. Успевао је у свему што је срцем замислио да уради и у Дому Господњем и у свом двору. 12Једне ноћи, Господ се јавио Соломону и рекао му:

„Чуо сам твоју молитву и изабрао ово место за себе као Дом за жртве.

13Ако затворим небеса и не буде кише, ако пошаљем скакавце да попасу земљу, ако пошаљем болест на народ; 14и понизи се народ који је по мени назван, помоле се, потраже моје лице и врате се са својих злих путева, ја ћу их чути са небеса, опростићу им грехе и излечићу им земљу. 15Сад ће моје очи бити отворене и уши пажљиве на молитве са овог места 16Сада сам изабрао и посветио овај Дом да у њему заувек буду моје име, моје срце и моје очи.

17А ти, ако будеш ходао преда мном као што је ходао твој отац Давид, према свему што сам ти заповедио, и будеш чувао моје прописе и уредбе, 18учврстићу твој царски престо, као што сам обећао твоме оцу Давиду – ’Никад ти неће понестати владар у Израиљу.’

19Али ако се одвратите и заборавите моје прописе и заповеди које сам ставио пред вас да их следите, па одете да служите другим боговима и да им се клањате – 20искоренићу их са лица моје земље коју сам вам дао, а Дом који сам посветио за своје име одбацићу од себе, па ће Израиљ постати предмет исмејавања и ругања међу свим народима. 21А свако ко буде пролазио поред овог Дома, који је сада узвишен, биће запрепаштен, па ће говорити: ’Зашто је Господ поступио овако са овом земљом и са овим Домом?’ 22Тада ће им рећи: ’Зато што су напустили Господа, Бога њихових отаца који их је извео из Египта и пригрлили друге богове клањајући им се и служећи им. Зато је Господ довео на њих сву ову невољу.’“