2 Mbiri 6 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 6:1-42

1Pamenepo Solomoni anati, “Yehova anati adzakhala mʼmitambo yakuda; 2ine ndakumangirani Nyumba yokongola kwambiri, malo woti muzikhalamo mpaka muyaya.”

3Aisraeli onse ali chiyimire pomwepo, mfumu inatembenuka ndi kuwadalitsa. 4Ndipo inati,

“Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli amene wachita ndi dzanja lake zimene analonjeza ndi pakamwa pake kwa Davide abambo anga. Pakuti Iye anati, 5‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga ku Igupto, sindinasankhe mzinda wina uliwonse pa fuko lina lililonse la Aisraeli kuti kumeneko andimangire Nyumba kuti ndizikhalamo kapena munthu wina aliyense kuti akhale mtsogoleri wa Aisraeli anthu anga. 6Koma tsopano ndasankha Yerusalemu kuti Dzina langa likhale kumeneko ndiponso ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisraeli.’

7“Abambo anga Davide anali ndi maganizo mu mtima mwawo oti amangire Nyumba Yehova Mulungu wa Israeli. 8Koma Yehova ananena kwa abambo anga Davide kuti, ‘Popeza zinali mu mtima mwako kumangira Nyumba dzina langa, unachita bwino kukhala ndi maganizo amenewa mu mtima mwakomo. 9Komatu si iwe amene udzamanga Nyumba ya Mulungu koma mwana wako, mwana amene iwe udzabereke. Iyeyo ndiye amene adzandimangire Nyumba.’

10“Yehova wasunga zimene analonjeza. Ine ndalowa mʼmalo mwa abambo anga Davide, ndipo tsopano ndili pa mpando waufumu wa Israeli, monga momwe Yehova analonjezera, ndipo ndamangira nyumba Dzina la Yehova Mulungu wa Israeli. 11Mʼmenemo ndayikamo Bokosi la Chipangano, mmene muli pangano la Yehova limene anapangana ndi ana a Israeli.”

Pemphero la Solomoni

12Pamenepo Solomoni anayimirira patsogolo pa guwa lansembe la Yehova patsogolo pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake. 13Iyeyo anali atapanga nsanja yamkuwa, kutalika kwake kunali mamita awiri, mulifupi mwake munali mamita awiri, msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka ndipo nsanjayo anayimika pakati pa bwalo lakunja. Iye anayimirira pa nsanjapo nagwada pamaso pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake kumwamba. 14Iye anati,

“Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wofanana nanu kumwamba kapena pa dziko. Inu amene mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa atumiki anu amene amayenda pamaso panu ndi mtima wawo wonse. 15Inu mwasunga lonjezo lanu kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu. Inde zimene munalonjeza ndi pakamwa panu, mwazikwaniritsa ndi manja anu monga mmene tikuonera lero lino.

16“Ndipo tsopano, Inu Yehova Mulungu wa Israeli, sungani zimene munalonjeza kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu pamene munati, ‘Sudzasowa munthu wokhala pamaso panga pa mpando waufumu wa Israeli, ngati ana ako adzasamalira mayendedwe awo ndi kusunga malamulo anga monga iwe wachitira.’ 17Ndipo tsopano Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, lolani kuti mawu anu akwaniritsidwe amene munalonjeza mtumiki wanu Davide.

18“Kodi Mulungu angakhaledi pa dziko lapansi ndi munthu? Mlengalenga ngakhale kumwamba kwenikweni sikungakukwaneni. Nanga kuli bwanji ndi Nyumba iyi imene ndamanga! 19Koma Inu Yehova, Mulungu wanga, imvani pemphero ndi pembedzero la mtumiki wanu. Imvani kulira ndi pemphero la mtumiki wanu limene ndikupempha pamaso panu. 20Maso anu azikhala otsekuka kuyangʼana Nyumba ino usana ndi usiku, malo ano amene Inu munati mudzayikamo Dzina lanu, imvani pemphero la mtumiki wanu limene akupemphera pa malo ano. 21Imvani mapembedzero a mtumiki wanu ndi a anthu anu Aisraeli pamene akupemphera akuyangʼana malo ano. Imvani kumwambako, malo anu amene mumakhala; ndipo mukamva muzitikhululukira.

22“Munthu akalakwira mnzake, nawuzidwa kuti alumbire, akabwera kudzalumbira patsogolo pa guwa lansembe la Nyumba ino, 23imvani kumwambako ndi kuchitapo kanthu. Weruzani atumiki anuwo, wochimwa mugamule kuti ndi wolakwa ndipo alangidwe chifukwa cha zimene wachita. Wosachimwa mugamule kuti wosalakwa, ndipo muonetse kusalakwa kwakeko.

24“Anthu anu Aisraeli akagonja kwa adani awo chifukwa akuchimwirani ndipo akatembenukira kwa Inu ndi kuvomereza Dzina lanu, kupemphera ndi kupembedzera pamaso panu mʼNyumba ino, 25pamenepo imvani kumwambako ndi kukhululukira tchimo la anthu anu Aisraeli ndi kuwabweretsa ku dziko limene munawapatsa iwo ndi makolo awo.

26“Pamene kumwamba kwatsekeka ndipo mvula sikugwa chifukwa anthu anu akuchimwirani, ndipo pamene apemphera akuyangʼana malo ano ndi kuvomereza Dzina lanu ndi kutembenuka kuchoka ku machimo awo chifukwa inu mwawalanga, 27pamenepo imvani kumwambako ndipo muwakhululukire atumiki anu, anthu anu Aisraeli. Aphunzitseni makhalidwe oyenera, ndipo gwetsani mvula mʼdziko limene munapereka kwa anthu anu monga cholowa chawo.

28“Pamene mʼdziko mwagwa njala kapena mliri, chinoni kapena chiwawu, dzombe kapena kapuchi, kapena pamene adani azungulira mzinda wawo wina uliwonse, kaya mavuto kapena matenda abwera, 29ndipo wina aliyense mwa Aisraeli akapemphera kapena kukudandaulirani, aliyense wa iwo akadziwa masautso ake ndi ululu wake, ndi kukweza manja awo kuloza Nyumba ino, 30pamenepo imvani kumwambako, malo anu wokhalamo. Khululukani ndipo muchitire aliyense molingana ndi zonse zimene anachita popeza Inu mumadziwa mtima wake, (pakuti ndinu nokha amene mumadziwa mitima ya anthu), 31motero iwo adzakuopani ndipo adzayenda mʼnjira zanu masiku onse amene adzakhale mʼdziko limene munalipereka kwa makolo athu.

32“Ndipo kunena za mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisraeli, koma wabwera kuchokera ku dziko lakutali chifukwa cha dzina lanu lotchukali, ndiponso za dzanja lanu lamphamvu ndi lochita zazikulu, kudzapemphera akuyangʼana Nyumba ino, 33pamenepo imvani kumwambako, malo anu okhalamo, ndipo muchite zonse zimene mlendoyo akukupemphani, kotero kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu ndi kukuopani monga amachitira anthu anu Aisraeli, ndipo adziwe kuti nyumba ino imene ndakumangirani imadziwika ndi dzina lanu.

34“Anthu akapita ku nkhondo kukamenyana ndi adani awo, kulikonse kumene mungawatume, ndipo akapemphera moyangʼana mzinda uno umene mwausankha ndi Nyumba yanu imene ndakumangirani, 35pamenepo imvani kumwamba pemphero lawo ndi kupempha kwawo ndipo muwapulumutse.

36“Pamene achimwira inu, pakuti palibe amene sachimwa, ndipo inu mwawakwiyira ndi kuwapereka kwa adani awo, amene awatenga ukapolo ku dziko lawo lakutali kapena pafupi. 37Ngati asintha mitima yawo ku dziko limene ali akapolo ndi kulapa ndi kukudandaulirani inu mʼdziko la ukapolo wawo ndi kunena kuti, ‘Ife tachimwa, tachita zolakwa ndipo tachita moyipa kwambiri.’ 38Ndipo ngati atembenukira kwa inu ndi mtima ndi moyo wawo wonse mʼdziko lawo la ukapolo kumene anatengedwako ndi kupemphera moyangʼana dziko limene inu munalipereka kwa makolo awo, moyangʼana Nyumba yanu imene ndakumangirani; 39pamenepo imvani kumwamba, malo anu okhala, pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo muwapulumutse. Ndipo mukhululukire anthu anu, amene akuchimwirani.

40“Tsono Inu Mulungu wanga, tsekulani maso anu ndi makutu anu kuti mumve mapemphero ochitikira pa malo ano.

41“Tsopano dzukani Inu Yehova Mulungu, ndipo bwerani ku malo anu ampumulo,

Inu ndi Bokosi la Chipangano la mphamvu zanu.

Inu Yehova Mulungu, ansembe anu avale chipulumutso,

oyera mtima anu akondwere ndi kukhulupirika kwanu.

42Inu Yehova Mulungu musamukane wodzozedwa wanu.

Kumbukirani chikondi chanu chachikulu chimene munalonjeza kwa Davide mtumiki wanu.”

New Serbian Translation

2. Књига дневника 6:1-42

1Тада Соломон рече: „Господ је рекао да ће пребивати у густој тами. 2Ја сам ти саградио величанствени Дом, стан где ћеш пребивати довека.“

3Затим се цар окренуо и благословио сав збор Израиљев, док је сав збор Израиљев стајао. 4Тада рече:

„Нека је благословен Господ, Бог Израиљев, који је својом руком извршио оно што је својим устима обећао моме оцу Давиду, рекавши: 5’Од дана кад сам извео свој народ из Египта, нисам изабрао град међу свим племенима Израиљевим да се сагради Дом где би пребивало моје име. Нисам изабрао ниједног човека да влада Израиљем, мојим народом. 6Ето, изабрао сам да у Јерусалиму буде моје име и изабрао сам Давида да влада над мојим народом Израиљем.’

7Мој отац Давид је наумио да сазида Дом имену Господа, Бога Израиљевог. 8Но, Господ рече моме оцу Давиду: ’Добро си учинио што си у свом срцу наумио да сазидаш Дом моме имену. 9Ипак, нећеш ти саградити Дом, него ће твој син, који је потекао из твојих бедара, саградити Дом моме имену.’

10Господ је одржао обећање, те сам ја наследио свога оца Давида на Израиљевом престолу, како је Господ обећао, и изградио Дом имену Господа, Бога Израиљевог. 11Поставио сам и Ковчег, где је савез Господњи, који је он склопио са синовима Израиљевим.“

Соломонова молитва посвећења

12Соломон је стао пред жртвеник Господњи, испред свег збора Израиљевог и испружио руке. 13Направио је бронзано постоље и поставио га на средину дворишта. Било је дуго и широко пет лаката и три лакта6,13 Око 2,5 m дуго и широко и око 1,5 m високо. високо. Тада је стао на њега, клекнуо испред свег збора Израиљевог, испружио руке према небу 14и рекао:

„О, Господе, Боже Израиљев, нема Бога као што си ти ни на небесима ни на земљи, који чуваш савез и милост својим слугама који ходају пред тобом свим својим срцем. 15Ти си испунио што си рекао своме слузи, моме оцу Давиду; што си рекао својим устима, то си извршио својом руком, као што је то данас.

16А сад, Господе, Боже Израиљев, одржи што си обећао своме слузи, моме оцу Давиду, кад си рекао: ’Неће ти нестати потомка преда мном који ће седети на Израиљевом престолу, само ако твоји синови буду пазили на свој пут и ходили по мом Закону, као што си ти ходио преда мном.’ 17А сад, Господе, Боже Израиљев, нека се обистини твоја реч, коју си рекао своме слузи Давиду.

18Али зар ће Бог заиста боравити на земљи са људима? Ни највиша те небеса не могу обухватити, а камоли овај Дом што сам саградио. 19Обазри се на молитву слуге свога и на његову молбу, Господе Боже; послушај вапај и молитву, коју слуга твој упућује пред тобом. 20Нека твоје очи мотре на овај Дом и дању и ноћу, према месту за које си рекао да ћеш ту ставити своје име, како би чуо молитву коју ти слуга твој упућује на овом месту. 21Почуј преклињање свога слуге и свога народа Израиља којим се моле на овом месту. Послушај с неба, с места где пребиваш – послушај и опрости.

22Кад неко згреши против свог ближњега, те се од њега тражи да се закуне, и он дође и закуне се пред твојим жртвеником у овом Дому, 23ти чуј с небеса и делуј, те осуди онога који је учинио безакоње сваљујући на његову главу према ономе што је учинио. А праведника награди према његовој праведности.

24Ако твој народ Израиљ буде поражен од непријатеља зато што су згрешили против тебе, али се покају пред тобом и дају славу твоме имену, па се помоле и преклињу за милост пред тобом у овом Дому, 25ти чуј на небесима и опрости грех свога народа Израиља, и врати их у земљу коју си дао њима и њиховим оцима.

26Ако се небо затвори и не даје кишу, јер су згрешили против тебе, па се помоле на овом месту, те одају славу твоме имену и покају се за своје грехе, пошто их понизиш, 27ти чуј на небесима и опрости грех својих слугу, свога народа Израиља. И кад их научиш добром путу да по њему ходе, пошаљи кишу својој земљи, коју си дао своме народу у наследство.

28Ако земљу задеси глад, или помор, суша, кукољ, скакавци, гусенице, или кад их непријатељи опколе у којем од њихових градова; каква год да је пошаст или болест, 29па било ко од свег твог народа Израиља осети тегобу и бол, па упути молитву или молбу ширећи руке према овом Дому, 30услиши с небеса, твога Пребивалишта. Опрости и дај свакоме по свим његовим делима, јер ти знаш његово срце – само ти знаш срце људи – 31да би те се бојали, да би твоје путеве следили у све дане док живе у земљи коју си дао њиховим оцима.

32Ако и странац, који није од твог народа Израиља, дође из далеке земље ради твог великог имена, и твоје моћне руке и испружене мишице – ако дође и помоли се у овом Дому – 33услиши га с небеса, твог Пребивалишта, и учини све за шта ти овај странац завапи, да би народи на земљи упознали твоје име и да би те се бојали, као твој народ Израиљ, и да би знали да се твоје име призива над овим Домом који сам саградио.

34Ако твој народ изађе у бој против својих непријатеља путем којим га ти пошаљеш, и они се помоле теби према овом граду који си изабрао, и према Дому који сам саградио твоме имену, 35чуј с небеса њихову молитву и њихову молбу, те им додели правду.

36Ако згреше против тебе – јер нема човека који не чини грех – и ти се разгневиш на њих и изручиш их њиховим непријатељима, који их одведу као заробљенике у земљу, било далеко или близу, 37ако тада дођу к себи у земљи у којој су заробљени и покају се, те се почну молити теби у земљи својих поробљивача, говорећи: ’Згрешили смо, учинили смо неправду, скривили смо’, 38па се врате к теби свим срцем и свом душом у земљи ропства где су их поробили, и помоле се теби према својој земљи коју си дао њиховим оцима и према граду који си изабрао и према Дому који сам саградио за твоје име, 39ти чуј с небеса, твог Пребивалишта, њихову молитву и молбу, и учини им по правди. Тада опрости своме народу, који је згрешио против тебе.

40А сада те молим, о, мој Боже, отвори своје очи и ушима пажљиво послушај молитве са овог места.

41Уздигни се сад, о, Господе Боже, на место свог починка;

ти и Ковчег Силе твоје!

Свештеници нек огрну спасење,

твоји верни добру нек се радују.

42О, Господе Боже, не окрећи се од лица свог помазаника

и сети се савеза милости према Давиду, свом слузи!“