2 Mbiri 4 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 4:1-22

Zipangizo za mʼNyumba ya Mulungu

1Solomoni anapanga guwa lamkuwa limene mulitali mwake linali mamita asanu ndi anayi, mulifupi mwakenso mamita asanu ndi anayi ndipo msinkhu wake unali mamita anayi ndi theka. 2Kenaka iye anapanga mbiya yayikulu yachitsulo. Inali yozungulira ndipo pakamwa pake panali pa mamita anayi ndi theka, poyeza modutsa pakati pake. Msinkhu wake unali wopitirirapo mamita awiri. Thunthu lake linali mamita 13. 3Mʼmunsi mwa mkombero wa mbiyayo anajambulamo zithunzi zangʼombe zazimuna mozungulira, zithunzi khumi pa theka la mita. Ngʼombezo zimajambulidwa mʼmizere iwiri ndipo anazipangira kumodzi ndi mbiyayo.

4Mbiyayo anayisanjika pa ngʼombe zamkuwa khumi ndi ziwiri, zitatu zoyangʼana kumpoto, zitatu zoyangʼana kumadzulo, zitatu zoyangʼana kummwera ndipo zitatu zoyangʼana kummawa. Mbiyayo inakhazikika pamwamba pa ngʼombezo, ndipo miyendo yake yonse yakumbuyo ya ngʼombezo inkaloza mʼkati. 5Mbiyayo inali yochindikala ngati chikhatho ndipo mkombero wake unali ngati mkombero wa chikho, ngati duwa lokongola kwambiri. Mʼmbiyamo munkalowa madzi okwana malita 60,000.

6Kenaka anapanga mabeseni khumi otsukira zinthu ndipo asanu amawayika mbali ya kummwera, asanu mbali ya kumpoto. Mʼmenemo amatsukiramo zinthu zimene zimagwiritsidwa ntchito pa nsembe zopsereza koma mbiyamo ndi mʼmene ankasambiramo ansembe.

7Solomoni anapanga zoyikapo nyale khumi zagolide monga momwe kunalembedwera ndipo anaziyika mʼNyumba ya Mulungu, zisanu mbali ya kummwera, ndi zisanu mbali ya kumpoto.

8Iye anapanga matebulo khumi ndipo anawayika mʼNyumba ya Mulungu, asanu mbali ya kummwera ndi asanu mbali ya kumpoto. Iye anapanganso mabeseni agolide okwanira 100.

9Iye anapanga bwalo la ansembe, bwalo lalikulu ndi zitseko za bwalolo ndipo anakuta zitsekozo ndi mkuwa. 10Anayika mbiya ija mbali yakummwera pamene mbali ya kummawa ndi kummwera zimakumana.

11Iye anapanganso miphika ndi mafosholo ndi mabeseni owazira magazi.

Kotero Hiramu anatsiriza ntchito yonse ya ku Nyumba ya Mulungu imene ankagwirira Mfumu Solomoni:

12Nsanamira ziwiri;

mbale ziwiri za mitu yapamwamba pa nsanamirazo;

maukonde awiri okongoletsera mbale ziwiri za mitu yapamwamba pa nsanamirazo;

13makangadza 400 a maukonde awiri okongoletserawo (mizere iwiri ya makangadza pa ukonde uliwonse, kukongoletsa mbale za mitu yapamwamba pa nsanamira);

14miyendo pamodzi ndi mabeseni ake;

15mbiya pamodzi ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri zazimuna zosanjikapo mbiyayo.

16Miphika, mafosholo, mafoloko otengera nyama ndi ziwiya zina zonse.

Zipangizo zonse zimene Hiramu Abi anapangira Mfumu Solomoni za mʼNyumba ya Yehova zinali zamkuwa wonyezimira. 17Mfumu inapangitsa zimenezi mʼchigwa cha Yorodani, ku malo amtapo amene anali pakati pa Sukoti ndi Zaretani. 18Zinthu zonse zimene Solomoni anapanga zinali zochuluka kwambiri kotero kuti kulemera kwa mkuwa sikunadziwike.

19Solomoni anapanganso ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Mulungu:

guwa lansembe lagolide;

matebulo pamene ankayikapo buledi woperekedwa kwa Mulungu;

20zoyikapo nyale zagolide ndi nyale zake zagolide weniweni, kuti ziziyaka mʼkati mwenimweni mwa malo opatulika monga analembera,

21maluwa agolide, nyale ndi mbaniro. (Zinali zagolide mmodzi);

22zozimitsira nyale zagolide weniweni, mbale zowazira magazi, mbale ndi zofukizira; ndiponso zitseko zagolide za Nyumba ya Mulungu, chitseko cha ku Malo Opatulika Kwambiri ndi zitseko za ku chipinda chachikulu.

New Serbian Translation

2. Књига дневника 4:1-22

Опрема Дома Господњег

1И направи Соломон бронзани жртвеник, двадесет лаката дуг и широк, а десет лаката4,1 Око 10 m дуг и око 5 m висок. висок. 2Затим је израдио море од искованог метала. Било је сасвим округло и имало је десет лаката од једног краја до другог, било је пет лаката високо, а у обиму је било тридесет лаката4,2 Око 5 m од једног краја до другог, око 2,5 m висине и око 15 m у обиму., мерено ужетом. 3Ликови волова су били изливени свуда около, окружујући море унаоколо по десет у лакту4,3 1 лакат око 50 cm.. У два реда су били волови, саливени с морем.

4Море је стајало на дванаест волова; три су гледала на север, три су гледала на запад, три су гледала на југ, а три су гледала на исток. Море је стајало на њима одозго, а њихова задња страна је била унутра. 5Дебљина му је била један педаљ4,5 Око 23 cm., а руб му је био као руб чаше, као цвет љиљана, и примало је три хиљаде вата.4,5 Око 66 m³, тј. килолитара.

6Соломон је направио десет посуда и ставио пет са леве и пет са десне стране, за прање онога што се приноси као жртве свеспалнице. Море је изливено за прање свештеника.

7Направио је десет златних свећњака, према пропису, и ставио их у Дом – пет са десне, а пет са леве стране.

8Десет столова је поставио у Дом, пет са десне, а пет са леве стране; и стотину златних чинија.

9Затим двориште за свештенике, велико двориште и врата за њих обложена бронзом. 10Море је поставио с десне стране ка југоистоку.

11Хирам је направио и умиваонице, лопатице и котлиће.

Тако је Хирам довршио сав посао који је радио за цара Соломона на Дому Господњем.

12Два стуба и два округла оглавља на врху два стуба, и две плетенице да покривају та два оглавља на врху два стуба;

13четири стотине нарова на две плетенице; два реда нарова на свакој плетеници, да покривају два округла оглавља на врху стубова;

14десет подножја и десет умиваоница на њима;

15једно море и дванаест волова испод њега;

16лонце, лопатице, виљушке и сву другу опрему од углачане бронзе.

То је Хирам-Ави направио за Дом Господњи цара Соломона. 17Цар их је лио у глиненим калупима, у долини Јордана између Сокота и Сартана. 18Направио је све те многе судове од бронзе; није се тражио извештај о тежини бронзе.

19Соломон је направио и све остало посуђе које је било у Дому Господњем:

златни жртвеник,

златне столове на којима је био принесени хлеб;

20свећњаке од чистог злата са жишцима који горе према прописима испред Светиње над светињама;

21латице, светиљке, машице – све од чистог, беспрекорног злата;

22усекаче и котлиће; кадионице и тепсије од чистог злата; златне преворнице за врата унутрашњег Дома – за Светињу над светињама и за врата велике дворане.