2 Mbiri 3 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 3:1-17

Solomoni Amanga Nyumba ya Mulungu

1Pamenepo Solomoni anayamba kumanga Nyumba ya Yehova mu Yerusalemu pa Phiri la Moriya, pamene Yehova anaonekera Davide abambo ake. Panali pabwalo lopunthirapo tirigu la Arauna Myebusi, malo amene anapereka Davide. 2Iye anayamba kumanga pa tsiku lachiwiri la mwezi wachiwiri mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake.

3Maziko amene Solomoni anayika pomanga Nyumba ya Mulungu ndi awa: Mulitali munali mamita 27, mulifupi munali mamita asanu ndi anayi (potsata miyeso yakale). 4Chipinda cha polowera mulitali mwake chinali mamita asanu ndi anayi ofanana ndi mulifupi mwake mwa nyumbayo. Msinkhu wake unali mamita 54.

Iye anakuta nyumbayo mʼkati mwake ndi golide woyengeka bwino. 5Chipinda chachikulu, khoma lake anakhomera matabwa a payini ndipo analikutira ndi golide wabwino ndi kulikongoletsa ndi zithunzi za kanjedza ndi maunyolo. 6Iye anakongoletsa Nyumba ya Mulunguyo ndi miyala yokongola. Ndipo golide amene anagwiritsa ntchito anali golide wa ku Paravaimu. 7Iye anakutira ndi golide mitanda ya ku denga, maferemu a zitseko, makoma ndi zitseko za Nyumba ya Mulungu, ndipo anajambula Akerubi mʼmakoma mwake.

8Iye anamanga Malo Opatulika Kwambiri ndipo mulitali mwake munali mofanana ndi mulifupi mwa Nyumba mamita asanu ndi anayi. Anakuta mʼkati mwake ndi golide wosalala wolemera matani makumi awiri. 9Misomali yagolide imalemera magalamu 570. Anakutanso ndi golide zipinda zapamwamba.

10Ku Malo Opatulika Kwambiri iye anapangako Akerubi awiri achitsulo ndipo anawakuta ndi golide. 11Kutalika kwa mapiko onse a Akerubi kunali mamita asanu ndi anayi. Phiko la Kerubi woyamba linali loposerapo mamita awiri ndipo limakhudza khoma la Nyumba ya Mulungu, pamene phiko linalo, lotalikanso koposerapo mamita awiri, limakhudza phiko la Kerubi winayo. 12Chimodzimodzinso phiko la Kerubi wachiwiri linali loposerapo mamita awiri ndipo limakhudza mbali ina ya khoma la Nyumba ya Mulungu, ndipo linalo limene linalinso loposera mamita awiri, limakhudza phiko la Kerubi woyamba uja. 13Mapiko a Akerubiwa akawatambasula amatalika mamita asanu ndi anayi. Akerubiwa anayimirira pa mapazi awo, kuyangʼana chipinda chachikulu.

14Solomoni anapanga nsalu zotchingira zobiriwira, zapepo ndi zofiira ndi nsalu zofewa zosalala, atajambulapo Akerubi.

15Kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu anamangako zipilala ziwiri, zimene zonse pamodzi zinali zotalika mamita khumi ndi asanu ndi theka; chipilala chilichonse chinali ndi mutu woposera mamita awiri. 16Iye anapanga maunyolo olumikizanalumikizana ndipo anawayika pamwamba pa zipilalazo. Anapanganso makangadza 100 ndipo anawalumikiza ku maunyolo aja. 17Solomoni anayimika nsanamirazo kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu, imodzi mbali ya kummwera ndi inayo mbali ya kumpoto. Nsanamira ya kummwera anayitcha Yakini ndipo ya kumpoto anayitcha Bowazi.

New Serbian Translation

2. Књига дневника 3:1-17

Соломон зида Дом Господњи

1Соломон је почео да зида Дом Господњи у Јерусалиму, на брду Морији, где се Господ објавио његовом оцу Давиду. То је место Давид већ припремио на гумну Јевусејца Орне. 2Он је почео да зида другог дана, другог месеца, четврте године своје владавине.

3И постави темеље Соломон за Дом Господњи, по старим мерама у дужину шездесет лаката а у ширину двадесет лаката.3,3 Око 30 m у дужину и око 10 m у ширину. 4Трем се налазио с прочеља Дома и одговарао је његовој ширини – двадесет лаката3,4 Око 10 m. – а био је висок стотину двадесет лаката.3,4 Око 60 m, док је према неким преписима Септуагинте и према арамејском тексту реч о двадесет лаката, тј. 10 m.

Изнутра је био обложен чистим златом. 5Највеће површине Дома је обложио чемпресовим дрветом и чистим златом, а сводове украсио палмама и ланцима. 6Ради лепоте, Дом је украсио драгим камењем и златом из Парваима. 7Златом обложи и греде, прагове, зидове, врата, а на зидовима је изрезбарио златне херувиме.

8У Дому је, по његовој дужини сазидао Светињу над светињама. Њена дужина и ширина су били двадесет лаката3,8 Око 10 m.. Обложио ју је са шест стотина таланата3,8 Око 20 t. чистог злата. 9Позлаћени ексери су тежили педесет шекела,3,9 Око 575 gr. а и горње просторије је обложио златом.

10У Светињи над светињама уметници су излили два херувима и обложили их златом. 11Крила херувима су била дуга двадесет лаката, а свако од њих пет лаката3,11 Око 10 m дуга а свако око 2,5 m.. Први је једним крилом дотицао крило другог, а другим крилом зид одаје. 12И други је крилом, пет лаката3,12 Око 2,5 m. дугим, дотицао зид, а другим се спајао са исто толико дугим крилом првог. 13Двадесет лаката3,13 Око 10 m. у дужину имају крила кад су раширена, а херувими су стајали на ногама лицем окренути према Дому.

14Сашио је завесу од раскошног гримизног и скерлетног платна, од финог лана и извезао по њему херувиме.

15Испред Дома је подигао два стуба висока тридесет пет лаката, који су на врху имали пет лаката дуга оглавља3,15 Око 17,5 m висине са 2,5 m дугим оглављима.. 16Поставио је ланце у Светињи над светињама и њима оплео врх стубова, а ланце је украсио са стотину нарова. 17Стубове је поставио испред Дома, један с леве, а други с десне стране. Десног је назвао Јакин а левог Воаз.