2 Mbiri 24 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 24:1-27

Yowasi Akonzanso Nyumba ya Mulungu

1Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba. 2Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada. 3Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.

4Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova. 5Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.

6Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”

7Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.

8Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova. 9Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu. 10Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza. 11Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri. 12Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.

13Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa. 14Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.

15Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130. 16Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.

Kuyipa kwa Yowasi

17Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera. 18Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu. 19Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.

20Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’ ”

21Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu. 22Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”

23Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko. 24Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi. 25Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.

26Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu. 27Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Bibelen på hverdagsdansk

2. Krønikebog 24:1-27

Joash og Jojada sætter templet i stand

2.Kong. 12,1-16

1Joash var syv år gammel, da han blev konge, og han regerede i Jerusalem i 40 år. Hans mor hed Zibja og var fra Be’ersheba. 2Han gjorde, hvad der var ret i Herrens øjne, så længe præsten Jojada levede og kunne rådgive ham. 3Jojada udvalgte to koner til kongen, og de fødte ham sønner og døtre.

4Nogen tid senere besluttede Joash at sætte Herrens hus i stand, 5og derfor sammenkaldte han præsterne og levitterne og sagde til dem: „Tag rundt til alle Judas byer for at indsamle den årlige tempelskat fra alle israelitter, så jeres Guds hus kan blive restaureret. Skynd jer af sted!” Men levitterne skyndte sig overhovedet ikke.

6Senere kaldte han ypperstepræsten Jojada til sig og spurgte: „Hvorfor sørger du ikke for, at levitterne opkræver den tempelskat i Jerusalem og Judas byer, som Herrens tjener Moses bestemte skulle indsamles hvert år til åbenbaringsteltet?”

7Den onde Ataljas folk var nemlig brudt ind i Guds hus og havde stjålet de hellige redskaber for at bruge dem til deres afgudsdyrkelse. 8Men nu befalede kongen, at levitterne skulle lave en stor indsamlingskiste og anbringe den uden for porten ind til Herrens hus. 9Derpå sendte han en ordre ud i hele landet, om at folk skulle komme med den skat til Herren, som Guds tjener Moses i sin tid i ørkenen havde forordnet skulle betales hvert år. 10Alle lederne og folket syntes godt om forslaget, og de kom og lagde deres guld- og sølvstykker i kisten. 11Hver aften bar levitterne kisten indenfor, og den blev bevogtet af kongens mænd. Når kisten var fuld, kom statssekretæren og ypperstepræstens repræsentant og tømte kisten for penge, hvorefter den blev bragt tilbage på sin plads. På den måde blev der indsamlet en stor sum penge.

12Kongen og Jojada gav pengene videre til arbejdsformændene, som udbetalte løn til stenhuggerne, tømrerne og metalarbejderne, der udførte restaureringsarbejdet. 13Alle sled hårdt i det, og snart var restaureringen fuldført. 14Efter at alle udgifter var betalt, blev de tiloversblevne guld- og sølvstykker overgivet til kongen og Jojada, som besluttede at smelte dem om til skåle og diverse redskaber af guld og sølv til brug under offerhandlingerne i Herrens hus.

Så længe Jojada levede, gennemførte man de regelmæssige ofre i templet. 15Han blev meget gammel—130 år—før han døde. 16På grund af sin store indsats for Israels folk, for Gud og for templet fik han en ærefuld begravelse i det kongelige gravsted i Davidsbyen.

Resten af Joash’ tid som konge i Juda

2.Kong. 12,17-21

17-18Men efter Jojadas død kom Judas ledere til kong Joash og overtalte ham til at opgive deres forfædres Guds tempel og dyrke afgudsbilleder og Asherapæle i stedet. Derfor ramte Guds vrede Juda og Jerusalem igen. 19Men først sendte han sine profeter for at advare folket og få dem til at adlyde ham, men ingen ville høre på dem.

20Da kom Guds Ånd over Zekarja, Jojadas søn, og han stillede sig op i forgården til templet og talte til folket: „Gud siger: Hvorfor overtræder I Herrens befalinger? Det fører kun ulykke med sig. I har vendt jer fra ham, og derfor vender han sig fra jer!”

21Lederne stiftede derpå en sammensværgelse for at skaffe Zekarja af vejen, og det lykkedes dem at overtale kongen til at udtale en dødsdom over Zekarja, så han blev stenet til døde i forgården til templet. 22Det var den måde, kong Joash gengældte Jojada for hans troskab—ved at dræbe hans søn! Zekarjas sidste ord lød: „Må Herren se det og straffe dem!”

23Ved årsskiftet gik den aramæiske hær til angreb på Juda og Jerusalem. Efter at have dræbt alle lederne sendte de et mægtigt krigsbytte tilbage til deres konge i Damaskus. 24Selv om aramæerne kom med en lille hær, lykkedes det dem at besejre den langt større judæiske hær, for det var Herren, der gav dem sejren. Judæerne havde jo vendt sig fra deres forfædres Gud. På den måde brugte Gud aramæerne til at straffe Joash.

25Da aramæerne trak sig tilbage, efterlod de Joash alvorligt såret. Da besluttede nogle af hans embedsmænd at slå ham ihjel som straf, fordi han havde dræbt ypperstepræsten Jojadas søn. De snigmyrdede ham i hans seng, hvorefter han blev begravet i Davidsbyen, men ikke i det kongelige gravsted. 26Attentatmændene var Zabad,24,26 „Zabad” er det samme som „Jozabad”. Sandsynligvis en kopieringsfejl. Der skulle nok have stået „(Jo)Zakar” som i 2.Kong. 12,22 (LXX). søn af Shimat fra Ammon, og Jozabad, søn af Shimrit fra Moab. 27Beretningen om Joash’ sønner, de mange profetier imod ham og yderligere detaljer om templets restaurering er nedskrevet i kommentaren til Kongernes Bog.

Hans søn Amatzja efterfulgte ham på tronen.