2 Mbiri 23 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 23:1-21

1Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri. 2Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu, 3msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu.

Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide. 4Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo, 5ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova. 6Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula. 7Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”

8Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite. 9Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu. 10Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.

11Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”

12Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko. 13Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”

14Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,” 15choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.

16Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova. 17Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.

18Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira. 19Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.

20Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka, 21ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

2 Летопись 23:1-21

Восстание против Аталии

(4 Цар. 11:4-20)

1На седьмом году правления Аталии Иодай решился действовать. Он заключил союз с сотниками: Азарией, сыном Иерохама, Исмоилом, сыном Иоханана, Азарией, сыном Овида, Маасеей, сыном Адаи, и Элишафатом, сыном Зихри. 2Они прошли по всей Иудее и собрали левитов и глав исроильских семейств из всех городов. Когда они пришли в Иерусалим, 3всё собрание заключило в храме Всевышнего соглашение с царём.

Иодай сказал им:

– Вот сын царя! Он должен править, как и обещал Вечный о потомках Довуда. 4И вот что вы должны сделать: треть из вас – священнослужители и левиты, которые заступают на службу по субботам, – должны стеречь двери храма, 5треть из вас – царский дворец, треть – ворота Основания, а весь народ должен находиться во дворах храма Вечного. 6Пусть никто не входит в храм Вечного, кроме священнослужителей и левитов, которые на службе, – они могут войти, потому что освятились, а весь остальной народ должен оставаться снаружи, как и повелел им Вечный. 7Левиты должны встать вокруг царя, каждый с оружием в руках. Всякого, кто войдёт в храм, следует убивать. Будьте при царе, куда бы он ни пошёл.

8Левиты и все мужчины Иудеи сделали всё так, как приказал священнослужитель Иодай. Каждый взял своих людей – и тех, кто заступал на службу в ту субботу, и тех, кто в ту субботу уходил со службы, потому что священнослужитель Иодай не отпустил ни одного из групп священнослужителей. 9Он раздал сотникам копья с большими и маленькими щитами, которые некогда принадлежали царю Довуду и находились в храме Вечного. 10Он поставил всех людей, каждого с оружием в руках, вокруг царя – от южной стороны храма до северной, вокруг жертвенника и храма.

11Иодай и его сыновья вывели сына царя, возложили на него корону, дали ему копию Закона и провозгласили его царём. Его помазали и воскликнули:

– Да здравствует царь!

12Услышав шум народа, бегущего и выкрикивающего приветствия царю, Аталия отправилась к ним в храм Вечного. 13Она посмотрела и увидела: у царской колонны при входе стоял царь! Возле него были начальники отрядов и трубачи, и весь народ страны ликовал и трубил в трубы, а певцы с музыкальными инструментами пели прославляющие песни. Аталия разорвала на себе одежду и закричала:

– Заговор! Заговор!

14Священнослужитель Иодай вызвал сотников, которые распоряжались войском, и сказал им:

– Выведите её за пределы храма и убейте мечом всякого, кто за ней пойдёт.

(Потому что священнослужитель сказал: «Не предавайте её смерти в храме Вечного».)

15Её схватили и привели к входу Конских ворот царского дворца, и там её предали смерти.

16А Иодай заключил соглашение, что он сам, народ и царь будут народом Вечного. 17Весь народ пошёл к храму Баала и разрушил его. Они разбили на куски жертвенники и идолов и убили перед жертвенниками Маттана, жреца Баала.

18Затем Иодай поручил присмотр за храмом Вечного священнослужителям-левитам. Им Довуд определил служение в храме, чтобы они приносили всесожжения Вечному, как написано в Законе Мусо, с радостью и пением, как приказал Довуд. 19Ещё он поставил у ворот храма Вечного привратников, чтобы тот, кто был почему-либо нечист, не мог туда войти.

20Он взял с собой сотников, приближённых царя, правителей и весь народ страны, и они вместе вывели царя из храма Вечного и вошли в царский дворец через Верхние ворота. Они посадили царя на царский престол, 21и весь народ страны ликовал. А город, после того как Аталия была убита мечом, успокоился.