2 Mbiri 2 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 2:1-18

Kukonzekera Kumanga Nyumba ya Mulungu

1Solomoni anatsimikiza zoti amange Nyumba ya Dzina la Yehova ndi nyumba yake yaufumu. 2Iye analemba ntchito anthu 70,000 onyamula katundu ndi anthu 80,000 okumba miyala ku mapiri ndiponso akapitawo 3,600 oyangʼanira anthuwo.

3Solomoni anatumiza uthenga uwu kwa Hiramu mfumu ya ku Turo:

“Munditumizire mitengo ya mkungudza monga munachitira ndi abambo anga pamene munawatumizira mitengo ya mkungudza yomangira nyumba yaufumu yokhalamo. 4Tsono ine ndikufuna kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wanga ndi kuyipereka kwa Iye kuti tiziyikamo buledi wopatulika nthawi zonse ndiponso kuperekeramo nsembe zopsereza mmawa uliwonse ndi madzulo ndi pa masabata ndi pa masiku a chikondwerero cha mwezi watsopano ndiponso pa masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova Mulungu wathu, monga mwa malamulo a Aisraeli mpaka muyaya.

5“Nyumba ya Mulungu imene ndidzamange idzakhala yayikulu, chifukwa Mulungu wathu ndi wamkulu kuposa milungu ina yonse. 6Koma ndani angathe kumumangira Iye Nyumba, pakuti mlengalenga, ngakhale kumwamba kwenikweni sikungamukwane? Tsono ine ndine yani kuti ndimangire Iyeyo Nyumba, kupatula malo chabe opserezerapo nsembe pamaso pake?

7“Tsono tumizireni munthu waluso pa ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, nsalu yapepo ndi yofiira ndi yobiriwira ndiponso waluso losema, kuti adzagwire ntchito mu Yuda ndi Yerusalemu pamodzi ndi anthu aluso amene abambo anga Davide anandipatsa.

8“Munditumizirenso mitengo ya mkungudza, payini ndiponso matabwa a mʼbawa wa ku Lebanoni, pakuti ndikudziwa kuti anthu anu ali ndi luso locheka matabwa kumeneko. Antchito anga adzagwira ntchito pamodzi ndi antchito anu 9kuti andipatse matabwa ambiri, chifukwa Nyumba imene ndikumanga iyenera kukhala yayikulu ndi yokongola. 10Ine ndidzalipira antchito anu amene adzacheke matabwa matani 1,000 a tirigu wopunthapuntha, matani 2,000 a barele, malita 440,000 a vinyo, ndiponso malita 440,000 a mafuta a olivi.”

11Hiramu, mfumu ya ku Turo, anamuyankha Solomoni pomulembera kalata kuti,

“Chifukwa Yehova amakonda anthu ake, wayika iwe kukhala mfumu yawo.”

12Ndipo Hiramu anawonjezera kunena kuti,

“Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi! Iye wamupatsa Davide mwana wanzeru, wodzaza ndi luntha ndi wozindikira, amene adzamanga Nyumba ya Mulungu ndi kudzimangira yekha nyumba yaufumu.

13“Ine ndikukutumizira Hiramu Abi, munthu wa luso lalikulu, 14amene amayi ake anali wochokera ku Dani ndipo abambo ake anali a ku Turo. Iye anaphunzitsidwa kugwira ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, miyala yokongola ndi matabwa, ndiponso nsalu zofewa zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Alinso ndi luso la zosemasema ndipo atha kupanga chilichonse chimene wapatsidwa. Iye adzagwira ntchito ndi amisiri anu ndi a mbuye wanga, Davide abambo anu.

15“Tsono mbuye wanga tumizirani antchito anu tirigu ndi barele, mafuta a olivi ndi vinyo zimene mwalonjeza, 16ndipo ife tidzadula mitengo yonse imene mukuyifuna kuchokera ku Lebanoni ndipo tidzayimanga pamodzi ndi kuyiyadamitsa pa madzi mpaka ku Yopa. Ndipo inu mudzatha kuyitenga mpaka ku Yerusalemu.”

17Solomoni anawerenga alendo onse amene anali mu Israeli, potsatira chiwerengero chimene abambo ake Davide anachita ndipo panapezeka kuti analipo anthu 153,600. 18Iye anayika anthu 70,000 kuti akhale onyamula katundu ndi anthu 80,000 kuti akhale ophwanya miyala mʼmapiri, anthu 3,600 anawayika kukhala akapitawo oyangʼanira anthu pa ntchitoyo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

2 Летопись 2:1-18

Подготовка к строительству храма

(3 Цар. 5:1-18)

1Сулейман повелел построить храм для поклонения Вечному и дворец для себя. 2Он поставил семьдесят тысяч человек работать носильщиками, восемьдесят тысяч – каменотёсами в горах и три тысячи шестьсот – начальниками над ними2:2 В этой книге говорится о 3 600 начальниках и о 250 главных начальниках (см. 8:10), а в 3 Цар. о 3 300 начальниках (3 Цар. 5:16) и о 550 главных начальниках (9:23), но при этом сохраняется общее число 3 850 человек..

3Сулейман послал сказать царю Тира Хираму:

«Присылай мне кедровые брёвна, как присылал их моему отцу Давуду, когда он строил себе дворец. 4Я хочу построить храм для поклонения Вечному, моему Богу, и посвятить его Ему, чтобы возжигать перед Ним благовония, постоянно выставлять священный хлеб и каждое утро, каждый вечер, по субботам, в Новолуния и в установленные праздники Вечного, нашего Бога, приносить всесожжения2:4 См. таблицы: «Праздники в Исраиле» и «Жертвоприношения в Исраиле» на странице ##.. Таково вечное установление для Исраила.

5Храм, который я хочу построить, будет велик, потому что велик наш Бог, превыше всех других богов. 6Но кто в силах построить Ему дом, если небеса и даже небеса небес не могут Его вместить? И кто я, чтобы строить Ему дом? Это лишь будет место для жертвоприношений Ему.

7Итак, пришли мне человека, искусного в работе по золоту и серебру, бронзе и железу, а также в работе с пурпурной, алой и голубой пряжей и в искусстве резьбы, чтобы он работал в Иудее и в Иерусалиме с моими искусными мастерами, которых выбрал Давуд, мой отец.

8Ещё пришли мне с Ливана брёвен из кедра, сосны и красного дерева, потому что я знаю, что твои люди умеют рубить деревья на Ливане. Мои люди будут работать вместе с твоими, 9чтобы заготовить мне дерева в избытке, потому что храм, который я строю, должен быть большим и величественным. 10Я дам дровосекам, твоим слугам, которые рубят деревья, три с половиной тысячи тонн смолотой пшеницы, столько же ячменя, четыреста сорок тысяч литров2:10 Букв.: «двадцать тысяч ко́ров… двадцать тысяч батов». вина и столько же оливкового масла».

11Хирам, царь Тира, ответил Сулейману в письме:

«Вечный любит Свой народ и поэтому сделал тебя его царём».

12И ещё добавил:

«Хвала Вечному, Богу Исраила, который создал небо и землю! Он даровал Давуду мудрого сына, наделённого разумом и проницательностью, который построит храм для Вечного и дворец для себя.

13Я посылаю к тебе Хурам-Ави, искуснейшего ремесленника, 14мать которого была из рода Дана, а отец был уроженцем Тира. Он опытен в работе по золоту и серебру, бронзе и железу, камню и дереву, а также в работе с пурпурной, голубой и алой пряжей и с тонкими льняными тканями. Он опытен во всякого рода резьбе и может выполнить любой данный ему заказ. Он будет работать с твоими мастерами и с мастерами моего господина Давуда, твоего отца.

15Итак, пусть мой господин пошлёт своим рабам пшеницу, ячмень, оливковое масло и вино, которые он обещал, 16и мы нарубим деревьев на Ливане столько, сколько тебе нужно, сплавим их плотами по морю в Иоппию, и ты сможешь перевезти их в Иерусалим».

17Сулейман сделал перепись всех чужеземцев, живших в Исраиле, после той переписи, которую сделал его отец Давуд, и их оказалось сто пятьдесят три тысячи шестьсот человек. 18Он поставил семьдесят тысяч человек из них работать носильщиками, восемьдесят тысяч – каменотёсами в горах и три тысячи шестьсот – начальниками, чтобы они побуждали народ работать.