2 Mbiri 3 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 3:1-17

Solomoni Amanga Nyumba ya Mulungu

1Pamenepo Solomoni anayamba kumanga Nyumba ya Yehova mu Yerusalemu pa Phiri la Moriya, pamene Yehova anaonekera Davide abambo ake. Panali pabwalo lopunthirapo tirigu la Arauna Myebusi, malo amene anapereka Davide. 2Iye anayamba kumanga pa tsiku lachiwiri la mwezi wachiwiri mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake.

3Maziko amene Solomoni anayika pomanga Nyumba ya Mulungu ndi awa: Mulitali munali mamita 27, mulifupi munali mamita asanu ndi anayi (potsata miyeso yakale). 4Chipinda cha polowera mulitali mwake chinali mamita asanu ndi anayi ofanana ndi mulifupi mwake mwa nyumbayo. Msinkhu wake unali mamita 54.

Iye anakuta nyumbayo mʼkati mwake ndi golide woyengeka bwino. 5Chipinda chachikulu, khoma lake anakhomera matabwa a payini ndipo analikutira ndi golide wabwino ndi kulikongoletsa ndi zithunzi za kanjedza ndi maunyolo. 6Iye anakongoletsa Nyumba ya Mulunguyo ndi miyala yokongola. Ndipo golide amene anagwiritsa ntchito anali golide wa ku Paravaimu. 7Iye anakutira ndi golide mitanda ya ku denga, maferemu a zitseko, makoma ndi zitseko za Nyumba ya Mulungu, ndipo anajambula Akerubi mʼmakoma mwake.

8Iye anamanga Malo Opatulika Kwambiri ndipo mulitali mwake munali mofanana ndi mulifupi mwa Nyumba mamita asanu ndi anayi. Anakuta mʼkati mwake ndi golide wosalala wolemera matani makumi awiri. 9Misomali yagolide imalemera magalamu 570. Anakutanso ndi golide zipinda zapamwamba.

10Ku Malo Opatulika Kwambiri iye anapangako Akerubi awiri achitsulo ndipo anawakuta ndi golide. 11Kutalika kwa mapiko onse a Akerubi kunali mamita asanu ndi anayi. Phiko la Kerubi woyamba linali loposerapo mamita awiri ndipo limakhudza khoma la Nyumba ya Mulungu, pamene phiko linalo, lotalikanso koposerapo mamita awiri, limakhudza phiko la Kerubi winayo. 12Chimodzimodzinso phiko la Kerubi wachiwiri linali loposerapo mamita awiri ndipo limakhudza mbali ina ya khoma la Nyumba ya Mulungu, ndipo linalo limene linalinso loposera mamita awiri, limakhudza phiko la Kerubi woyamba uja. 13Mapiko a Akerubiwa akawatambasula amatalika mamita asanu ndi anayi. Akerubiwa anayimirira pa mapazi awo, kuyangʼana chipinda chachikulu.

14Solomoni anapanga nsalu zotchingira zobiriwira, zapepo ndi zofiira ndi nsalu zofewa zosalala, atajambulapo Akerubi.

15Kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu anamangako zipilala ziwiri, zimene zonse pamodzi zinali zotalika mamita khumi ndi asanu ndi theka; chipilala chilichonse chinali ndi mutu woposera mamita awiri. 16Iye anapanga maunyolo olumikizanalumikizana ndipo anawayika pamwamba pa zipilalazo. Anapanganso makangadza 100 ndipo anawalumikiza ku maunyolo aja. 17Solomoni anayimika nsanamirazo kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu, imodzi mbali ya kummwera ndi inayo mbali ya kumpoto. Nsanamira ya kummwera anayitcha Yakini ndipo ya kumpoto anayitcha Bowazi.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

2 Летопись 3:1-17

Сулейман строит храм

(3 Цар. 6:1-38)

1И Сулейман начал строить храм Вечного в Иерусалиме на горе Мория, где Вечный явился его отцу Давуду. Это было на гумне иевусея Арауны3:1 Букв.: «Орнан»; во 2 Цар. 24:16 он назван Арауной., на месте, которое приготовил Давуд. 2Он начал строить во второй день второго месяца в четвёртый год своего правления (в середине весны 966 г. до н. э.).

3Вот размеры основания, на котором Сулейман строил храм Аллаха: тридцать метров3:3 Букв.: «шестьдесят локтей». в длину и десять метров3:3 Букв.: «двадцать локтей», также в ст. 4, 8, 11 и 13. в ширину. 4Притвор перед храмом был десять метров в длину, соответственно ширине храма, и десять метров3:4 В других рукописях: «сто двадцать локтей», т. е. 60 м. в высоту. Изнутри он покрыл его чистым золотом.

5Сулейман обшил большой зал сосной, вызолотил его и украсил орнаментом из пальм и цепей. 6Он выложил храм драгоценными камнями и золотом, доставленным из Парваима. 7Он покрыл золотом потолочные балки, дверные рамы, стены и двери храма и вырезал на стенах херувимов3:7 Херувим – один из высших ангельских чинов. См. также пояснительный словарь..

8Затем он построил Святая Святых3:8 Святая Святых – внутренняя комната храма, где находился сундук соглашения., длина которого совпадала с шириной храма: по десять метров в длину и в ширину. Изнутри Сулейман покрыл его лучшим золотом весом в двадцать одну тонну и шестьсот килограммов3:8 Букв.: «шестьсот талантов».. 9Золотые гвозди весили шестьсот граммов3:9 Букв.: «пятьдесят шекелей».. Золотом он покрыл также и верхние комнаты.

10В Святая Святых он сделал двух херувимов резной работы и покрыл их золотом. 11Их крылья были длиной десять метров. Одно крыло первого херувима было два с половиной метра3:11 Букв.: «пять локтей», также в ст. 12. в длину и касалось стены храма, а второе крыло, такой же длины, касалось крыла другого херувима. 12Точно так же одно крыло второго херувима, длиной два с половиной метра, касалось противоположной стены храма, а второе крыло, такой же длины, касалось крыла первого херувима. 13Крылья этих херувимов простирались на десять метров. Они стояли на ногах, лицами к большому залу.

14Сулейман сделал завесу из голубой, пурпурной и алой пряжи и лучшего льна с изображёнными на ней херувимами.

Две бронзовые колонны

(3 Цар. 7:15-22)

15Перед храмом Сулейман сделал две колонны, общая длина которых была семнадцать с половиной метров. Капители на каждой из колонн были по два с половиной метра3:15 Букв.: «тридцать пять… пять локтей». высотой. 16Он сделал круговые цепи и украсил ими верхние части колонн. Ещё он сделал сто гранатовых плодов и прикрепил их к цепям. 17Он установил колонны перед храмом: одну с южной стороны и одну с северной. Ту, что с южной стороны, он назвал Иахин («Он утвердит»), а ту, что с северной стороны, – Боаз («в Нём сила»).