2 Mbiri 13 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 13:1-22

Abiya Mfumu ya Yuda

1Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda, 2ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka zitatu. Dzina la amayi ake linali Maaka mwana wa Urieli wa ku Gibeya.

Koma panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu. 3Abiya anapita ku nkhondo ndi asilikali odziwa bwino nkhondo 400,000, ndipo Yeroboamu anandandalitsa ankhondo, asilikali 800,000 odziwa bwino nkhondo, osankhidwa ndi amphamvu, woti amenyane naye.

4Abiya anayima pa phiri la Zemaraimu, mʼdziko lamapiri la Efereimu, ndipo anati, “Yeroboamu ndi Aisraeli onse, tandimverani! 5Kodi inu simukudziwa kuti Yehova, Mulungu wa Israeli, wapereka ufumu wa Israeli kwa Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya ndiponso pangano la mchere? 6Komabe Yeroboamu mwana wa Nebati, mtumiki wa Solomoni mwana wa Davide, anawukira mbuye wake. 7Ndipo anthu ena achabechabe anasonkhana kwa iye ndipo anatsutsana ndi Rehobowamu mwana wa Solomoni pamene anali wamngʼono ndi wosalimba mtima ndi wopanda mphamvu kuti athe kulimbana nawo.

8“Ndipo tsopano inu mwakonzekera kutsutsana ndi ufumu wa Yehova, umene uli mʼmanja mwa zidzukulu za Davide. Inu ndithu mulipo ankhondo ambirimbiri ndipo muli ndi ana angʼombe agolide amene Yeroboamu anapanga kuti akhale milungu yanu. 9Koma kodi inu simunathamangitse ansembe a Yehova, ana a Aaroni ndiponso Alevi ndi kudzisankhira ansembe anuanu monga anthu ena amachitira? Aliyense amene amabwera kuti adzipatule atatenga mwana wangʼombe wamwamuna ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri amakhala wansembe wa zinthu zimene sizili milungu.

10“Koma kunena za ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, ndipo sitinamusiye. Ansembe amene amatumikira Yehova ndi ana a Aaroni ndipo amathandizidwa ndi Alevi. 11Mmawa uliwonse ndi madzulo aliwonse amapereka nsembe zopsereza ndi kufukiza lubani kwa Yehova. Iwo amayika buledi pa tebulo loyeretsedwa monga mwa mwambo ndipo amayatsa nyale pa zoyikapo nyale zagolide madzulo aliwonse. Ife timachita zofuna za Yehova Mulungu wathu. Koma inu mwamusiya. 12Mulungu ali nafe pakuti ndiye mtsogoleri wathu. Ansembe ake atanyamula malipenga, adzayimba mfuwu wankhondo kulimbana nanu. Inu Aisraeli musalimbane ndi Yehova, Mulungu wa makolo anu, pakuti simungathe kupambana.”

13Tsono Yeroboamu anali atatumiza asilikali kumbuyo mowazungulira, kotero kuti iye ali kutsogolo kwa anthu a ku Yuda, anthu owabisalira anali kumbuyo kwawo. 14Asilikali a Yuda anatembenuka ndipo anaona kuti nkhondo imachitikira kutsogolo ndi kumbuyo. Ndipo iwo anafuwulira Yehova. Ansembe anayimba malipenga awo 15ndipo asilikali a Yuda anafuwula mawu ankhondo. Atafuwula mawu ankhondowo, Mulungu anagonjetsa Yeroboamu pamodzi ndi Aisraeli onse pamaso pa Abiya ndi Yuda. 16Aisraeli anathawa Ayuda. Ndipo Mulungu anawapereka mʼmanja mwawo. 17Abiya pamodzi ndi anthu ake anapha anthu ambiri, kotero kuti Aisraeli 500,000 odziwa bwino nkhondo anaphedwa. 18Ankhondo a Israeli anagonjetsedwa pa nthawi imeneyi, ndipo ankhondo a Yuda anapambana chifukwa anadalira Yehova, Mulungu wa makolo awo.

19Abiya anathamangitsa Yeroboamu ndipo anamulanda mizinda ya Beteli, Yesana, ndi Efroni pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. 20Yeroboamu sanapezenso mphamvu nthawi ya Abiya. Ndipo Yehova anamukantha nafa.

21Koma Abiya mphamvu zake zinakula. Iye anakwatira akazi 14 ndipo anali ndi ana aamuna 22 ndi ana aakazi 16.

22Zina ndi zina zokhudza Abiya, zimene anachita ndi zimene anayankhula, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mneneri Ido.

La Bible du Semeur

2 Chroniques 13:1-23

Abiya règne sur Juda

(1 R 15.1-2, 6)

1La dix-huitième année du règne de Jéroboam, Abiya devint roi de Juda. 2Il régna trois ans à Jérusalem13.2 De 913 à 910 av. J.-C.. Sa mère s’appelait Mikaya, elle était fille d’Ouriel, de Guibéa. Bientôt, il y eut guerre entre Abiya et Jéroboam.

3Abiya engagea le combat avec une armée de quatre cent mille guerriers valeureux, des soldats d’élite. Jéroboam lui opposa une armée de huit cent mille guerriers valeureux, des soldats d’élite. 4Abiya se tint debout sur le mont Tsemaraïm, situé dans la région montagneuse d’Ephraïm13.4 A une trentaine de kilomètres au nord de Jérusalem (voir Jos 18.22 qui parle d’une ville de ce nom)., et se mit à crier : Jéroboam et tout Israël, écoutez-moi ! 5Ne devriez-vous pas reconnaître que l’Eternel, le Dieu d’Israël, a donné pour toujours la royauté sur Israël à David et à ses descendants en vertu d’une alliance irrévocable13.5 Voir Nb 18.19 et la note. ? 6Mais Jéroboam, fils de Nebath, un serviteur de Salomon, fils de David, s’est révolté contre son maître. 7Des gens sans scrupules, des vauriens se sont groupés autour de lui et se sont opposés à Roboam, le fils de Salomon. Celui-ci était jeune et inexpérimenté, et il n’a pas pu leur résister. 8Et maintenant, croyez-vous que vous allez résister au pouvoir royal de l’Eternel qu’il a confié aux descendants de David ? Vous êtes une multitude nombreuse et vous avez avec vous les veaux d’or que Jéroboam a fabriqués pour vous servir de dieux13.8 Voir 1 R 12.26-33.. 9Mais vous avez chassé les prêtres de l’Eternel, les descendants d’Aaron, et les lévites, et vous vous êtes pris des prêtres comme le font les autres peuples ! Il suffit chez vous de se présenter avec un jeune taureau et sept béliers pour être investi du sacerdoce au service de dieux qui n’en sont pas. 10Quant à nous, c’est l’Eternel qui est notre Dieu : nous ne l’avons pas abandonné ; nos prêtres qui servent l’Eternel sont des descendants d’Aaron et ce sont les lévites qui les assistent. 11Chaque matin et chaque soir, nous offrons des holocaustes à l’Eternel, nous faisons fumer des parfums aromatiques, nous disposons sur la table rituellement pure les pains qui doivent être exposés devant l’Eternel13.11 Voir Lv 24.5-9., et chaque soir nous allumons les lampes du chandelier d’or. Nous suivons le rituel prescrit par l’Eternel notre Dieu, alors que vous, vous l’avez abandonné. 12Réfléchissez : Dieu est avec nous, il est notre chef, ses prêtres sont munis des trompettes13.12 Voir Nb 10.9. retentissantes, prêts à en sonner contre vous. Israélites ! Ne combattez pas contre l’Eternel, le Dieu de vos ancêtres, car vous ne réussirez pas dans cette entreprise !

13Jéroboam fit exécuter un mouvement tournant à une partie de ses troupes pour prendre les Judéens à revers ; le gros de ses troupes faisait face à celles de Juda, alors que les hommes embusqués se trouvaient derrière eux. 14Les troupes de Juda se virent donc attaquées à la fois par-devant et par-derrière. Alors les Judéens poussèrent des cris pour implorer l’Eternel et les prêtres sonnèrent des trompettes. 15En même temps, ils poussèrent le cri de guerre. Au bruit de la clameur des hommes de Juda, l’Eternel battit Jéroboam et toute l’armée d’Israël et les fit succomber devant Abiya et les Judéens. 16Les hommes d’Israël s’enfuirent devant Juda, et Dieu donna aux Judéens la victoire sur eux. 17Abiya et son armée leur infligèrent une grande défaite : cinq cent mille de leurs soldats d’élite tombèrent transpercés. 18Ce fut un jour d’humiliation pour ceux d’Israël, tandis que les Judéens remportèrent la victoire parce qu’ils s’étaient appuyés sur l’Eternel, le Dieu de leurs ancêtres.

19Abiya poursuivit Jéroboam et lui enleva plusieurs villes : Béthel, Yeshana et Ephrôn, avec toutes les localités qui en dépendaient. 20Pendant tout le règne d’Abiya, Jéroboam ne retrouva pas sa puissance ; finalement l’Eternel le frappa et il mourut. 21Au contraire, Abiya vit s’accroître sa puissance. Il épousa quatorze femmes et eut vingt-deux fils et seize filles.

(1 R 15.7-8)

22Les autres faits et gestes d’Abiya, sa conduite, ainsi que ses discours, sont cités dans le livre des Mémoires du prophète Iddo.

23Quand il rejoignit ses ancêtres décédés, on l’enterra dans la Cité de David, et son fils Asa lui succéda sur le trône13.23 Asa régna de 910 à 869 av. J.-C..

Le début du règne d’Asa en Juda

Sous le règne de ce dernier, le pays connut dix ans de paix.