2 Mbiri 12 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 12:1-16

Sisaki Athira Nkhondo Dziko la Yuda

1Rehobowamu atakhazikika monga mfumu nakhaladi wamphamvu, iyeyo pamodzi ndi Aisraeli onse anasiya malamulo a Yehova. 2Chifukwa anakhala osakhulupirika pamaso pa Yehova, Sisaki mfumu ya dziko la Igupto inathira nkhondo Yerusalemu mʼchaka chachisanu cha mfumu Rehobowamu. 3Sisakiyo anabwera ndi magaleta 1,200 ndi anthu okwera akavalo 60,000 ndiponso asilikali osawerengeka ochokera ku Libiya, Suki ndi Kusi amene anabwera naye kuchokera ku Igupto. 4Iye analanda mizinda yotetezedwa ya Yuda ndipo anafika mpaka ku Yerusalemu.

5Ndipo mneneri Semaya anabwera kwa Rehobowamu ndi kwa atsogoleri a Yuda amene anasonkhana mu Yerusalemu chifukwa cha Sisaki ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova akuti, ‘Inu mwandisiya, choncho Inenso ndakusiyani ndi kukuperekani kwa Sisaki.’ ”

6Atsogoleri a Israeli pamodzi ndi mfumu anadzichepetsa nati, “Yehova ndi wolungama.”

7Yehova ataona kuti adzichepetsa, anayankhula ndi Semaya kuti, “Pakuti adzichepetsa, Ine sindiwawononga koma posachedwapa ndiwapulumutsa. Sinditsanulira ukali wanga pa Yerusalemu kudzera mwa Sisaki. 8Komabe iwo adzakhala pansi pa ulamuliro wake, kuti aphunzire kudziwa kusiyanitsa pakati pa kutumikira Ine ndi kutumikira mafumu a mayiko ena.”

9Sisaki mfumu ya dziko la Igupto atathira nkhondo Yerusalemu, iye anatenga chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu. Iye anatenga zinthu zonse kuphatikizapo zishango zagolide zimene Solomoni anapanga. 10Ndipo mfumu inapereka zishango zamkuwa kwa oyangʼanira mʼmalo mwake ndipo iwo anazipereka kwa oyangʼanira alonda amene amayangʼanira pa chipata cha nyumba yaufumu. 11Nthawi ina iliyonse imene mfumu ikupita ku Nyumba ya Yehova, alonda amapita nayo atanyamula zishango, ndipo kenaka amakazibwezera ku chipinda cha alonda.

12Pakuti mfumu Rehobowamu inadzichepetsa, mkwiyo wa Yehova unamuchokera, sanawonongedweretu. Kunena zoona, munali zinthu zina zabwino mu Yuda.

13Mfumu Rehobowamu anayika maziko a ufumu wake mwamphamvu mu Yerusalemu ndipo anapitirira kukhala mfumu. Iye anali ndi zaka 41 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka 17 mu Yerusalemu, mzinda wa Yehova umene anasankha pakati pa mafuko a Aisraeli mmene Yehova anakhazikikamo. Dzina la amayi ake linali Naama, amene anali Mwamoni. 14Rehobowamu anachita zoyipa chifuwa mtima wake sunafunefune Yehova.

15Ntchito za Rehobowamu, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri la mneneri Semaya ndi mlosi Ido amene amalemba mbiri? Panali nkhondo yosatha pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu. 16Rehobowamu anamwalira, ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Ndipo mwana wake Abiya analowa ufumu mʼmalo wake.

La Bible du Semeur

2 Chroniques 12:1-16

L’invasion égyptienne

(1 R 14.21-31)

1Une fois que Roboam eut affermi son autorité royale et qu’il fut devenu puissant, il cessa d’obéir à la Loi de l’Eternel, et tout Israël avec lui. 2La cinquième année du règne de Roboam, Shishaq, roi d’Egypte12.2 Shishaq, fondateur de la XXIIe dynastie égyptienne, a régné de 945 à 924 av. J.-C. La cinquième année du règne de Roboam correspond à 925 av. J.-C., vint attaquer Jérusalem ; ce fut la conséquence de l’infidélité d’Israël envers l’Eternel. 3Shishaq vint d’Egypte avec mille deux cents chars et soixante mille soldats sur char. Il commandait une armée innombrable de soldats égyptiens, libyens, soukkiens et éthiopiens. 4Il s’empara des villes fortifiées de Juda et s’avança jusqu’à Jérusalem.

5Alors le prophète Shemaya alla trouver Roboam et les chefs de Juda qui s’étaient retirés à Jérusalem à l’approche de Shishaq. Il leur dit : Voici ce que déclare l’Eternel : « Vous m’avez abandonné. A mon tour, je vous abandonne entre les mains de Shishaq. »

6Les chefs d’Israël et le roi s’humilièrent et déclarèrent : L’Eternel est juste !

7Quand l’Eternel vit qu’ils s’humiliaient, il adressa une nouvelle parole à Shemaya : Puisqu’ils se sont humiliés, dit-il, je ne les détruirai pas ; d’ici peu de temps, je leur accorderai la délivrance et je ne déchaînerai pas ma colère sur Jérusalem par le moyen de Shishaq. 8Toutefois, ils lui seront assujettis et ils pourront apprécier la différence entre me servir et servir des rois d’autres pays.

9Shishaq, roi d’Egypte, vint attaquer Jérusalem. Il s’empara des trésors du temple de l’Eternel et de ceux du palais royal. Il prit absolument tout, notamment les boucliers d’or que Salomon avait fait faire12.9 Voir 2 Ch 9.15-16.. 10Le roi Roboam fit faire des boucliers de bronze pour les remplacer et les confia aux chefs des gardes chargés de surveiller l’entrée du palais royal. 11Chaque fois que le roi se rendait au temple de l’Eternel, les gardes venaient les enlever, puis ils les replaçaient dans la salle du corps de garde.

12Lorsque Roboam s’humilia, la colère de l’Eternel se détourna de lui et sa ruine ne fut pas totale. D’ailleurs, il y avait encore de bonnes choses en Juda. 13Le roi Roboam affermit son pouvoir à Jérusalem et continua à régner. Il avait quarante et un ans à son avènement, et il régna dix-sept ans à Jérusalem12.13 De 930 à 913 av. J.-C., la ville que l’Eternel avait choisie parmi toutes les tribus d’Israël pour y établir sa présence. Sa mère était une Ammonite nommée Naama. 14Il fit ce qui est mal, parce qu’il n’appliqua pas son cœur à s’attacher à l’Eternel.

15Les faits et gestes de Roboam, des premiers aux derniers, sont cités dans les Actes du prophète Shemaya et du prophète Iddo où sont enregistrées des listes généalogiques. Roboam et Jéroboam furent tout le temps en guerre l’un avec l’autre. 16Quand Roboam rejoignit ses ancêtres décédés, il fut enterré dans la Cité de David. Son fils Abiya lui succéda sur le trône.