2 Mbiri 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 1:1-17

Solomoni Apempha Nzeru

1Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.

2Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja. 3Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja. 4Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu. 5Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko. 6Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.

7Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”

8Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake. 9Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi. 10Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”

11Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo, 12Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”

13Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.

14Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu. 15Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa. 16Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe. 17Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.

Bibelen på hverdagsdansk

2. Krønikebog 1:1-18

Salomon beder Gud om visdom

1.Kong. 3,4-15

1Salomon, kong Davids søn, styrkede sit greb om magten i Israel, for Herren, hans Gud, hjalp ham og gjorde ham til en mægtig konge. 2Han sammenkaldte alle officererne i hæren, dommerne, stammelederne og slægtsoverhovederne, 3og gik i spidsen for dem til offerhøjen i Gibeon, for dér stod åbenbaringsteltet, som Herrens tjener Moses havde ladet fremstille i ørkenen. 4Pagtens ark stod dog i Jerusalem i det telt, som kong David havde rejst, dengang han hentede arken fra Kirjat-Jearim. 5Men det bronzealter, som Betzalel, søn af Uri, som var søn af Hur, havde lavet, stod stadig foran det gamle åbenbaringstelt. Derfor tog Salomon og Israels ledere derhen for at søge Herren og bringe ofre til ham. 6Salomon ofrede tusind brændofre på alteret.

7Samme nat viste Gud sig for Salomon i en drøm og sagde: „Bed om, hvad du vil, og jeg vil give det til dig!”

8Salomon svarede: „Du har været umådelig god imod min far, David, og nu har du gjort mig til hans efterfølger. 9Jeg beder om din hjælp, så dit løfte til min far kan gå i opfyldelse, for du har gjort mig til konge over et folk så talrigt som jordens støv. 10Giv mig da den visdom og indsigt, der skal til for at regere dem på den rette måde, for hvem kan i egen kraft regere over dit mægtige folk?”

11Gud svarede: „Fordi dit største ønske er at hjælpe dit folk, og fordi du ikke bad om personlig rigdom og ære eller død over dine fjender eller et langt liv, men du bad om visdom og indsigt til at regere mit folk, som jeg gjorde dig til konge over, 12så vil jeg give dig den visdom og indsigt du bad om. Men jeg giver dig mere end det! Jeg giver dig også større rigdom og ære, end nogen konge har haft før dig, eller nogen konge siden skal få.”

13Den næste dag vendte Salomon tilbage til Jerusalem, og han regerede med visdom over Israel i mange år.

Salomons rigdom

1.Kong. 10,14-29

14Salomon anskaffede sig masser af stridsvogne og heste. Han havde 1400 stridsvogne og 12.000 heste, som han stationerede i de dertil indrettede vognbyer og i selve Jerusalem. 15Salomons rigdom betød, at guld og sølv blev lige så almindeligt et syn i Jerusalem som stenene i byens gader, og det kostbare cedertræ blev lige så almindeligt som morbærfigentræ fra de vestlige bakkeskråninger. 16Salomons heste blev importeret fra Egypten og Kilikien, hvor hans opkøbere konstant var på udkig. 17En egyptisk stridsvogn leveret i Jerusalem kostede syv kilo sølv, og en hest kostede godt halvandet kilo sølv. En del af disse heste og vogne blev solgt videre til de hittitiske og aramæiske konger.

Tempelbyggeriet forberedes

1.Kong. 5,1-16

18Salomon gav nu ordre til at igangsætte byggeriet af Herrens hus og sit eget palads.