2 Atesalonika 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Atesalonika 1:1-12

1Paulo, Silivano ndi Timoteyo.

Kulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

2Chisomo ndi mtendere kwa inu kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu.

Kuyamika ndi Pemphero

3Ife tiyenera kuyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu abale. Ndipo tiyenera kutero chifukwa chikhulupiriro chanu chikukulirakulirabe, ndiponso chikondi chimene aliyense wa inu ali nacho pa mnzake chikuchulukirachulukirabe. 4Nʼchifukwa chake, timayankhula monyadira mʼmipingo yonse ya Mulungu za kupirira kwanu ndi chikhulupiriro chanu pakati pa masautso onse ndi mayesero amene mukudutsamo.

5Zonsezi zikutsimikiza kuti Mulungu amaweruza molungama. Zotsatira zake ndi zakuti mudzatengedwa kukhala oyenera kulowa mu ufumu wa Mulungu umene mukuwuvutikira. 6Mulungu ndi wolungama ndipo adzalanga amene amakusautsaniwo 7ndikukupatsani mpumulo amene mukusautsidwa, pamodzi ndi ifenso. Izi zidzachitika Ambuye Yesu akadzaoneka mʼmalawi amoto kuchokera kumwamba pamodzi ndi angelo ake amphamvu. 8Iye adzalanga amene sadziwa Mulungu ndi amene samvera Uthenga Wabwino wa Ambuye athu Yesu. 9Adzalangidwa ndi chiwonongeko chamuyaya ndipo sadzaonanso nkhope ya Ambuye ndi ulemerero wamphamvu zake 10pa tsiku limene iye adzabwera kudzalemekezedwa mwa oyera mtima ndi kuyamikidwa ndi onse amene anakhulupirira. Inu mudzakhala nawo mʼgulumo chifukwa munakhulupirira umboni wathu.

11Nʼchifukwa chake timakupemphererani nthawi zonse, kuti Mulungu wathu akusandutseni oyenera mayitanidwe ake, ndi kuti mwa mphamvu zake akwaniritse cholinga chanu chilichonse chabwino ndi chilichonse chochitika mwachikhulupiriro. 12Ife timapempherera zimenezi kuti dzina la Ambuye athu Yesu lilemekezedwe mwa inu, ndi inu mulemekezedwe mwa Iyeyo. Zonsezi zidzachitika chifukwa cha chisomo cha Mulungu wathu ndi Ambuye Yesu Khristu.

New Russian Translation

2 Фессалоникийцам 1:1-12

1От Павла, Силуана1:1 Силуан – по всей вероятности, Силуан и Сила (см. Деян. 15:22) – одно и то же лицо. и Тимофея – церкви фессалоникийцев в Боге, нашем Отце, и Господе Иисусе Христе.

2Благодать и мир вам от Бога Отца и от Господа Иисуса Христа!

В ожидании дня возвращения Господа

3Мы всегда должны благодарить Бога за вас, братья, и это правильно, потому что ваша вера растет все больше и больше, увеличивается и любовь каждого из вас друг к другу. 4Мы с гордостью говорим в Божьих церквах о вашей стойкости и о вере, которую вы проявили во всех преследованиях и несчастьях, переносимых вами.

5Все это – свидетельство тому, что Бог судит справедливо и что в конце концов вы будете признаны достойными Божьего Царства, за которое вы и страдаете. 6Бог справедлив, и Он отплатит несчастьями тем, кто причиняет несчастья вам, 7а нам с вами, перенесшим такие несчастья, Он даст покой. Это произойдет тогда, когда Господь Иисус придет с небес с могущественными ангелами 8в пламени огня, чтобы наказать всех тех, кто не познал Бога1:8 См. Пс. 78:6; Ис. 66:15; Иер. 10:25. и остался непослушным Радостной Вести нашего Господа Иисуса Христа. 9Они будут наказаны вечной гибелью: будут навсегда отделены от Господа и от славы Его могущества. 10Это произойдет в тот День, когда Он придет, чтобы быть прославленным среди Своего святого народа и вызвать восхищение у всех верующих. И вы тоже будете среди них, потому что вы поверили нашему свидетельству.

11Поэтому мы постоянно молимся о вас, чтобы Бог наш счел вас достойными вашего призвания, и просим, чтобы Своей силой Он исполнил каждое ваше доброе начинание и дело веры. 12Мы молимся о том, чтобы по благодати нашего Бога и Господа Иисуса Христа было прославлено благодаря вам имя нашего Господа Иисуса, и чтобы вы были прославлены вместе с Ним.