1 Timoteyo 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 1:1-20

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa lamulo la Mulungu, Mpulumutsi wathu ndiponso Khristu Yesu chiyembekezo chathu.

2Kwa Timoteyo mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro.

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Ambuye athu zikhale ndi iwe.

Kutsutsa Aphunzitsi Onyenga

3Monga ndinakupempha pamene ndinkapita ku Makedoniya, khala ku Efeso komweko kuti uletse anthu ena kuphunzitsa ziphunzitso zonyenga, 4kapena kumangoyika mitima pa nthano zopeka ndi kufufuza za mayina a makolo awo. Zinthu zotere zimapititsa mʼtsogolo mikangano mʼmalo mwa ntchito ya Mulungu yomwe ndi ya chikhulupiriro. 5Cholinga cha lamuloli ndi chikondi, chomwe chimachokera mu mtima woyera, chikumbumtima chabwino ndi chikhulupiriro choona. 6Anthu ena anapatuka pa zimenezi ndipo anatsata nkhani zopanda tanthauzo. 7Iwo amafuna kukhala aphunzitsi amalamulo, koma sadziwa zimene akunena, kapena zimene akufuna kutsimikiza.

8Tikudziwa kuti Malamulo ndi abwino ngati munthu awagwiritsa ntchito bwino. 9Tikudziwanso kuti Malamulo sakhazikitsidwa chifukwa cha anthu olungama, koma ophwanya lamulo ndi owukira, osaopa Mulungu ndi ochimwa, wopanda chiyero ndi osapembedza; amene amapha abambo awo ndi amayi awo, kapena anthu ena. 10Malamulo amayikidwa chifukwa cha anthu achigololo ndi ochita zadama ndi amuna anzawo, anthu ogulitsa akapolo, abodza ndi olumbira zabodza, ndi ochita chilichonse chotsutsana ndi chiphunzitso choona. 11Chiphunzitso chimene chimagwirizana ndi Uthenga Wabwino wonena za ulemerero wa Mulungu wodala, umene Iye mwini anandisungitsa.

Chisomo cha Ambuye kwa Paulo

12Ndikuthokoza Khristu Yesu Ambuye athu, amene anandipatsa mphamvu pa ntchitoyi. Iye ananditenga kukhala wokhulupirira, nandipatsa ntchito mu utumiki wake. 13Ngakhale kuti kale ndinali wachipongwe, wozunza ndi wankhanza, anandichitira chifundo chifukwa ndinkachita mwaumbuli ndi mopanda chikhulupiriro. 14Chisomo cha Ambuye athu chinatsanulidwa pa ine mochuluka, pamodzi ndi chikhulupiriro ndi chikondi zimene zili mwa Khristu Yesu.

15Mawu odalirika ndi woyenera kuwavomereza kwathunthu ndi awa: Yesu Khristu anabwera pa dziko lapansi kudzapulumutsa ochimwa, ndipo mwa iwowo ine ndiye wochimwitsitsa. 16Ndipo pa chifukwa chimenechi, Mulungu anandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwitsitsa, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse kuti ndikhale chitsanzo cha omwe angathe kumukhulupirira ndi kulandira moyo wosatha. 17Tsopano kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Ameni.

Ntchito ya Timoteyo

18Mwana wanga Timoteyo, ndikukupatsa langizo ili molingana ndi maulosi amene aneneri ananena za iwe. Pamene ukumbukira mawu amenewa udzatha kumenya bwino nkhondo 19utagwiritsitsa chikhulupiriro ndi chikumbumtima chabwino. Ena anazikana zimenezi motero chikhulupiriro chawo chinawonongeka. 20Ena mwa amenewa ndi Humenayo ndi Alekisandro, amene ndinawapereka kwa Satana kuti aphunzire kusachita chipongwe Mulungu.

New Russian Translation

1 Тимофею 1:1-20

1От Павла, апостола Христа Иисуса, по велению Бога, нашего Спасителя, и Иисуса Христа – нашей надежды.

2Моему истинному сыну в вере Тимофею.

Благодать, милость, мир тебе от Бога Отца и Господа нашего Христа Иисуса.

Предупреждение о ложных учениях

3Отправляясь в Македонию, я настоятельно попросил тебя остаться в Эфесе и потребовать от некоторых людей не учить чему-то другому, 4не расточать свое время на всевозможные россказни и бесконечные родословные. Это лишь порождает споры, а не способствует успеху дела Божьего, которое строится на вере. 5Цель этого требования – любовь, которая исходит из чистого сердца, доброй совести и искренней веры. 6Но некоторые люди, оставив все это, стали заниматься бессмысленными разговорами. 7Они хотят быть учителями Закона, но сами не разбираются ни в том, о чем говорят, ни в том, что так решительно утверждают.

8Мы знаем, что Закон хорош, если им правильно пользоваться. 9Мы знаем также, что Закон существует не для праведного, а для нарушителей Закона и для непокорных, для нечестивых и грешных, для тех, кто не признает ничего святого, и для безбожников, для тех, кто бьет своего отца или мать, для убийц, 10для развратников, гомосексуалистов, работорговцев, лжецов, клятвопреступников и всех, кто занимается тем, что противоречит здравому учению 11и не соответствует доверенной мне славной Радостной Вести от Бога, достойного всякой хвалы.

Благодарность за милость Божью

12Я благодарю Господа нашего Иисуса Христа, давшего мне силы, за то, что Он счел меня верным и поручил мне служение, 13несмотря на то что я прежде был кощунником, гонителем и наглецом. Но ко мне была проявлена милость, потому что я действовал по незнанию и неверию. 14Благодать же нашего Господа была проявлена во мне во всем ее богатстве вместе с верой и любовью, которая в Иисусе Христе.

15Правильно и достоверно изречение: Иисус Христос пришел в этот мир, чтобы спасти грешников, самый худший из которых – я. 16Но для того ко мне и была проявлена такая милость, чтобы на мне, худшем из грешников, Иисус Христос показал, как велико Его терпение, и чтобы другие, видя это, тоже поверили и получили вечную жизнь. 17Так пусть же вечному Царю, бессмертному, невидимому и единому Богу, будет честь и слава вовеки! Аминь.

Наставления Павла о сохранении веры

18Тимофей, сын мой, я пишу тебе это наставление, помня о пророчествах, которые были сказаны о тебе. Я хочу, чтобы ты, следуя им, вел битву за истину, 19сохраняя свою веру и чистую совесть. Некоторые ее отвергли, и в результате их вера потерпела кораблекрушение. 20Среди них Гименей и Александр, которых я предал во власть сатаны1:20 Предал во власть сатаны – исходя из того, что греховный мир находится под властью сатаны, то, вероятнее всего, здесь речь идет об отлучении от церкви, которая принадлежит Богу (см. 1 Кор. 5). По другому толкованию у посланников Христа была особая власть предавать согрешающих власти сатаны, тем самым навлекая на него физические страдания, а в некоторых случаях даже физическую смерть (см. Деян. 5:1-11)., чтобы они научились не кощунствовать.