2 Akorinto 12 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 12:1-21

Masomphenya a Paulo ndi Minga ya Mʼthupi Mwake

1Ndiyenera kupitiriza kudzitamandira. Ngakhale palibe choti ndipindule, ndipitiriza kufotokoza za masomphenya ndi mavumbulutso ochokera kwa Ambuye. 2Ndikudziwa munthu mwa Khristu amene zaka khumi ndi zinayi zapitazo anatengedwa kupita kumwamba kwachitatu. Sindikudziwa ngati zinachitika ali mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu. 3Ndipo ndikumudziwa munthu ameneyu. Sindikudziwa ngati zinachitika mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu. 4Munthuyu anatengedwa kupita ku paradizo. Ndipo anamva zinthu zosatheka kuneneka, zinthu zimene munthu saloledwa kunena. 5Ndidzatamanda za munthu ngati ameneyu, koma sindidzadzitamandira ine mwini kupatula za kufowoka kwanga. 6Ngakhale nditafuna kudzitamandira, sindingakhale chitsiru, chifukwa ndikunena zoona. Koma ndimapewa kuti pasapezeke munthu wondiganizira moposera chimene ndili chifukwa cha zimene ndimachita kapena kuyankhula, 7kapena chifukwa cha mavumbulutso aakulu kuposa awa. Choncho, kuti ndisadzitukumule, ndinayikidwa minga mʼthupi langa, wamthenga wa Satana, kuti adzindizunza. 8Katatu konse ndinapempha Ambuye kuti andichotsere. 9Koma anandiwuza kuti, “Chisomo changa ndi chokukwanira, pakuti mphamvu zanga zimaoneka kwathunthu mwa munthu wofowoka.” Choncho ndidzadzitamandira mokondwera chifukwa cha zofowoka zanga, kuti mʼkutero mphamvu ya Khristu ikhale pa ine. 10Tsono, chifukwa cha Khristu, ndimakondwera pamene ndili wofowoka, pamene akundinyoza, pamene ndikumva zowawa, ndi pamene akundizunza ndi kundisautsa. Pakuti pamene ndili wofowoka ndiye kuti ndili wamphamvu.

Paulo Akhudzidwa ndi Akorinto

11Ndadzisandutsa wopusa, koma inu mwandichititsa zimenezi. Ndinu amene munayenera kundichitira umboni. Ngakhale kuti sindine kanthu, koma sindine wochepetsetsa kwa “atumwi apamwamba” aja. 12Ndinapirira pokuonetserani zizindikiro za mtumwi weniweni, pochita pakati panu zizindikiro, zodabwitsa ndi ntchito zamphamvu. 13Kodi inu munaoneka ochepa motani ku mipingo ina, kupatula kuti sindinali cholemetsa kwa inu? Mundikhululukire cholakwa chimenechi!

14Ndakonzeka tsopano kudzakuyenderani kachitatu, ndipo sindidzakhala cholemetsa kwa inu chifukwa ndikungofuna inuyo osati zinthu zanu. Pakuti ana sasamalira makolo koma makolo ndiwo asamalira ana. 15Motero ndidzakondwera kukupatsani zanga zonse zimene ndili nazo ndi kudziperekanso ine mwini chifukwa cha inu. Kodi ine ndikamakukondani kwambiri chotere, inuyo mudzandikonda pangʼono? 16Ena mwa inu amavomereza kuti sindinali cholemetsa. Komabe ena amaganiza kuti ndine wochenjera, ndipo ndinakuchenjererani. 17Kodi ndinakudyerani masuku pamutu kudzera mwa wina aliyense amene ndinamutumiza kwa inu? 18Ndinamupempha Tito kuti abwere kwanuko ndipo ndinamutumiza pamodzi ndi mʼbale wathu. Kodi kapena Tito anakudyerani masuku pamutu? Kodi iye ndi ine sitinachite zinthu mofanana ndi Mzimu mmodzi yemweyo?

19Kodi mukuyesa kuti nthawi yonseyi takhala tikudzitchinjiriza tokha? Takhala tikuyankhula pamaso pa Mulungu monga anthu amene ali mwa Khristu; ndipo abwenzi okondedwa, chilichonse chimene timachita ndi chofuna kukulimbikitsani. 20Pakuti ndikuona kuti pamene ndibwera sindidzakupezani monga mmene ndikufunira kuti muzikhalira, ndipo simungadzandione monga mmene mukufunira kundionera. Ndikuopa kuti pangadzakhale mkangano, nsanje, kupserana mitima, kugawikana, ugogodi, miseche, kudzitukumula ndi chisokonezo. 21Ndikuopa kuti pamene ndidzabwerenso, Mulungu adzandichepetsa pamaso panu, ndipo ndidzamva chisoni ndi ambiri amene anachimwa kale ndipo sanalape zonyansa, zachigololo ndi zilakolako zoyipa zimene anachita.

Knijga O Kristu

2 Korinćanima 12:1-21

Pavlovo viđenje i trn u tijelu

1Nije uputno tako se hvastati, ali reći ću vam i o viđenjima i otkrivenjima Gospodnjim. 2Poznajem čovjeka u Kristu koji je prije četrnaest godina bio uznesen do trećega neba. Ne znam je li u tijelu ili bez njega; Bog zna. 3Za toga čovjeka znam da je—u tijelu ili izvan tijela, to samo Bog zna— 4uznesen u raj i da je čuo neizrecive riječi koje čovjeku nije dopušteno govoriti. 5Iskustvom tog čovjeka mogao bih se hvaliti, ali se sobom neću hvaliti osim svojim slabostima. 6Kad bih se i htio hvaliti, ne bih bio bezuman, već bih govorio istinu. Ali neću to činiti da tko ne bi o meni mislio više od onoga što na meni vidi ili što od mene čuje. 7Da se ne bih umislio zbog izobilja Božjih otkrivenja, dan mi je trn u tijelo, Sotonina poslanika, da me muči da se ne uzoholim. 8Već sam triput molio Gospodina da me toga oslobodi. 9Svaki put mi je odgovorio: “Dosta ti je moja milost, jer se moja snaga najbolje očituje u slabosti.” Radostan sam što se mogu hvaliti svojom slabošću, da kroz mene može djelovati Kristova snaga. 10Uživam u slabostima, uvredama, nevoljama, progonstvima i teškoćama jer znam da to sve podnosim za Krista; jer kad sam slab—jak sam.

Pavlova briga za Korinćane

11Natjerali ste me, eto, da se ponesem poput bezumnika! Vi biste, zapravo, meni trebali pisati preporuke jer nisam nimalo gori od tih “nadapostola”, iako nisam ništa. 12A da sam od Boga poslan apostol, dokazao sam vam, dok bijah s vama, s mnogo strpljenja, brojnim znakovima i čudesnim djelima. 13Pa u čemu sam to onda lošije postupio prema vama nego prema ostalim crkvama, osim što vam nisam bio na teret? Oprostite mi za tu “nepravdu”!

14Spreman sam vam doći i treći put i neću vam biti na teret jer ne želim vaš novac. Vas želim! I tako ste moja djeca, a nisu djeca dužna prehranjivati roditelje, već roditelji djecu. 15Rado ću potrošiti sve što imam, pa i samoga sebe, za vašu duhovnu hranu, iako mi se čini da što ja vas više volim, vi mene volite manje. 16Nisam vam bio na teret, ali sam vas, “lukav” kakav već jesam, “uhvatio na prijevaru”? 17Ali kako? Zar sam vas iskoristio po nekom svojem suradniku kojega sam vam poslao? 18Kad sam zamolio Tita da vas posjeti i s njime poslao drugog brata, zar su se oni okoristili vama i u nečemu vas zakinuli? Jer mi smo istoga Duha, te hodimo istim stopama radeći isto.

19Možda smatrate da vam sve to govorimo zato da bismo se pred vama opravdali. Nije tako! Govorimo vam pred Bogom i u Kristu: sve je to zbog vaše duhovne izgradnje. 20Bojim se da vas, kada dođem, ne zateknem kakve bih želio, a vama se onda neće svidjeti moj postupak. Bojim se da ću vas zateći u svađi, srdžbi, suparništvu, klevetama, ogovaranju, oholosti i neredu. 21Bojim se da će me Bog, kad dođem, poniziti pred vama i da ću biti žalostan, da ću oplakivati mnoge koji su zgriješili, a nisu se pokajali za nečistoću, razvrat i blud koji su počinili.