1 Timoteyo 2 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 2:1-15

Malangizo Achipembedzo

1Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika. 2Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima. 3Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu, 4amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi. 5Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu. 6Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera. 7Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.

8Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.

9Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali. 10Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.

11Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu. 12Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete. 13Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava. 14Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa. 15Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.

New International Reader’s Version

1 Timothy 2:1-15

Teachings About Worship

1First, I want you to pray for all people. Ask God to help and bless them. Give thanks for them. 2Pray for kings. Pray for everyone who is in authority. Pray that we can live peaceful and quiet lives. And pray that we will be godly and holy. 3This is good, and it pleases God our Savior. 4He wants all people to be saved. He wants them to come to know the truth. 5There is only one God. And there is only one go-between for God and human beings. He is the man Christ Jesus. 6He gave himself to pay for the sins of all people. We have been told this message at just the right time. 7I was appointed to be a messenger and an apostle to preach the good news. I am telling the truth. I’m not lying. God appointed me to be a true and faithful teacher of the Gentiles.

8So I want the men in every place to pray. I want them to lift up holy hands. I don’t want them to be angry when they pray. I don’t want them to argue. 9In the same way, I want the women to be careful how they dress. They should wear clothes that are right and proper. They shouldn’t wear their hair in very fancy styles. They shouldn’t wear gold or pearls. They shouldn’t wear clothes that cost a lot of money. 10Instead, they should put on good works as if good works were their clothes. This is proper for women who claim to worship God.

11When a woman is learning, she should be quiet. She should follow her leaders in every way. 12I do not let women teach or take authority over a man. They must be quiet. 13That’s because Adam was made first. Then Eve was made. 14Adam was not the one who was tricked. The woman was tricked and became a sinner. 15Will women be saved by having children? Only if they keep on believing, loving, and leading a holy life in a proper way.