1 Timoteyo 2 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 2:1-15

Malangizo Achipembedzo

1Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika. 2Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima. 3Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu, 4amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi. 5Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu. 6Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera. 7Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.

8Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.

9Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali. 10Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.

11Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu. 12Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete. 13Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava. 14Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa. 15Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

提摩太前书 2:1-15

要为他人祷告

1我劝你首先要为所有的人恳求、祷告、代求,为他们感谢上帝。 2也要为所有的君王和掌权者祷告,使我们可以怀着虔诚、端正的心过和平安宁的生活。 3这样做很美好,是蒙我们的救主上帝悦纳的。 4因为祂愿全人类都得救,明白真理。 5上帝只有一位,在上帝和人类之间只有一位中保,就是降世为人的基督耶稣。 6祂舍命作全人类的赎价,这在所定的时候已显明出来。 7为此,我被指派做传道人和使徒,教导外族人认识信仰和真理。我说的是实话,并非谎言。

信徒的操守

8我愿男人举起圣洁的手随处祷告,不发怒,不争辩2:8 争辩”或译“疑惑”。9我愿女人衣着朴素端庄,不靠发型、珠宝金饰或名贵衣服来妆饰自己, 10要有良好的行为,这样才配称为敬畏上帝的妇女。 11妇女应当安安静静地学习,完全顺服。

12我不准女人教导或管辖男人,她们应当保持安静。 13因为先造的是亚当,后造的是夏娃14受骗犯罪的不是亚当,是夏娃15不过,女人如果持守信心和爱心,圣洁自律,就必在生育的事上得救。