2 Timoteyo 1 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 1:1-18

1Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.

2Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa:

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Chilimbikitso Pokhala Wokhulupirika

3Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga. 4Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe. 5Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.

Kumvera Paulo ndi Uthenga Wabwino

6Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja. 7Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.

8Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu. 9Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. 10Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe. 11Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu. 12Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.

13Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu. 14Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.

Zitsanzo za Kusakhulupirika ndi Kukhulupirika

15Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.

16Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo. 17Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza. 18Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

提摩太后书 1:1-18

1保罗奉上帝的旨意,按照在基督耶稣里所应许的生命做基督耶稣的使徒, 2写信给我亲爱的儿子提摩太

愿父上帝和我们的主基督耶稣的恩典、怜悯和平安临到你!

勉励忠心事奉

3我日夜不停地为你祷告,对我效法祖先用清洁的良心事奉的上帝充满了感恩。 4每逢想起你流泪的情形,我就渴望见你,好使我的心充满喜乐。 5我记得你那真诚无伪的信心。你外祖母罗以和你母亲友妮基首先有了这信心,我深信你也有。 6因此我提醒你,要把上帝在我把手按在你身上时赐给你的恩赐充分发挥出来。 7因为上帝赐给我们的不是懦弱的心,而是刚强、仁爱、自律的心。

8所以,你不要羞于为我们的主做见证,也不要以我这为主被囚的人为耻,要靠着上帝的能力和我一同为福音受苦。 9上帝拯救了我们,并呼召我们过圣洁的生活,不是因为我们的行为,而是出于祂的旨意和恩典。早在万古以前,祂就在基督耶稣里把这恩典赐给我们了, 10如今借着我们救主基督耶稣的降世显明了出来。基督已经消灭了死亡,借着福音将不朽的生命彰显了出来。

11我为了这福音受委派做传道人、使徒和教师。 12我因此而遭受这些苦难,但我不以为耻,因为我知道我所信的是谁,也深信祂能保守祂所托付我的1:12 祂所托付我的”又可翻译为“我所信托祂的”。,一直到那日1:12 那日”指保罗站在基督面前交账的日子。13你要以在基督耶稣里的信心和爱心,把从我这里听到的正确教导当作典范遵守, 14要靠着住在我们里面的圣灵牢牢守住交托给你的美善之道。

15你知道几乎所有亚细亚的人都离弃了我,其中包括腓吉路黑摩其尼16愿主怜悯阿尼色弗一家人,他常常鼓励我,不以我被囚禁为耻。 17他在罗马的时候千方百计寻访我的下落,直到找着我为止。 18你很清楚,他从前在以弗所怎样在各个方面服侍我。愿主再来时格外地怜悯他。