1 Timoteyo 1 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 1:1-20

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa lamulo la Mulungu, Mpulumutsi wathu ndiponso Khristu Yesu chiyembekezo chathu.

2Kwa Timoteyo mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro.

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Ambuye athu zikhale ndi iwe.

Kutsutsa Aphunzitsi Onyenga

3Monga ndinakupempha pamene ndinkapita ku Makedoniya, khala ku Efeso komweko kuti uletse anthu ena kuphunzitsa ziphunzitso zonyenga, 4kapena kumangoyika mitima pa nthano zopeka ndi kufufuza za mayina a makolo awo. Zinthu zotere zimapititsa mʼtsogolo mikangano mʼmalo mwa ntchito ya Mulungu yomwe ndi ya chikhulupiriro. 5Cholinga cha lamuloli ndi chikondi, chomwe chimachokera mu mtima woyera, chikumbumtima chabwino ndi chikhulupiriro choona. 6Anthu ena anapatuka pa zimenezi ndipo anatsata nkhani zopanda tanthauzo. 7Iwo amafuna kukhala aphunzitsi amalamulo, koma sadziwa zimene akunena, kapena zimene akufuna kutsimikiza.

8Tikudziwa kuti Malamulo ndi abwino ngati munthu awagwiritsa ntchito bwino. 9Tikudziwanso kuti Malamulo sakhazikitsidwa chifukwa cha anthu olungama, koma ophwanya lamulo ndi owukira, osaopa Mulungu ndi ochimwa, wopanda chiyero ndi osapembedza; amene amapha abambo awo ndi amayi awo, kapena anthu ena. 10Malamulo amayikidwa chifukwa cha anthu achigololo ndi ochita zadama ndi amuna anzawo, anthu ogulitsa akapolo, abodza ndi olumbira zabodza, ndi ochita chilichonse chotsutsana ndi chiphunzitso choona. 11Chiphunzitso chimene chimagwirizana ndi Uthenga Wabwino wonena za ulemerero wa Mulungu wodala, umene Iye mwini anandisungitsa.

Chisomo cha Ambuye kwa Paulo

12Ndikuthokoza Khristu Yesu Ambuye athu, amene anandipatsa mphamvu pa ntchitoyi. Iye ananditenga kukhala wokhulupirira, nandipatsa ntchito mu utumiki wake. 13Ngakhale kuti kale ndinali wachipongwe, wozunza ndi wankhanza, anandichitira chifundo chifukwa ndinkachita mwaumbuli ndi mopanda chikhulupiriro. 14Chisomo cha Ambuye athu chinatsanulidwa pa ine mochuluka, pamodzi ndi chikhulupiriro ndi chikondi zimene zili mwa Khristu Yesu.

15Mawu odalirika ndi woyenera kuwavomereza kwathunthu ndi awa: Yesu Khristu anabwera pa dziko lapansi kudzapulumutsa ochimwa, ndipo mwa iwowo ine ndiye wochimwitsitsa. 16Ndipo pa chifukwa chimenechi, Mulungu anandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwitsitsa, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse kuti ndikhale chitsanzo cha omwe angathe kumukhulupirira ndi kulandira moyo wosatha. 17Tsopano kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Ameni.

Ntchito ya Timoteyo

18Mwana wanga Timoteyo, ndikukupatsa langizo ili molingana ndi maulosi amene aneneri ananena za iwe. Pamene ukumbukira mawu amenewa udzatha kumenya bwino nkhondo 19utagwiritsitsa chikhulupiriro ndi chikumbumtima chabwino. Ena anazikana zimenezi motero chikhulupiriro chawo chinawonongeka. 20Ena mwa amenewa ndi Humenayo ndi Alekisandro, amene ndinawapereka kwa Satana kuti aphunzire kusachita chipongwe Mulungu.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרת פולוס הראשונה אל-טימותיוס 1:1-20

1מאת פולוס, שליחו של ישוע המשיח לפי מצוותו הישירה של האלוהים מושיענו וישוע המשיח, שהוא תקוותנו היחידה.

2אל טימותיוס, בני האמיתי באמונה.

מי ייתן שהאלוהים אבינו וישוע המשיח אדוננו יברך אותך בחסד, ברחמים ובשלום.

3אני חוזר ומבקש ממך את מה שביקשתי לפני צאתי למקדוניה: אנא, הישאר כאן באפסוס, וצווה על אנשים מסוימים להפסיק ללמד את תורות השקר שלהם, ולהפסיק לרמות את האנשים. 4שים קץ לאגדות, לשקרים ולאמונה במגילות־יוחסין אינסופיות, הגורמים לוויכוחים ולספקות, ומונעים את בניית בית האלוהים באמונה. 5אני משתוקק שכל המאמינים המשיחיים ימלאו באהבה שנובעת מלב טהור, מצפון נקי ואמונה אמיתית. 6אבל ישנם אנשים שתעו מהדברים האלה ופנו לדיבורי הבל. 7הם רוצים שיכירו בהם כבעלי סמכות בהוראת התורה, בזמן שאינם בקיאים בתורה ואינם יודעים כלל מה שהם אומרים.

8אנחנו יודעים שחוקי התורה הם טובים, בתנאי שמשתמשים בהם כפי שאלוהים רצה. 9אנחנו גם יודעים שחוקי התורה לא נחקקו למען האנשים הישרים והטובים, אלא למען אנשים חסרי מוסר, חסרי שליטה עצמית – למען הרשעים. כן, חוקי התורה נחקקו עבור אנשים שמכים את הוריהם, רוצחים את חבריהם, 10‏-11זונים, הומוסקסואלים, סוחרי נפש, רמאים, שקרנים, וכל אלה שעושים מעשים שהם נגד הבשורה הנפלאה של האל המבורך, אשר אני שליחו.

12אני אסיר תודה לישוע המשיח אדוננו על שבחר בי להיות אחד משליחיו, שבטח בי ומינה אותי לשרת אותו, 13למרות שבעבר לעגתי לשמו וקיללתי אותו. רדפתי את המאמינים במשיח, הצקתי להם ופגעתי בהם, אולם אלוהים ריחם עלי, כי בזמנו לא הכרתי את המשיח ולא ידעתי מה אני עושה. 14מה רב חסדו של אדוננו! – הוא לימדני לבטוח ולהאמין בו, ולהימלא באהבת המשיח.

15מה נהדר הדבר ומה משתוקק אני שכל העולם יידע: שישוע המשיח בא לעולם כדי להושיע את החוטאים, ואני הייתי הגדול שבהם! 16אך אלוהים ריחם עלי, כדי שישוע המשיח יוכל להציגני לדוגמה לפני כל העתידים להאמין בו, כהוכחה לסבלנותו הרבה אף כלפי החוטא הגדול ביותר! כך יבינו שגם הם יכולים לזכות בחיי נצח, 17כל הכבוד וההדר לאלוהים מעולם ועד עולם! הוא מלך העולמים, הבלתי־נראה אשר חי לנצח; הוא בלבד האלוהים והוא מלא חכמה. – אמן.

18טימותיוס, בני, אני מצווה עליך להילחם היטב במלחמת האדון, כפי שביקש ממך האדון באמצעות נביאיו. 19שמור היטב על אמונתך במשיח, שמור את מצפונך נקי תמיד, ועשה את הישר והנכון. כי יש אנשים שאטמו את אוזניהם לקול מצפונם ועשו את הרע בכוונה תחילה. לאחר שמאסו באלוהים בצורה כזאת, אין פלא שעד מהרה איבדו את אמונתם במשיח! 20הומניוס ואלכסנדרוס הם דוגמה לכך: נאלצתי להענישם ולמסרם לשטן, כדי שילמדו לא לבייש יותר את שם המשיח.