2 Atesalonika 3 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Atesalonika 3:1-18

Tipempherereni

1Potsiriza, abale, mutipempherere kuti uthenga wa Ambuye ufalikire msanga ndi kulemekezedwa monga momwe munachitira inu. 2Ndipo pempherani kuti tilanditsidwe mʼmanja mwa anthu ovuta ndi oyipa, pakuti si onse amene ali nacho chikhulupiriro. 3Koma Ambuye ndi wokhulupirika, ndipo adzakulimbikitsani ndi kukutetezani kwa woyipayo. 4Tili ndi chikhulupiriro mwa Ambuye kuti mukuchita zonse ndipo mudzapitirira kuchita zimene tinakulamulirani. 5Ambuye atsogolere mitima yanu kuti mudziwe chikondi cha Mulungu ndiponso kupirira kumene Khristu amapereka.

Awachenjeza za Kusagwira Ntchito

6Abale, tikukulamulani mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, kuti mupewe mʼbale aliyense amene ndi waulesi ndi wachisokonezo, wosafuna kutsata zimene tinakuphunzitsani. 7Pakuti inu mukudziwa zimene muyenera kuchita pofuna kutitsatira. Ife sitinali alesi pamene tinali nanu 8ndipo sitinadye chakudya cha aliyense osalipira. Komatu tinkagwira ntchito mwamphamvu usiku ndi usana kuti tisakhale cholemetsa kwa aliyense. 9Sitinachite zimenezi chifukwa choti tinalibe mphamvu zolamula kuti mutithandize koma kuti tikhale chitsanzo choti mutsatire. 10Pakuti ngakhale pamene tinali nanu, tinakupatsani lamulo lakuti, “Munthu wosafuna kugwira ntchito, asadye.”

11Ife tikumva kuti pakati panu pali ena amene ndi alesi. Iwo safuna kugwira ntchito, koma amangolowerera pa za eni. 12Mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, tikuwalamula ndi kuwakakamiza kuti azigwira ntchito mwabata ndi kumadya chakudya chodzigwirira ntchito okha. 13Koma inu abale, musatope nʼkuchita zabwino.

14Ngati wina aliyense akana kumvera malangizo athu a mʼkalatayi, mumuonetsetse ameneyo ndipo musayanjane naye kuti achite manyazi. 15Komatu musamutenge kukhala mdani, koma muchenjezeni ngati mʼbale.

Malonje Otsiriza

16Tsopano Ambuye mwini mtendere akupatseni mtendere nthawi zonse mwa njira iliyonse. Ambuye akhale ndi inu nonse.

17Ine Paulo, ndikulemba malonje awa ndi dzanja langa, chimene ndi chizindikiro chodziwika mʼmakalata anga onse. Umo ndi mmene ndimalembera.

18Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרת פולוס השנייה אל-התסלוניקים 3:1-18

1לסיום, אחים יקרים, אנא, התפללו בעדנו. ראשית כל התפללו שבשורת ה׳ תופץ במהירות וביעילות בכל מקום, ותביא לו כבוד רב כפי שהביאה ביניכם. 2שנית, התפללו שלא ניפול בידי אנשים רשעים, שהרי לא כולם אוהבים את האדון. 3אך אתם יכולים לסמוך על האדון שיחזק וישמור אתכם מכל רע. 4האדון גם העניק לנו את הביטחון שאתם מקיימים הלכה למעשה את מה שלימדנו אתכם, ואף שתמשיכו בכך בעתיד. 5והאדון ישוע יכשיר את לבבכם להבין את משמעותה ועומקה של אהבת אלוהים וסבלנותו של המשיח.

6אחים יקרים, אנו מצווים עליכם בשם ישוע המשיח אדוננו ובסמכותו: התרחקו מכל מאמין עקשן שמסרב לקיים את ההוראות שמסרנו לכם. 7אתם יודעים היטב שעליכם להתנהג כמונו, שכן מעולם לא ראיתם אותנו סוטים מהדרך הנכונה; 8מעולם לא אכלנו בחינם – תמיד שילמנו בעד מה שקיבלנו. עבדנו קשה יומם ולילה כדי להרוויח את מחייתנו, כי לא רצינו להכביד על איש מכם. 9אל תחשבו שלא הייתה לנו הזכות לבקש מכם לספק את מזוננו – פשוט רצינו להראות לכם כיצד עליכם לעבוד לפרנסתכם.

10עוד בהיותנו אצלכם ביקשנו מכם לשמור על העיקרון: ”מי שלא יעבוד לא יאכל!“

11אך בכל זאת אנו שומעים כי יש ביניכם טפילים עצלים, המסרבים לעבוד ומבזבזים את זמנם ברכילות וחרחורי־ריב. 12אנחנו מזהירים את האנשים האלה ומצווים עליהם בשם אדוננו ישוע המשיח: לכו לעבוד והרוויחו את לחמכם בכבוד! 13ולשאר האחים אני אומר: לעולם אל תתייאשו ואל תפסיקו לעשות מעשים טובים.

14גרשו מקרבכם את מי שמסרב לשמוע לדברינו שכתובים במכתב זה, כדי שיתבייש בעצמו. 15אל תתייחסו אליו כאל אויב, אלא כאל אח תועה שיש להזהירו ולהחזירו לדרך הישר. 16ואדון השלום בעצמו יעניק לכם את שלומו בכל עת ובכל מקום. יהיה האדון עם כולכם.

17‏-18עתה אני, פולוס, מברך את כולכם בכתב־ידי, כמנהגי בסיום כל מכתבי, לאות וסימן שאני באמת הכתבתי אותם. זהו כתב ידי וזוהי חתימתי. יברך אדוננו ישוע המשיח את כולכם.