1 Samueli 22 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 22:1-23

Davide Apita ku Adulamu ndi ku Mizipa

1Davide anachoka kumeneko nathawira ku phanga la Adulamu. Abale ake ndi banja lonse la abambo ake anamva izi, anapita kumene kunali Davide. 2Ndipo aliyense amene anali pa mavuto, kapena ndi ngongole kapenanso amene anali wosakondwa anasonkhana kwa iye, ndipo iye anakhala mtsogoleri wawo. Onse pamodzi analipo amuna 400.

3Kuchokera kumeneko Davide anapita ku Mizipa ku Mowabu ndipo anapempha mfumu ya Mowabu kuti, “Bwanji abambo ndi amayi anga akhale nanu mpaka ine nditadziwa chimene Mulungu adzachite nane?” 4Choncho iye anawasiya kwa mfumu ya Mowabu ndipo anakhala naye nthawi yonse imene Davide ankabisala ku phanga kuja.

5Koma mneneri Gadi anawuza Davide kuti, “Usakhale ku phanga kuno. Pita ku dziko la Yuda.” Kotero Davide anachoka ndi kupita ku nkhalango ya Hereti.

Sauli Apha Ansembe a ku Nobi

6Tsono Sauli anamva kuti Davide ndi anthu ake apezeka. Nthawiyo nʼkuti Sauli atakhala pansi pa mtengo wa bwemba pa phiri la ku Gibeya, mkondo uli mʼdzanja lake ndi ankhondo ake atayima chomuzungulira. 7Tsono Sauli anafunsa ankhondo ake aja kuti, “Tamverani inu anthu a fuko la Benjamini! Kodi mwana wa Yese adzakupatsani nonsenu minda ndi minda ya mpesa? Kodi nonsenu adzakuyikani kukhala atsogoleri a magulu ankhondo? 8Mwinatu nʼchifukwa chake mwagwirizana zondichita chiwembu. Palibe amene anandiwuza pamene mwana wanga ankapanga pangano ndi mwana wa Yese. Palibe aliyense amene ankalabadirako za ine kapena kundiwuza kuti mwana wanga wautsa mtima wa wantchito wanga kuti andiwukire monga wachitira lero.”

9Koma Doegi Mwedomu anayima pafupi ndi nduna za Sauli nati, “Ine ndinaona mwana wa Yese atabwera kwa Ahimeleki mwana wa Ahitubi ku Nobi. 10Ahimelekiyo anafunsa kwa Yehova chomwe Davide ayenera kuchita. Iye anamupatsa zakudya ndiponso lupanga la Goliati Mfilisiti uja.”

11Pamenepo mfumu inayitanitsa wansembe Ahimeleki mwana wa Ahitubi ndi banja lonse la abambo ake, amene anali ansembe ku Nobi. Ndipo onse anabwera kwa mfumu. 12Sauli anati, “Tsono tamvera, mwana wa Ahitubi.”

Iye anayankha kuti, “Inde mbuye wanga.”

13Sauli anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani iwe ndi mwana wa Yese mwandiwukira ine? Wamupatsa buledi ndi lupanga. Wafunsiranso kwa Yehova zoti andiwukire ndi kundibisalira monga wachita leromu?”

14Ahimeleki anayankha mfumu kuti, “Kodi ndani mwa ankhondo anu onse amene ali wokhulupirika monga Davide? Iye uja ndi mkamwini wa mfumu, kapitawo wa asilikali okutetezani ndiponso munthu amene amalemekezedwa mʼbanja lanu? 15Kodi tsiku limeneli linali loyamba kuti ndimufunsire kwa Yehova? Ayi sichoncho! Mfumu musandinenere kanthu kalikonse koyipa kapena banja la abambo anga, pakuti sindikudziwa kanthu kena kalikonse ka zimenezi.”

16Koma mfumu inati, “Iwe Ahimeleki ndi banja lonse la abambo ako mudzaphedwa ndithu.”

17Kenaka mfumu inalamulira alonda amene anali naye kuti, “Iphani ansembe a Yehovawa chifukwa iwo akugwirizana ndi Davide. Iwo amadziwa kuti Davide ankathawa koma sanandiwuze.”

Koma antchito a mfumu aja sanasamule dzanja kuti aphe ansembe a Yehova.

18Kotero mfumu inalamula Doegi kuti, “Uwaphe ndiwe ansembewa.” Choncho Doegi Mwedomu anapita ndi kuwapha. Tsiku limenelo iye anapha amuna 85 amene amavala efodi wa nsalu yofewa. 19Kunena za Nobi, mzinda wa ansembe, Sauli anapha amuna ndi amayi, ana ndi makanda pamodzi ndi ngʼombe, abulu ndi nkhosa.

20Koma Abiatara mwana wa Ahimeleki mwana wa Ahitubi anapulumuka ndi kuthawira kwa Davide. 21Abiatara anawuza Davide kuti Sauli wapha ansembe a Yehova. 22Ndipo Davide anati kwa Abiatara, “Tsiku lija pamene Doegi Mwedomu anali kumene kuja, ine ndimadziwa kuti salephera kukamuwuza Sauli. Ine ndi amene ndaphetsa banja lonse la abambo ako. 23Iwe khala ndi ine, usaope munthu amene akufuna moyo wako komanso wanga. Udzatetezeka ukakhala ndi ine.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

1 Царств 22:1-23

Довуд находит соратников

1Довуд покинул Гат и укрылся в пещере Адуллама. Когда его отец и весь его дом услышали об этом, они спустились к нему. 2Все несчастные, обиженные и все должники собрались вокруг него, и он стал их вождём. С ним было около четырёхсот человек.

3Оттуда Довуд пошёл в Мицпу, что в Моаве, и сказал царю Моава:

– Пожалуйста, позволь моим родителям прийти и побыть у вас, пока я не узнаю, что сделает для меня Всевышний.

4Он оставил их у царя Моава, и они оставались у него всё время, пока Довуд находился в том убежище. 5Но пророк Гад сказал Довуду:

– Не оставайся в убежище. Иди в Иудею.

И Довуд ушёл из Моава и пришёл в Херетский лес.

Шаул убивает священнослужителей Нова

6А Шаул услышал о том, что Довуд и его люди обнаружены. Шаул с копьём в руке сидел под тамариском на холме в Гиве, и его приближённые стояли вокруг него.

7Шаул сказал им:

– Слушайте, вениамитяне! Разве сын Есея даст вам всем поля и виноградники? Разве он сделает всех вас тысячниками и сотниками? 8Неужели поэтому вы все сговорились против меня? Никто не открыл мне, когда мой сын заключил дружеский союз с сыном Есея. Никто из вас не пожалел меня и не открыл мне, что мой сын настроил против меня моего слугу, чтобы тот устроил мне засаду, как он и делает сегодня.

9Но эдомитянин Доэг, который стоял вместе с приближёнными Шаула, сказал:

– Я видел, как сын Есея приходил к Ахи-Малику, сыну Ахитува, в город Нов. 10Ахи-Малик спрашивал для него Вечного. Ещё он снабдил его продовольствием и дал ему меч филистимлянина Голиафа.

11Тогда царь послал за священнослужителем Ахи-Маликом, сыном Ахитува, и за всей семьёй его отца, члены которой были священнослужителями в Нове, и все они пришли к царю. 12Шаул сказал:

– Послушай-ка, сын Ахитува.

– Да, мой господин, – ответил тот.

13Шаул сказал ему:

– Почему вы сговорились против меня, ты и сын Есея?! Ты дал ему хлеб и меч, спрашивал для него Всевышнего, чтобы он восстал против меня и устроил мне засаду, как он и делает сегодня.

14Ахи-Малик ответил царю:

– Кто из всех твоих слуг так верен тебе, как Довуд, который и зять царя, и начальник над твоей стражей, и высоко почитаем в твоём доме? 15Разве в тот день я в первый раз спрашивал для него Всевышнего? Конечно нет! Пусть царь не винит ни меня, твоего раба, ни мою семью, ведь я совсем ничего не знаю об этом деле.

16Но царь сказал:

– Ты непременно умрёшь, Ахи-Малик, ты и вся семья твоего отца.

17И царь приказал страже, которая стояла при нём:

– Ступайте и убейте священнослужителей Вечного, потому что они также примкнули к Довуду. Они знали, что он сбежал, а мне не открыли.

Но слуги царя не хотели поднять руку на священнослужителей Вечного. 18Тогда царь приказал Доэгу:

– Ты ступай и умертви священнослужителей.

И эдомитянин Доэг пошёл и умертвил их. В тот день он убил восемьдесят пять человек, которые носили льняной ефод. 19Затем он предал мечу Нов, город священнослужителей, вместе со всеми его мужчинами и женщинами, детьми и младенцами, волами, ослами и овцами.

20Но один из сыновей Ахи-Малика, сына Ахитува, по имени Авиатар, спасся и бежал к Довуду. 21Он рассказал Довуду, что Шаул убил священнослужителей Вечного. 22И Довуд сказал Авиатару:

– Когда там был эдомитянин Доэг, я знал, что он непременно расскажет Шаулу. Я в ответе за гибель всей семьи твоего отца. 23Оставайся со мной, не бойся, тот, кто охотится за твоей жизнью, охотится и за моей. У меня ты в безопасности.