1 Petro 4 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 4:1-19

Moyo Watsopano

1Popeza kuti Khristu anamva zowawa mʼthupi lake, mukhale nawonso mtima omwewo, chifukwa iye amene wamva zowawa mʼthupi lake walekana nawo uchimo. 2Chifukwa cha ichi, iwo sakhalanso moyo wawo akuchita zofuna za matupi awo, koma amachita chifuniro cha Mulungu. 3Pakuti mwataya kale nthawi yambiri mʼmbuyomu pochita zimene anthu osapembedza amachita, moyo wokhumba zonyansa, zilakolako zoyipa kuledzera, zochitika zoyipa za pa phwando, mapokoso ndi kupembedza mafano onyansa. 4Anthu osapembedza amadabwa pamene simuthamangira nawo kuchita zoyipitsitsazi, nʼchifukwa chake amakuchitani chipongwe. 5Koma adzafotokoza okha mlandu wawo kwa Mulungu amene wakonzeka kuweruza amoyo ndi akufa. 6Pa chifukwa chimenechi, Uthenga Wabwino unalalikidwa ngakhale kwa iwo amene tsopano ndi akufa, kuti adzaweruzidwe monga anthu ku thupi, koma adzakhale ndi moyo monga mwa Mulungu mu mzimu.

7Chimaliziro cha zinthu zonse chili pafupi. Choncho khalani maso ndi odziletsa kuti muthe kupemphera. 8Koposa zonse muzikondana wina ndi mnzake kwambiri, chifukwa chikondi chimaphimba machimo ambiri. 9Muzisamalirana wina ndi mnzake osamanyinyirika. 10Aliyense agwiritse ntchito mokhulupirika mphatso iliyonse imene anayilandira potumikira ena ngati adindo ogwiritsa bwino ntchito mphatso za Mulungu za mitundumitundu. 11Ngati wina ayankhula, ayankhuledi mawu enieni a Mulungu. Ngati wina atumikira, atumikire ndi mphamvu imene Mulungu amapereka, kuti pa zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu mpaka muyaya, Ameni.

Kumva Zowawa Chifukwa cha Chikhristu

12Abale okondedwa musadabwe ndi mayesero owawa amene mukukumana nawo ngati kuti china chake chachilendo chakuchitikirani. 13Koma kondwerani popeza mukumva zowawa pamodzi ndi Khristu, kuti mudzakondwere kwakukulu pamene ulemerero wake udzaonekera. 14Ngati akuchitani chipongwe chifukwa cha dzina la Khristu, ndinu odala, ndiye kuti Mzimu waulemerero wa Mulungu uli pa inu. 15Ngati mumva zowawa, zisakhale chifukwa cha kupha munthu, kapena kuba, kapena kuchita choyipa, kapena kulowerera za anthu ena, 16koma ngati mumva zowawa chifukwa ndinu Mkhristu, musachite manyazi, koma muyamike Mulungu chifukwa cha dzinalo. 17Pakuti nthawi yafika kuti chiweruzo chiyambe mʼnyumba ya Mulungu, ndipo ngati chiyamba ndi ife nanga podzafika kwa osamvera Uthenga Wabwino wa Mulungu, chidzakhala chotani? 18Monga Malemba akuti,

“Ngati kuli kovuta kuti olungama apulumuke,

nanga munthu wochimwa, wosasamala za Mulungu adzatani?”

19Nʼchifukwa chake, iwo amene akumva zowawa monga mwa chifuniro cha Mulungu, adzipereke okha mʼmanja mwa Mlengi wawo wokhulupirika ndi kumapitiriza kuchita zabwino.

New Russian Translation

1 Петра 4:1-19

Жизнь для Бога

1Итак, поскольку Христос пострадал телом, то и вы вооружитесь той же мыслью, ведь тот, кто страдал телесно, перестал грешить, 2чтобы остаток земной жизни прожить, руководствуясь уже не человеческими желаниями, а Божьей волей. 3Вы достаточно долго вели образ жизни, какой ведут язычники, предаваясь распутству, страстям, пьянству, обжорству, оргиям и отвратительному идолопоклонству. 4Поэтому язычники и удивляются, что вы больше не участвуете с ними в их распутстве, и злословят вас. 5Но они ответят за все перед Тем, Кто готов судить живых и мертвых. 6Поэтому Радостная Весть была возвещена и мертвым4:6 Мертвым – существует несколько толкований, например: 1) речь здесь идет о духовно мертвых (см. Эф. 2:1); 2) это ныне мертвые, которые при жизни успели услышать Радостную Весть и поверили в нее., чтобы они, как и все люди, были телесно осуждены, но жили в духе, подобно тому, как живет Бог.

7Скоро придет всему конец. Поэтому сохраняйте благоразумие, будьте бдительны, чтобы всегда быть в состоянии молиться. 8Прежде всего, преданно любите друг друга, потому что любовь покрывает множество грехов4:8 См. Прит. 10:12.. 9Будьте гостеприимны друг к другу без жалоб. 10Служите друг другу тем даром, какой каждый получил, верно распоряжаясь различными дарами благодати Божьей. 11Тот, кто говорит, должен делать это как произносящий Божьи слова. Кто служит, пусть служит с силой, которую дает Бог. Пусть во всем этом будет прославлен Бог через Иисуса Христа. Ему да будет слава и сила во веки веков, аминь.

Страдания за веру

12Возлюбленные, не удивляйтесь тому, что вам приходится проходить через огненные испытания, в этом нет ничего странного. 13Наоборот, радуйтесь тому, что вы тоже участвуете в страданиях Христа, чтобы вам радоваться и веселиться и тогда, когда откроется Его слава. 14Если вас оскорбляют за имя Христа, то вы блаженны, это значит, что Дух славы – Дух Божий – покоится на вас. 15Главное, чтобы никто из вас не страдал как убийца, или вор, или злодей, или как человек, вмешивающийся в чужие дела. 16Если же кто-то страдает потому, что он христианин, то пусть он не стыдится, а прославляет Бога за то, что носит это имя. 17Время суда настало, и суд начнется с Божьего дома. Подумайте, если он начнется с нас, то какая участь постигнет тех, кто не повинуется Божьей Радостной Вести?

18«Если праведнику нелегко получить спасение,

так что же станет с безбожниками и грешниками?»4:18 См. Прит. 11:31 в греческом переводе Ветхого Завета.

19Поэтому те, кто страдает по Божьей воле, пусть отдадут свою жизнь в руки Создателя, Который верен, и продолжают делать добро.